Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Davide Amva za Imfa ya Sauli
1 Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
Davide Alira Maliro a Sauli ndi Yonatani
17 Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani. 18 Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
19 “Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda.
Taonani amphamvu agwa kumeneko!
20 “Musakanene zimenezi ku Gati,
musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni,
kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale,
ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
21 “Inu mapiri a ku Gilibowa,
musakhalenso ndi mame kapena mvula,
kapena minda yobereka zopereka za ufa.
Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa,
chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
22 “Pa magazi a ophedwa,
pa mnofu wa amphamvu,
uta wa Yonatani sunabwerere,
lupanga la Sauli silinabwere chabe.
23 “Sauli ndi Yonatani,
pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima,
ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe.
Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga,
anali ndi mphamvu zoposa mkango.
24 “Inu ana aakazi a Israeli,
mulireni Sauli,
amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa,
amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
25 “Taonani amphamvu agwa ku nkhondo!
Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
26 Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani,
unali wokondedwa kwambiri kwa ine.
Chikondi chako pa ine chinali chopambana,
chopambana kuposa chikondi cha akazi.
27 “Taonani amphamvu agwa!
Zida zankhondo zawonongeka!”
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
130 Ndikulirira kwa Inu Yehova ndili mʼdzenje lozama;
2 Ambuye imvani mawu anga.
Makutu anu akhale tcheru kumva
kupempha chifundo kwanga.
3 Inu Yehova, mukanamawerengera machimo,
Inu Yehova, akanayima chilili ndani wopanda mlandu?
4 Koma kwa Inu kuli chikhululukiro;
nʼchifukwa chake mumaopedwa.
5 Ndimayembekezera Yehova, moyo wanga umayembekezera,
ndipo ndimakhulupirira mawu ake.
6 Moyo wanga umayembekezera Ambuye,
kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa,
inde, kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa,
7 Yembekeza Yehova, iwe Israeli,
pakuti Yehova ali ndi chikondi chosasinthika
ndipo alinso ndi chipulumutso chochuluka.
8 Iye mwini adzawombola Israeli
ku machimo ake onse.
7 Popeza pa zinthu zonse munachita bwino, monga pachikhulupiriro, poyankhula, pachidziwitso, pakhama lambiri ndi pachikondi chanu pa ife, onetsetsani kuti muchitenso bwino pachisomo ichi chopereka.
8 Sindikukulamulirani, koma ndikufuna kuona ngati chikondi chanu nʼchoona pofananitsa ndi changu cha anthu ena. 9 Pakuti mukudziwa chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, kuti ngakhale anali wolemera, koma chifukwa cha inuyo anasanduka wosauka, kuti umphawi wakewo, inuyo mulemere.
10 Ndipo nawa malangizo anga pa zoyenera inu kuchita pa nkhaniyi. Chaka chatha munali oyamba, osati ongofuna kupereka kokha komanso okhala ndi mtima ofuna kupereka. 11 Tsopano tsirizani ntchitoyi, ndipo changu chanu chofunitsitsa kugwira ntchitoyi ndi kuyitsiriza chichitike molingana ndi zimene muli nazo. 12 Ndipo ngati mtima ofunitsitsa ulipo, mphatsoyo imalandiridwa molingana ndi zimene munthuyo ali nazo, osati zimene alibe.
13 Cholinga chathu sikuti tipeputse ena pamene inuyo mukuvutika, koma kuti pakhale kufanana. 14 Zambiri zimene muli nazo pakati panu muthandize nazo osowa, kuti nawonso akadzakhala nazo zambiri adzakuthandizeni pa zosowa zanu. Cholinga nʼkuchita mofanana, 15 monga kwalembedwa kuti, “Iye amene anatola zambiri sizinamutsalireko ndipo amene anatola pangʼono sizinamuchepere.”
Mtsikana Womwalira ndi Mayi Wodwala
21 Yesu atawolokeranso pa bwato kupita mbali ina ya nyanja, gulu lalikulu la anthu linasonkhana momuzungulira. Ali mʼmbali mwa nyanja, 22 mmodzi wa akulu a mʼsunagoge, dzina lake Yairo anafika pamenepo. Ataona Yesu, anagwa pa mapazi ake, 23 ndi kumudandaulira kwambiri nati, “Mwana wanga wamkazi wamngʼono ali pafupi kufa. Chonde tiyeni kuti mukamusanjike manja kuti akachiritsidwe nakhala ndi moyo.” 24 Ndipo Yesu anapita naye.
Gulu lalikulu la anthu linamutsata ndi kumamupanikiza Iye. 25 Pomwepo panali mayi amene amadwala nthenda yotaya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri. 26 Iye anavutika kwambiri pamene asingʼanga ambiri ankamusamalira ndipo anagwiritsa ntchito zonse anali nazo, koma mʼmalo mochira, nthenda yake inkakulakulabe. 27 Atamva za Yesu, anabwera kumbuyo kwake mʼgulu la anthu ndipo anakhudza mkanjo wake, 28 chifukwa anaganiza kuti, “Ngati nditangokhudza mkanjo wake, ndidzachiritsidwa.” 29 Nthawi yomweyo magazi ake analeka kutuluka ndipo anamva mʼthupi mwake kuti wamasulidwa ku vuto lake.
30 Pomwepo Yesu anazindikira kuti mphamvu inachoka mʼthupi mwake. Anatembenuka mʼgulu la anthu ndipo anafunsa kuti, “Ndani wakhudza zovala zanga?”
31 Ophunzira ake anayankha kuti, “Mukuona kuti anthu akukupanikizani, ndipo Inu mukufunsa kuti, ‘Ndani wandikhudza?’ ”
32 Koma Yesu anapitirizabe kuyangʼana kuti aone amene anachita zimenezi. 33 Kenaka mayi uja pozindikira chimene chinamuchitikira, anabwera ndi kugwa pa mapazi ake, ndipo akunjenjemera ndi mantha, anamuwuza zoona zokhazokha. 34 Anati kwa iye, “Mwana wamkazi, chikhulupiriro chako chakuchiritsa. Pita mu mtendere ndipo khala womasulidwa ku mavuto ako.”
35 Pamene Yesu ankayankhulabe, amuna ena anafika kuchokera ku nyumba ya Yairo, mkulu wa sunagoge. Iwo anati, “Mwana wanu wamkazi wamwalira, muvutitsiranjinso aphunzitsiwa?”
36 Posasamala zomwe ananena, Yesu anamuwuza mkulu wa sunagoge uja kuti, “Usachite mantha; ingokhulupirira.”
37 Iye sanalole munthu wina aliyense kuti amutsatire koma Petro, Yakobo ndi Yohane mʼbale wa Yakobo. 38 Atafika ku nyumba ya mkulu wa sunagoge, Yesu anaona chipiringu cha anthu akulira ndi kufuwula kwambiri. 39 Analowa nati kwa iwo, “Mukuchita phokoso ndi kulira chifukwa chiyani? Mwanayu sanamwalire koma ali mtulo.” 40 Koma anamuseka Iye.
Atawatulutsa onse panja, Iye anatenga abambo ndi amayi ake a mwanayo ndi ophunzira omwe anali naye, ndipo analowa mʼmene munali mwanayo. 41 Anagwira dzanja lake nanena kwa iye, “Talita Kumi!” (Kutanthauza kuti, “Mtsikana, ndikunena ndi iwe, imirira!”) 42 Nthawi yomweyo anayimirira nayenda mozungulira (anali wa zaka khumi ndi ziwiri). Pa ichi onse anadabwa kwambiri. 43 Anawalamulira kwambiri kuti asawuze wina aliyense za ichi, ndipo anawawuza kuti amupatse kanthu koti adye.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.