Beginning
Yehova Alonjeza Kudalitsa Yerusalemu
8 Awa ndi mawu amene Yehova Wamphamvuzonse ananena. 2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikuchitira nsanje yayikulu Ziyoni. Mtima wanga ukupweteka chifukwa cha nsanje pa iyeyo.”
3 Yehova akuti, “Ndidzabwerera ku Ziyoni ndi kukakhala ku Yerusalemu. Pamenepo Yerusalemu adzatchedwa Mzinda wa Choonadi ndipo phiri la Yehova Wamphamvuzonse lidzatchedwa Phiri Lopatulika.”
4 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Abambo ndi amayi okalamba adzakhalanso mʼmisewu ya mu Yerusalemu, aliyense ali ndi ndodo mʼmanja mwake chifukwa cha kuchuluka kwa masiku ake. 5 Ndipo misewu ya mu mzindamo idzadzaza ndi anyamata ndi atsikana akusewera.”
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati zikuoneka kuti nʼzosatheka kwa anthu otsala pa nthawi ino, kodi zidzakhala zosathekanso kwa Ine?” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
7 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani ndidzapulumutsa anthu anga kuchokera ku mayiko a kummawa ndi kumadzulo. 8 Ndidzawabweretsa kuti adzakhale mu Yerusalemu; adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, wokhulupirika ndi wolungama pakati pawo.”
9 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Inu amene tsopano mukumva mawu awa amene akuyankhula aneneri amene analipo pamene ankayika maziko a nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, ‘limbani mtima kuti mumange Nyumba ya Yehova.’ 10 Mpaka nthawi imeneyi panalibe munthu wolandira malipiro pa ntchito kapena ndalama zolipirira nyama zogwira ntchito. Panalibe munthu amene ankadzigwirira ntchito mwamtendere chifukwa choopa adani ake, pakuti Ine ndinkawayambanitsa. 11 Koma tsopano sindidzachitira otsala mwa anthu awa zomwe ndinachita kale,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
12 “Pakuti mbewu zidzamera bwino, mpesa udzabala zipatso zake, nthaka idzatulutsa zomera zake, ndi thambo lidzagwetsa mame. Ndidzapereka zonse kukhala cholowa cha otsala mwa anthu awa. 13 Monga mwakhala muli chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu ina ya anthu, inu Yuda ndi Israeli, choncho ndidzakupulumutsani, ndipo mudzakhala dalitso. Musachite mantha, koma limbani mtima.”
14 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Monga ndinatsimikiza mtima kubweretsa choyipa pa inu, komanso osakuchitirani chisoni pamene makolo anu anandikwiyitsa,” akutero Yehova, 15 “Choncho tsopano ndatsimikiza mtima kuchitiranso zabwino Yerusalemu ndi Yuda. Musachite mantha. 16 Zinthu zoti muchite ndi izi: Muziwuzana zoona zokhazokha, muziweruza moona ndi mwachilungamo mʼmabwalo anu; 17 musamachitire mnzanu chiwembu, musamakonde kulumbira zonama. Zonsezi Ine ndimadana nazo,” akutero Yehova.
18 Yehova Wamphamvuzonse anayankhulanso nane. 19 Ndipo ananena kuti, “Kusala zakudya kwa pa mwezi wachinayi, chisanu, chisanu ndi chiwiri ndi wakhumi, kudzakhala nthawi yachimwemwe, ya chisangalalo ndi nthawi ya madyerero chikondwerero kwa Yuda. Nʼchifukwa chake muzikonda choonadi ndi mtendere.”
20 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a mitundu yambiri ndi anthu okhala mʼmizinda yambiri adzabwerabe, 21 ndipo nzika za mzinda wina zidzapita ku mzinda wina, kukanena kuti, ‘Tiyeni mwamsanga tikapemphe madalitso kwa Yehova ndi kukapembedza Yehova Wamphamvuzonse. Inenso ndikupita kumeneko.’ 22 Anthu ambiri ndiponso a ku mayiko amphamvu adzabwera ku Yerusalemu kudzapembedza Yehova Wamphamvuzonse ndi kudzapempha madalitso.”
23 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Masiku amenewo anthu khumi ochokera ku mitundu ya anthu a ziyankhulo zosiyana adzagwira mkanjo wa Myuda ndi kunena kuti, ‘Tipite nawo, chifukwa tamva kuti Mulungu ali nanu.’ ”
Chiweruzo pa Adani a Israeli
Ulosi
9 Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki
ndi mzinda wa Damasiko
pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli
ali pa Yehova—
2 ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli,
komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
3 Ndipo Turo anadzimangira linga;
wadziwunjikira siliva ngati fumbi,
ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
4 Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho
ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja,
ndipo adzapserera ndi moto.
5 Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha;
Gaza adzanjenjemera ndi ululu,
chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu.
Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa
ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
6 Mu Asidodi mudzakhala mlendo,
ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
7 Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo,
chakudya choletsedwa mʼmano mwawo.
Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu,
adzasanduka atsogoleri mu Yuda,
ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
8 Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga
ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza.
Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga,
pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.
Kubwera kwa Mfumu ya Ziyoni
9 Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni!
Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu!
Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe,
yolungama ndi yogonjetsa adani,
yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu,
pa mwana wamphongo wa bulu.
10 Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu
ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu,
ndipo uta wankhondo udzathyoka.
Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu.
Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina,
ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
11 Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine,
ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
12 Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo;
ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
13 Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga,
ndipo Efereimu ndiye muvi wake.
Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni,
kulimbana ndi ana ako iwe Grisi,
ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.
Kuoneka kwa Yehova
14 Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake;
mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani.
Ambuye Yehova adzaliza lipenga;
ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
15 ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza.
Iwo adzawononga
ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni.
Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo;
magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi
pa ngodya za guwa lansembe.
16 Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa
pakuti anthu ake ali ngati nkhosa.
Adzanyezimira mʼdziko lake
ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
17 Taonani chikoka ndi kukongola kwawo!
Tirigu adzasangalatsa anyamata,
ndi vinyo watsopano anamwali.
Yehova Adzasamalira Yuda
10 Pemphani mvula kwa Yehova pa nthawi yamphukira;
ndi Yehova amene amapanga mitambo ya mvula.
Iye amagwetsa mivumbi ya mvula kwa anthu,
ndi kumeretsa mbewu za mʼmunda kwa aliyense.
2 Mafano amayankhula zachinyengo,
owombeza mawula amaona masomphenya abodza;
amafotokoza maloto onama,
amapereka chitonthozo chopandapake.
Choncho anthu amangoyendayenda ngati nkhosa zozunzika
chifukwa chosowa mʼbusa.
3 “Ine ndawakwiyira kwambiri abusa,
ndipo ndidzalanga atsogoleri;
pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzasamalira
nkhosa zake, nyumba ya Yuda,
ndi kuwasandutsa ngati akavalo aulemerero ankhondo.
4 Mu Yuda mudzachokera mwala wapangodya,
mudzachokera chikhomo cha tenti,
mudzachokera uta wankhondo,
mudzachokera mtsogoleri aliyense.
5 Onse pamodzi adzakhala ngati ngwazi zankhondo
zoponda mʼmatope a mʼmisewu nthawi yankhondo.
Chifukwa Yehova adzakhala nawo,
adzachita nkhondo ndi kugonjetsa okwera pa akavalo.
6 “Ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda
ndi kupulumutsa nyumba ya Yosefe.
Ndidzawabwezeretsa
chifukwa ndawamvera chisoni.
Adzakhala ngati kuti
sindinawakane,
chifukwa ndine Yehova Mulungu wawo
ndipo ndidzawayankha.
7 Aefereimu adzakhala ngati ankhondo amphamvu
adzasangalala ngati anthu amene amwa vinyo.
Ana awo adzaziona zimenezi ndipo adzasangalala;
mʼmitima mwawo adzakondwa mwa Ambuye.
8 Ndidzaliza mluzu
ndi kuwasonkhanitsa pamodzi.
Ndithu ndawawombola;
adzachulukana ngati poyamba paja.
9 Ndinawamwaza pakati pa mitundu ina ya anthu,
koma ku mayiko akutaliwo adzandikumbukira.
Iwo pamodzi ndi ana awo adzapulumuka,
ndipo adzabwerera.
10 Ndidzawabweretsa kuchokera ku Igupto
ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku Asiriya.
Ndidzawabwezera ku Giliyadi ndi ku Lebanoni,
mpaka malo woti nʼkukhalamo adzatheratu.
11 Adzawoloka nyanja ya masautso;
nyanja yokokoma idzagonja
ndipo madzi onse a mu Nailo adzaphwa.
Kudzikuza kwa Asiriya kudzatha
ndipo ndodo yaufumu ya Igupto idzathyoka.
12 Ndidzalimbitsa iwo mwa Yehova
ndipo adzayenda mʼdzina lake,”
akutero Yehova.
11 Tsekula zitseko zako, iwe Lebanoni,
kuti moto unyeketse mikungudza yako!
2 Lira mwachisoni, iwe mtengo wa payini, pakuti mkungudza wagwa;
mtengo wamphamvu wawonongeka!
Lirani mwachisoni, inu mitengo ya thundu ya Basani;
nkhalango yowirira yadulidwa!
3 Imvani kulira mwachisoni kwa abusa;
msipu wawo wobiriwira wawonongeka!
Imvani kubangula kwa mikango;
nkhalango yowirira ya ku Yorodani yawonongeka!
Abusa Awiri
4 Yehova Mulungu wanga akuti, “Dyetsa nkhosa zimene zikukaphedwa. 5 Amene amagula nkhosazo amazipha ndipo salangidwa. Amene amazigulitsa amanena kuti, ‘Alemekezeke Yehova, ine ndalemera!’ Abusa ake omwe sazimvera chisoni nkhosazo. 6 Pakuti Ine sindidzamveranso chisoni anthu okhala mʼdziko,” akutero Yehova. “Ndidzapereka munthu aliyense mʼmanja mwa mnansi wake ndi mwa mfumu yake. Iwo adzazunza dziko, ndipo Ine sindidzawapulumutsa mʼmanja mwawo.”
7 Choncho ine ndinadyetsa nkhosa zokaphedwa, makamaka nkhosa zoponderezedwa. Pamenepo ndinatenga ndodo ziwiri ndipo yoyamba ndinayitcha Kukoma mtima ndipo yachiwiri ndinayitcha Umodzi ndipo ndinadyetsa nkhosazo. 8 Pa mwezi umodzi ndinachotsa abusa atatu.
Abusawo anadana nane, ndipo ndinatopa nawo. 9 Ndinawuza gulu la nkhosalo kuti, “Sindidzakhalanso mʼbusa wanu. Imene ikufa, ife, ndipo imene ikuwonongeka, iwonongeke, zimene zatsala zizidyana.”
10 Kenaka ndinatenga ndodo yanga yotchedwa Kukoma mtima ndi kuyithyola, kuphwanya pangano limene ndinachita ndi mitundu yonse ya anthu. 11 Linaphwanyidwa tsiku limenelo ndipo nkhosa zosautsidwa zimene zimandiyangʼanitsitsa zinadziwa kuti anali mawu a Yehova.
12 Ndinawawuza kuti, “Ngati mukuganiza kuti zili bwino, patseni malipiro anga; koma ngati si choncho, sungani malipirowo.” Kotero anandipatsa ndalama zasiliva makumi atatu.
13 Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ziponye kwa wowumba mbiya,” mtengo woyenera umene anapereka pondigula Ine! Choncho ndinatenga ndalama zasiliva makumi atatu ndi kuziponya mʼnyumba ya Yehova kwa wowumba mbiya.
14 Kenaka ndinathyola ndodo yanga yachiwiri yotchedwa Umodzi, kuthetsa ubale pakati pa Yuda ndi Israeli.
15 Pamenepo Yehova anayankhula nane kuti, “Tenganso zida za mʼbusa wopusa. 16 Pakuti ndidzawutsa mʼbusa mʼdzikomo amene sadzasamalira zotayika, kapena kufunafuna zazingʼono, kapena zovulala, kapena kudyetsa nkhosa zabwino, koma iye adzadya nyama ya nkhosa zonenepa, nʼkumakukuta ndi ziboda zomwe.
17 “Tsoka kwa mʼbusa wopandapake,
amene amasiya nkhosa!
Lupanga limukanthe pa mkono wake ndi pa diso lake lakumanja!
Mkono wake ufote kotheratu,
diso lake lamanja lisaonenso.”
Kuphedwa kwa Adani a Yerusalemu
Ulosi
12 Uthenga wa Yehova kwa Israeli. Yehova, amene amayala mlengalenga, amene amayika maziko a dziko lapansi, ndiponso amene amalenga mzimu wokhala mwa munthu, akunena kuti, 2 “Taonani, ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala chakumwa choledzeretsa chimene chidzasokoneza mitundu yonse ya anthu yomuzungulira. Yuda adzazingidwa pamodzinso ndi Yerusalemu. 3 Pa tsiku limenelo, pamene mitundu yonse ya anthu a dziko lapansi idzasonkhana kulimbana naye, ndidzasandutsa Yerusalemu thanthwe losatheka kusunthidwa ndi mitundu yonse ya anthu. Onse oyesa kumusuntha adzadzipweteka. 4 Pa tsiku limenelo kavalo aliyense ndidzamuchititsa mantha kuti asokonezeke, ndipo wokwerapo wake ndidzamuchititsa misala,” akutero Yehova. “Ndidzayangʼanira nyumba ya Yuda koma ndidzachititsa khungu akavalo onse a anthu a mitundu ina. 5 Pamenepo atsogoleri a Yuda adzayankhula mʼmitima mwawo kuti, ‘Anthu a ku Yerusalemu ndi amphamvu, chifukwa Yehova Wamphamvuzonse ndiye Mulungu wawo.’
6 “Pa tsiku limenelo ndidzasandutsa atsogoleri a Yuda kukhala ngati mbawula yotentha pakati pa nkhuni, ngati sakali yoyaka pa mitolo ya tirigu. Adzatentha mitundu yonse ya anthu yowazungulira, kumanja ndi kumanzere, koma Yerusalemu sadzasuntha pa malo ake.
7 “Yehova adzapulumutsa malo okhala Yuda poyamba, kuti ulemu wa nyumba ya Davide ndi wa anthu okhala mu Yerusalemu usapambane ulemu wa Yuda. 8 Pa tsiku limenelo Yehova adzatchinjiriza onse okhala mu Yerusalemu, kotero kuti anthu ofowoka kwambiri pakati pawo adzakhala ngati Davide, ndipo nyumba ya Davide idzakhala ngati Mulungu, ngati mngelo wa Yehova wowatsogolera. 9 Pa tsiku limenelo ndidzawononga mitundu yonse yofuna kuthira nkhondo Yerusalemu.
Kulirira amene Anamulasa
10 “Ndipo pa nyumba ya Davide ndi pa anthu okhala mu Yerusalemu ndidzakhuthulirapo mzimu wachisomo ndi wopemphera. Iwo adzandiyangʼana Ine, amene anamubaya, ndipo adzamulirira kwambiri monga momwe munthu amalirira mwana wake mmodzi yekhayo, ndiponso adzamva chisoni kwambiri monga momwe amachitira ndi mwana woyamba kubadwa. 11 Pa tsiku limenelo mudzakhala kulira kwakukulu mu Yerusalemu, monga kulira kwa ku Hadadi-Rimoni ku chigwa cha Megido. 12 Dziko lidzalira kwambiri, fuko lililonse pa lokha, akazi awo pa okhanso: fuko la Davide pamodzi ndi akazi awo, fuko la Natani pamodzi ndi akazi awo, 13 nyumba ya Levi pamodzi ndi akazi awo, fuko la Simei pamodzi ndi akazi awo, 14 ndiponso mafuko onse pamodzi ndi akazi awo.
Kuyeretsedwa ku Tchimo
13 “Pa tsiku limenelo nyumba ya Davide adzayitsekulira kasupe wa madzi pamodzi ndi okhala mu Yerusalemu, kuti awachotsere tchimo lawo ndi chodetsa chawo.
2 “Pa tsiku limenelo, ndidzafafaniziratu mayina a mafano mʼdziko, ndipo sadzawakumbukiranso,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndidzachotsa mʼdziko aneneri pamodzi ndi mzimu wonyansa. 3 Ndipo ngati wina aliyense adzafuna kunenera, abambo ndi amayi ake amene anamubereka, adzamuwuza kuti, ‘Uyenera kufa, chifukwa wayankhula bodza mʼdzina la Yehova.’ Pamene anenera, makolo ake omwe adzamubaya.
4 “Pa tsiku limenelo mneneri aliyense adzachita manyazi chifukwa cha masomphenya ake. Sadzavala chovala chake chaubweya ndi cholinga chonamiza anthu. 5 Iye adzati, ‘Sindine mneneri. Ndine mlimi; ndakhala ndi kulima munda kuyambira ubwana wanga.’ 6 Ngati wina adzamufunsa, ‘Zilonda zili mʼthupi lakoli ndi chiyani?’ Iye adzayankha kuti, ‘Zilondazi ndinazilandira mʼnyumba ya abwenzi anga.’
Kukantha Mʼbusa, Nkhosa Kubalalika
7 “Dzambatuka iwe lupanga, ukanthe mʼbusa wanga,
ukanthe munthu amene ali pafupi ndi Ine!”
akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Kantha mʼbusa
ndipo nkhosa zidzabalalika,
ndipo ndidzatambalitsa dzanja langa kuwononga zazingʼono.
8 Mʼdziko monse, akutero Yehova Wamphamvuzonse,
“zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu za anthu zidzakanthidwa ndi kuwonongeka;
koma chigawo chimodzi chidzatsala mʼdzikomo.
9 Chigawo chachitatuchi ndidzachiyika pa moto;
ndidzawayeretsa monga momwe amayeretsera siliva
ndi kuwayesa monga momwe amayesera golide.
Adzayitana pa dzina langa
ndipo Ine ndidzawayankha;
Ine ndidzanena kuti, ‘Awa ndi anthu anga,’
ndipo iwo adzanena kuti, ‘Yehova ndiye Mulungu wathu.’ ”
Yehova Akubwera ndipo Akulamulira
14 Taonani tsiku la Yehova likubwera pamene zinthu zimene adani ako anakulanda azidzagawana iwe ukuona.
2 Ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse kuti adzathire nkhondo Yerusalemu; mzindawu udzalandidwa, nyumba zidzaphwasulidwa, ndipo akazi adzagwiriridwa. Theka la anthu a mu mzindamu lidzapita ku ukapolo, koma ena onse otsala mu mzindamu sadzachotsedwa.
3 Pamenepo Yehova adzabwera kudzamenyana ndi mitundu ya anthu imeneyi, ngati mmene amachitira pa nthawi ya nkhondo. 4 Tsiku limenelo adzayimirira pa Phiri la Olivi, kummawa kwa Yerusalemu, ndipo Phiri la Olivilo lidzagawikana pawiri kuyambira kummawa mpaka kumadzulo, kupanga chigwa chachikulu, kuchititsa kuti theka la phiri lisunthire kumpoto ndi linalo kummwera. 5 Inu mudzathawa podzera mʼchigwa chapakati pa phirilo, pakuti chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa monga munachitira pa tsiku la chivomerezi nthawi ya Uziya mfumu ya Yuda. Kenaka Yehova Mulungu wanga adzabwera, pamodzi ndi oyera ake onse.
6 Tsiku limenelo sipadzakhala kuwala, kuzizira kapena chisanu. 7 Lidzakhala tsiku lapaderadera, silidzakhala usana kapena usiku; tsiku limeneli akulidziwa ndi Yehova yekha. Ikadzafika nthawi ya madzulo, kudzakhala kukuwalabe.
8 Tsiku limenelo madzi amoyo adzatuluka mu Yerusalemu, theka lidzapita ku nyanja ya kummawa ndipo theka lina ku nyanja ya kumadzulo, nthawi yachilimwe ndi nthawi yozizira yomwe.
9 Ndipo Yehova adzakhala mfumu pa dziko lonse lapansi. Tsiku limenelo padzakhala Ambuye mmodzi yekha, ndipo dzina lidzakhala limodzi lomwelo.
10 Dziko lonse, kuyambira ku Geba mpaka ku Rimoni, kummwera kwa Yerusalemu, lidzakhala ngati Araba. Koma Yerusalemu adzakwezedwa ndipo adzakhala pamalo pakepo, kuyambira ku Chipata cha Benjamini mpaka ku malo amene ali ku Chipata Choyamba, ku Chipata Chapangodya, ndipo kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku malo opsinyira mphesa za mfumu. 11 Mʼmenemo mudzakhala anthu; sadzawonongedwanso. Yerusalemu adzakhala pa mtendere.
12 Mliri umene Yehova adzakanthire nawo mitundu yonse ya anthu imene inkamenyana ndi Yerusalemu ndi uwu: Matupi awo adzawola iwo eni akuyenda, maso awo adzawola ali mʼmalo mwake, ndipo malilime awo adzawola ali mʼkamwa mwawo. 13 Pa tsiku limenelo Yehova adzasokoneza anthu akuluakulu. Munthu aliyense adzagwira dzanja la mnzake, ndi kuyamba kumenyana okhaokha. 14 Yuda nayenso adzachita nkhondo ku Yerusalemu. Chuma chonse cha anthu a mitundu yozungulira adzachisonkhanitsa pamodzi; golide, siliva ndi zovala zochuluka kwambiri. 15 Mliri womwewo udzapha akavalo ndi nyulu, ngamira ndi abulu, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku misasako.
16 Kenaka opulumuka ochokera mwa mitundu yonse ya anthu amene anathira nkhondo Yerusalemu, azidzapita chaka ndi chaka kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, ndiponso kukachita Chikondwerero cha Misasa. 17 Ngati mitundu ina ya anthu pa dziko lapansi sidzapita ku Yerusalemu kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, idzakhala wopanda mvula. 18 Ndipo ngati anthu a ku Igupto sadzapita ndi kukakhala nawo kumeneko, adzakhala wopanda mvula. Yehova adzabweretsa pa iwo mliri umene analangira mitundu ina ya anthu imene sinapite ku Chikondwerero cha Misasa. 19 Chimenechi chidzakhala chilango cha Igupto ndiponso mitundu ina yonse imene sidzapita ku Chikondwerero cha Misasa.
20 Pa tsiku limenelo pa maberu a akavalo padzalembedwa mawu oti wopatulikira Yehova, ndipo miphika ya mʼNyumba ya Yehova idzakhala yopatulika ngati mbale za ku guwa. 21 Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.