Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
19 Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu;
thambo limalalikira ntchito za manja ake.
2 Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri,
usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
3 Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse;
liwu lawo silimveka.
4 Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi,
mawuwo amafika mpaka
kumalekezero a dziko lapansi.
5 Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake,
ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
6 Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo
ndi kuzungulira mpaka mbali inanso;
palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
7 Lamulo la Yehova ndi langwiro,
kutsitsimutsa moyo.
Maumboni a Yehova ndi odalirika,
amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
8 Malangizo a Yehova ndi olungama,
amapereka chimwemwe mu mtima.
Malamulo a Yehova ndi onyezimira,
amapereka kuwala.
9 Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro,
chimakhala mpaka muyaya.
Maweruzo a Yehova ndi owona
ndipo onse ndi olungama;
10 ndi a mtengowapatali kuposa golide,
kuposa golide weniweni;
ndi otsekemera kuposa uchi,
kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
11 Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo;
powasunga pali mphotho yayikulu.
12 Ndani angathe kudziwa zolakwa zake?
Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
13 Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa;
iwo asandilamulire.
Kotero ndidzakhala wosalakwa,
wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
14 Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga
zikhale zokondweretsa pamaso panu,
Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.
21 Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova;
Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
2 Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo,
koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
3 Za chilungamo ndi zolondola
ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
4 Maso odzikuza ndi mtima wonyada,
zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
5 Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake;
koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
6 Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa
ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
7 Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga,
pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
8 Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota,
koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
9 Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba,
kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
10 Munthu woyipa amalakalaka zoyipa;
sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
11 Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru;
koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
12 Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova,
ndipo Iye adzawononga woyipayo.
13 Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira,
nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
14 Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo,
ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
15 Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala,
koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
16 Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru
adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
17 Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi,
ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
Amufunsa Yesu za Ulamuliro Wake
23 Yesu analowa mʼNyumba ya Mulungu, ndipo pamene ankaphunzitsa, akulu a ansembe ndi akuluakulu anabwera kwa Iye namufunsa kuti, “Muchita izi ndi ulamuliro wanji ndipo anakupatsani ndani ulamuliro umenewu?”
24 Yesu anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani funso limodzi, mukandiyankha, Inenso ndikukuwuzani ndi ulamuliro wa yani umene ndikuchitira izi. 25 Ubatizo wa Yohane unachokera kuti? Kumwamba kapena kwa anthu?”
Anakambirana pakati pawo ndipo anati, “Tikati, ‘Kuchokera kumwamba,’ Iye adzafunsa kuti, ‘Bwanji simunakhulupirire?’ 26 Koma tikati, ‘Kuchokera kwa anthu,’ ife tikuopa anthuwa, pakuti onse amakhulupirira kuti Yohane anali mneneri.”
27 Choncho anamuwuza Yesu kuti, “Sitikudziwa.”
Pamenepo Iye anati, “Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wa yani umene ndichitira izi.”
Fanizo la Ana Amuna Awiri
28 “Kodi muganiza bwanji? Panali munthu wina anali ndi ana aamuna awiri. Anapita kwa woyamba nati, ‘Mwanawe pita kagwire ntchito lero mʼmunda wamphesa.’
29 “Iye anayankha kuti, ‘Sindipita,’ koma pambuyo pake anasintha maganizo napita.
30 “Kenaka abambowo anapita kwa mwana winayo nanena chimodzimodzi. Iye anayankha kuti, ‘Ndipita abambo,’ koma sanapite.
31 “Ndani wa awiriwa anachita chimene abambo ake amafuna?”
Anamuyankha nati, “Woyambayo.”
Yesu anawawuza kuti, “Ndikuwuzani zoonadi, kuti amisonkho ndi adama akulowa mu ufumu wa Mulungu inu musanalowemo.” 32 Pakuti Yohane anabwera kwa inu kuti akuonetseni njira yachilungamo, koma inu simunakhulupirire iye, koma amisonkho ndi adama anamukhulupirira. Koma ngakhale munaona izi, simunatembenuke mtima ndi kumukhulupirira iye.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.