Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
12 Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama
ndipo amawakukutira mano;
13 koma Ambuye amaseka oyipa
pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
14 Oyipa amasolola lupanga
ndi kupinda uta
kugwetsa osauka ndi osowa,
kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe,
ndipo mauta awo anathyoka.
16 Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo
ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka,
koma Yehova amasunga olungama.
18 Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova,
ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
19 Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota;
mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
20 Koma oyipa adzawonongeka;
adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo,
iwo adzazimirira ngati utsi.
21 Oyipa amabwereka ndipo sabweza
koma olungama amapereka mowolowamanja.
22 Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko,
koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
Kumwalira kwa Solomoni
29 Tsono ntchito zina zonse za Solomoni, kuyambira pachiyambi mpaka kumaliza, kodi sizinalembedwa mʼbuku la mbiri la mneneri Natani, ndi mʼbuku la uneneri wa Ahiya wa ku Silo ndi mʼbuku la masomphenya a mlosi Ido, lokamba za Yeroboamu mwana wa Nebati? 30 Solomoni analamulira Aisraeli onse ku Yerusalemu zaka makumi anayi. 31 Ndipo anamwalira nagona ndi makolo ake. Anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Rehobowamu, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.
35 Pa nthawi iyi nʼkuti dzuwa litapendeka, ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kuthengo, ndipo ano ndi madzulo. 36 Awuzeni anthuwa azipita ku midzi ndi madera ozungulira, kuti akadzigulire kanthu kakuti adye.”
37 Koma Iye anayankha kuti, “Apatseni kanthu koti adye.”
Iwo anati kwa Iye, “Apa pafunika ndalama za miyezi isanu ndi itatu zomwe munthu amalandira! Kodi tipite kukagwiritsa ntchito ndalama zotere kugulira buledi kuti tiwapatse adye?”
38 Iye anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati? Pitani mukaone.”
Ataona anati kwa Iye, “Asanu ndi nsomba ziwiri.”
39 Pamenepo Yesu anawalamulira kuti awakhazike anthu pansi mʼmagulu pa msipu obiriwira. 40 Ndipo anakhala pansi mʼmagulu a anthu 100 ndi gulu la anthu makumi asanu. 41 Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri, nayangʼana kumwamba, Iye anayamika nagawa malofu a bulediwo. Kenaka anawapatsa ophunzira ake kuti awapatse anthu. Ndipo anagawanso nsomba ziwirizo kwa onse. 42 Onse anadya ndipo anakhuta, 43 ndipo ophunzira ake anatola buledi ndi nsomba zotsalira zokwanira madengu khumi ndi awiri. 44 Chiwerengero cha amuna amene anadya chinali 5,000.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.