Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
125 Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni,
limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
2 Monga mapiri azungulira Yerusalemu,
momwemonso Yehova azungulira anthu ake
kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala
pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama,
kuti anthu olungamawo
angachite nawonso zoyipa.
4 Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino,
amene ndi olungama mtima
5 Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota,
Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa.
Mtendere ukhale pa Israeli.
10 Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena,
ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru.
Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana;
ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi.
Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Usayende mʼnjira za anthu oyipa
kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo;
uzilambalala nʼkumangopita.
16 Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa;
tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi
ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha
kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani;
iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena;
tchera khutu ku mawu anga.
21 Usayiwale malangizo angawa,
koma uwasunge mu mtima mwako.
22 Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza
ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu
pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota;
ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Maso ako ayangʼane patsogolo;
uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako
ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Usapatukire kumanja kapena kumanzere;
usapite kumene kuli zoyipa.
12 Onse amene amachimwa osadziwa Malamulo, adzawonongeka ngakhale kuti sadziwa Malamulowo. Ndipo onse amene amachimwa akudziwa Malamulo adzaweruzidwa potsata Malamulowo. 13 Pakuti si amene amangomva Malamulo amene amakhala wolungama pamaso pa Mulungu, koma ndi okhawo amene amachita zili mʼMalamulomo amene adzatchedwa olungama. 14 Ndithu, pamene a mitundu ina, amene alibe Malamulo, koma mwachikhalidwe chawo amachita zimene zili mʼMalamulo, iwowo ndi Malamulo pa iwo okha, ngakhale kuti alibe Malamulowo. 15 Ntchito zawo zimaonetsa kuti Malamulowo alembedwa mʼmitima mwawo. Chikumbumtima chawonso chimawachitira umboni pakuti maganizo awo amawatsutsa kapena kuwavomereza. 16 Izi zidzachitika pa tsiku limene Mulungu adzaweruza zinsinsi za anthu kudzera mwa Yesu Khristu, monga momwe Uthenga wanga Wabwino unenera.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.