Beginning
Israeli Akolola Kamvuluvulu
8 “Ika lipenga pakamwa pako.
Ngati chiwombankhanga, kutsutsana ndi nyumba ya Yehova
chifukwa anthu aphwanya pangano langa
ndiponso agalukira lamulo langa.
2 Israeli akulirira kwa Ine kuti,
‘Inu Mulungu wathu, ife timakudziwani!’
3 Koma Israeli wakana zabwino;
mdani adzamuthamangitsa.
4 Amalonga mafumu mosatsata kufuna kwanga.
Amasankha akalonga popanda chilolezo changa.
Amadzipangira mafano
asiliva ndi agolide
koma adzawonongeka nawo.
5 Iwe Samariya, taya fano lako la mwana wangʼombe!
Mkwiyo wanga wayakira anthuwo.
Padzapita nthawi yayitali chotani asanasinthike kukhala oyera mtima?
6 Mafanowa ndi ochokera ku Israeli!
Mwana wa ngʼombe uyu anapangidwa ndi munthu waluso;
si Mulungu amene anamupanga.
Adzaphwanyidwa nʼkukhala zidutswa,
mwana wangʼombe wa ku Samariya.
7 “Aisraeli amadzala mphepo
ndipo amakolola kamvuluvulu.
Tirigu alibe ngala;
sadzabala chakudya.
Akanabala chakudya
alendo akanadya chakudyacho.
8 Israeli wamezedwa,
tsopano ali pakati pa anthu a mitundu ina
ngati chinthu cha chabechabe.
9 Pakuti iwo anapita ku Asiriya
ngati mbidzi yongodziyendera pa yokha.
Efereimu wadzigulitsa kwa zibwenzi zake.
10 Ngakhale wadzigulitsa pakati pa mitundu ya anthu,
Ine ndidzawasonkhanitsa pamodzi.
Iwo adzayamba kuzunzika pansi pa
ulamuliro wankhanza wa mfumu yamphamvu.
11 “Ngakhale Efereimu anamanga maguwa ambiri a nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo,
maguwa amenewa akhala malo ochimwirapo.
12 Ndinawalembera zinthu zambiri za malamulo anga,
koma iwo anaziyesa ngati zinthu zachilendo.
13 Amapereka nsembe za nyama kwa Ine
ndipo iwo amadya nyamayo,
koma Yehova sakondwera nazo.
Tsopano Iye adzakumbukira zoyipa zawo
ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo:
iwowo adzabwerera ku Igupto.
14 Israeli wayiwala Mlengi wake
ndipo wamanga nyumba zaufumu;
Yuda wachulukitsa mizinda ya malinga.
Koma Ine ndidzaponya moto pa mizinda yawoyo,
moto umene udzatenthe malinga awo.”
Chilango cha Israeli
9 Iwe Israeli, usakondwere;
monga imachitira mitundu ina.
Pakuti wakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wako;
umakonda malipiro a chiwerewere
pa malo aliwonse opunthira tirigu.
2 Malo opunthira tirigu ndi malo opsinyira mphesa sadzadyetsa anthu;
adzasowa vinyo watsopano.
3 Sadzakhalanso mʼdziko la Yehova.
Efereimu adzabwerera ku Igupto
ndipo mudzadya chakudya chodetsedwa ku Asiriya.
4 Iwo sadzaperekanso chopereka cha chakumwa kwa Yehova,
kapena nsembe zawo kuti akondweretse Yehovayo.
Nsembe zotere zidzakhala kwa iwo ngati chakudya cha anamfedwa;
onse akudya chakudya chimenechi adzakhala odetsedwa.
Chakudya ichi chidzakhala chodya okha,
sichidzalowa mʼnyumba ya Yehova.
5 Kodi mudzachita chiyani pa tsiku la maphwando anu oyikika;
pa masiku a zikondwerero za Yehova?
6 Ngakhale iwo atathawa chiwonongeko,
Igupto adzawasonkhanitsa,
ndipo Mefisi adzawayika mʼmanda.
Khwisa adzamera pa ziwiya zawo zasiliva,
ndipo minga idzamera mʼmatenti awo.
7 Masiku achilango akubwera,
masiku obwezera ali pafupi.
Israeli adziwe zimenezi.
Chifukwa machimo anu ndi ochuluka kwambiri
ndipo udani wanu pa Mulungu ndi waukulu kwambiri.
Mneneri amamuyesa chitsiru,
munthu wanzeru za kwa Mulungu ngati wamisala.
8 Mneneri pamodzi ndi Mulungu wanga
ndiwo alonda a Efereimu,
koma mneneri amutchera misampha mʼnjira zake zonse,
ndipo udani ukumudikira mʼnyumba ya Mulungu wake.
9 Iwo azama mu zachinyengo
monga masiku a Gibeya.
Mulungu adzakumbukira zolakwa zawo
ndipo adzawalanga chifukwa cha machimo awo.
10 “Pamene ndinamupeza Israeli
zinali ngati kupeza mphesa mʼchipululu.
Nditaona makolo anu,
zinali ngati ndikuona nkhuyu zoyambirira kupsa.
Koma atafika ku Baala Peori,
anadzipereka ku fano lija lochititsa manyazi
ndipo anakhala onyansa ngati chinthu chimene anachikondacho.
11 Ulemerero wa Efereimu udzawuluka ngati mbalame.
Sipadzakhalanso kubereka ana, kuyembekezera kapena kutenga pathupi.
12 Ngakhale atalera ana
ndidzachititsa kuti mwana aliyense amwalire.
Tsoka kwa anthuwo
pamene Ine ndidzawafulatira!
13 Ndaona Efereimu ngati Turo,
atadzalidwa pa nthaka ya chonde.
Koma Efereimu adzatsogolera
ana ake kuti akaphedwe.”
14 Inu Yehova, muwapatse.
Kodi mudzawapatsa chiyani?
Apatseni mimba yomangopita padera
ndi mawere owuma.
15 “Chifukwa cha zoyipa zawo zonse ku Giligala,
Ine ndinawada kumeneko.
Chifukwa cha machitidwe awo auchimo,
ndidzawapirikitsa mʼnyumba yanga.
Sindidzawakondanso;
atsogoleri awo onse ndi owukira.
16 Efereimu wathedwa,
mizu yake yauma
sakubalanso zipatso.
Ngakhale atabereka ana,
Ine ndidzapha ana awo okondedwawo.”
17 Mulungu wanga adzawakana
chifukwa sanamumvere Iye;
adzakhala oyendayenda pakati pa anthu a mitundu ina.
10 Israeli anali mpesa wotambalala;
anabereka zipatso zambiri.
Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka,
anawonjezera kumanga maguwa ansembe.
Pamene dziko lake linkatukuka,
anakongoletsa miyala yake yopatulika.
2 Mtima wawo ndi wonyenga
ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo.
Yehova adzagumula maguwa awo ansembe
ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.
3 Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu
chifukwa sitinaope Yehova.
Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu,
kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”
4 Mafumu amalonjeza zambiri,
amalumbira zabodza
pochita mapangano.
Kotero maweruzo amaphuka
ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.
5 Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha
chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni.
Anthu ake adzalirira fanolo,
chimodzimodzinso ansembe ake adamawo,
amene anakondwera ndi kukongola kwake,
chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.
6 Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya
ngati mphatso kwa mfumu yayikulu.
Efereimu adzachititsidwa manyazi
chifukwa cha mafano ake amitengo.
7 Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali
ngati kanthambi koyenda pa madzi.
8 Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa.
Ili ndiye tchimo la Israeli.
Minga ndi mitungwi zidzamera
ndi kuphimba maguwa awo ansembe.
Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!”
ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”
9 “Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya,
ndipo wakhala uli pomwepo.
Kodi nkhondo sinagonjetse anthu
ochita zoyipa ku Gibeya?
10 Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo;
mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo,
kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.
11 Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa
amene amakonda kupuntha tirigu,
choncho Ine ndidzayika goli
mʼkhosi lake lokongolalo.
Ndidzasenzetsa Efereimu goli,
Yuda ayenera kulima,
ndipo Yakobo ayenera kutipula.
12 Mufese nokha chilungamo
ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika.
Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo;
pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova,
mpaka Iye atabwera
kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.
13 Koma inu munadzala zolakwa,
mwakolola zoyipa;
mwadya chipatso cha chinyengo.
Chifukwa mumadalira mphamvu zanu
ndiponso ankhondo anu ochulukawo,
14 phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga
kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka,
monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo;
pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.
15 Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli
chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu.
Tsiku limeneli likadzafika,
mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.
Chikondi cha Mulungu pa Israeli
11 “Israeli ali mwana, ndinamukonda,
ndipo ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.
2 Koma ndimati ndikamapitiriza kuyitana
iwo amandithawa kupita kutali.
Ankapereka nsembe kwa Abaala
ndipo ankafukiza lubani kwa mafano.
3 Ndi Ine amene ndinaphunzitsa Efereimu kuyenda,
ndipo ndinawagwira pa mkono;
koma iwo sanazindikire
kuti ndine amene ndinawachiritsa.
4 Ndinawatsogolera ndi zingwe zachifundo cha anthu
ndi zomangira za chikondi;
ndinachotsa goli mʼkhosi mwawo
ndipo ndinawerama nʼkuwadyetsa.
5 “Sadzabwerera ku Igupto,
koma Asiriya ndiye adzakhala mfumu yawo
pakuti akana kutembenuka.
6 Malupanga adzangʼanima mʼmizinda yawo,
ndipo adzawononga mipiringidzo ya zipata zawo
nadzathetseratu malingaliro awo.
7 Anthu anga atsimikiza zondifulatira Ine.
Ngakhale atayitana Wammwambamwamba,
sizidzatheka kuti Iye awakwezenso.
8 “Kodi ndingakusiye bwanji iwe Efereimu?
Kodi ndingakupereke bwanji iwe Israeli?
Kodi ndingakuchitire bwanji zimene ndinachitira Adima?
Kodi ndingathe bwanji kukuchitira zimene ndinachitira Zeboimu?
Mtima wanga wakana kutero;
chifundo changa chonse chikusefukira.
9 Sindidzalola kuti ndikulange ndi mkwiyo wanga woopsa,
kapena kutembenuka ndi kuwononga Efereimu.
Pakuti Ine ndine Mulungu osati munthu,
Woyerayo pakati panu.
Sindidzabwera mwaukali.
10 Iwo adzatsatira Yehova;
Iye adzabangula ngati mkango.
Akadzabangula,
ana ake adzabwera akunjenjemera kuchokera kumadzulo.
11 Adzabwera akunjenjemera
ngati mbalame kuchokera ku Igupto,
ngati nkhunda kuchokera ku Asiriya.
Ine ndidzawakhazikanso mʼnyumba zawo,”
akutero Yehova.
Tchimo la Israeli
12 Efereimu wandizungulira ndi mabodza,
nyumba ya Israeli yandizungulira ndi chinyengo.
Ndipo Yuda wawukira Mulungu,
wawukira ngakhale Woyerayo amene ndi wokhulupirika.
12 Efereimu amadya mpweya;
tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa
ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa.
Amachita mgwirizano ndi Asiriya
ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
2 Yehova akuyimba mlandu Yuda;
Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake,
adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
3 Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake;
iye atakula analimbana ndi Mulungu.
4 Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana;
analira napempha kuti amukomere mtima.
Mulungu anakumana naye ku Beteli
ndipo anayankhula naye kumeneko,
5 Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,
Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
6 Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu;
pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama,
ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.
7 Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo;
iyeyo amakonda kubera anthu.
8 Efereimu amadzitama ponena kuti,
“Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri.
Palibe amene angandiloze chala
chifukwa cha kulemera kwanga.”
9 “Ine ndine Yehova Mulungu wako
amene ndinakutulutsa mu Igupto.
Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti,
monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
10 Ndinayankhula ndi aneneri,
ndinawaonetsa masomphenya ambiri,
ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”
11 Kodi Giliyadi ndi woyipa?
Anthu ake ndi achabechabe!
Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala?
Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala
mʼmunda molimidwa.
12 Yakobo anathawira ku dziko la Aramu,
Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi,
ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
13 Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto;
kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
14 Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri.
Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa.
Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.
Mkwiyo wa Yehova pa Israeli
13 Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera;
anali wolemekezeka mu Israeli.
Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
2 Tsopano akunka nachimwirachimwirabe;
akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo,
zifanizo zopangidwa mwaluso,
zonsezo zopangidwa ndi amisiri.
Amanena za anthu awa kuti,
“Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe
ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
3 Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa,
ngati mame amene amakamuka msanga,
ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu,
ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
4 Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
amene ndinakutulutsani mu Igupto.
Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha,
palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
5 Ndinakusamalira mʼchipululu,
mʼdziko lotentha kwambiri.
6 Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta;
iwo atakhuta anayamba kunyada;
ndipo anandiyiwala Ine.
7 Motero ndidzawalumphira ngati mkango,
ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
8 Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake,
ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola.
Ndidzawapwepweta ngati mkango;
chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
9 “Iwe Israeli, wawonongedwa,
chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
10 Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse?
Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti,
amene iwe unanena za iwo kuti,
‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
11 Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima,
ndipo ndinayichotsa mwaukali.
12 Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa,
machimo ake alembedwa mʼbuku.
13 Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera,
koma iye ndi mwana wopanda nzeru,
pamene nthawi yake yobadwa yafika
iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
14 “Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda;
ndidzawawombola ku imfa.
Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti?
Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti?
“Sindidzachitanso chifundo,
15 ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake,
mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera,
ikuwomba kuchokera ku chipululu.
Kasupe wake adzaphwa
ndipo chitsime chake chidzawuma.
Chuma chake chonse chamtengowapatali
chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
16 Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo,
chifukwa anawukira Mulungu wawo.
Adzaphedwa ndi lupanga;
ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi,
akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”
Kulapa Kubweretsa Madalitso
14 Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako.
Machimo anu ndi amene akugwetsani!
2 Bweretsani zopempha zanu
ndipo bwererani kwa Yehova.
Munene kwa Iye kuti,
“Tikhululukireni machimo athu onse
ndi kutilandira mokoma mtima,
kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
3 Asiriya sangatipulumutse;
ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo,
sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’
kwa zimene manja athu omwe anazipanga,
pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
4 Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo
ndipo ndidzawakonda mwaufulu
pakuti ndaleka kuwakwiyira.
5 Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli
Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo.
Adzazika mizu yake pansi
ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
6 mphukira zake zidzakula.
Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi,
kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
7 Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake.
Iye adzakula bwino ngati tirigu.
Adzachita maluwa ngati mphesa
ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
8 Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano?
Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira.
Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira;
zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
9 Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi.
Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi.
Njira za Yehova ndi zolungama;
anthu olungama amayenda mʼmenemo,
koma anthu owukira amapunthwamo.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.