Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
BUKU LOYAMBA
Masalimo 1–41
1 Wodala munthu
amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,
kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,
kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
2 Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova
ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
3 Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,
umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake
ndipo masamba ake safota.
Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
4 Sizitero ndi anthu oyipa!
Iwo ali ngati mungu
umene umawuluzidwa ndi mphepo.
5 Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,
kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
6 Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,
koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.
18 Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa,
zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
19 Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga;
mmene iyendera njoka pa thanthwe;
mmene chiyendera chombo pa nyanja;
ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
20 Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo:
Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake
iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
21 Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi,
pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
22 Kapolo amene wasanduka mfumu,
chitsiru chimene chakhuta,
23 mkazi wonyozeka akakwatiwa
ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
24 Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi,
komatu ndi zochenjera kwambiri:
25 Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu,
komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
26 mbira zili ngati anthu opanda mphamvu
komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
27 dzombe lilibe mfumu,
komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
28 Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja
komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
29 “Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya,
pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
30 Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse,
ndipo suthawa kanthu kalikonse.
31 Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna,
ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
32 “Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha,
kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa,
ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
33 Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa,
ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka,
ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”
Aisraeli Onse Adzapulumuka
25 Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa za chinsinsi ichi, kuti mungadziyese nokha anzeru. Kuwuma mtima kumene Aisraeli akuchita ndi kwa kanthawi kufikira chiwerengero cha a mitundu chitalowa. 26 Kotero tsono Aisraeli onse adzapulumuka, monga kwalembedwa kuti,
“Mpulumutsi adzachokera ku Ziyoni;
Iye adzachotsa zoyipa zonse za Yakobo.
27 Ndipo ili lidzakhala pangano langa ndi iwo
pamene Ine ndidzachotsa machimo awo.”
28 Chifukwa cha Uthenga Wabwino, Aisraeli asanduka adani a Mulungu kuti inu mupindule. Koma kunena za kusankhidwa, iwo ndi okondedwa ndi Mulungu chifukwa cha makolo awo aja. 29 Pakuti Mulungu akayitana munthu ndi kumupatsa mphatso sangasinthenso. 30 Monga mmene inu munalili, osamvera Mulungu pa nthawi ina, tsopano mwalandira chifundo chifukwa cha kusamvera kwawo. 31 Chonchonso iwo akhala osamvera tsopano kuti iwonso alandire chifundo chifukwa cha chifundo cha Mulungu kwa inu. 32 Pakuti Mulungu anasandutsa anthu onse a mʼndende ya kusamvera kuti Iye akaonetse chifundo kwa onse.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.