Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 120

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

120 Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga,
    ndipo Iye amandiyankha.
Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza,
    ndi kwa anthu achinyengo.

Kodi adzakuchitani chiyani,
    ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo,
    ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.

Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki,
    kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati
    pa iwo amene amadana ndi mtendere.
Ine ndine munthu wamtendere;
    koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.

Yeremiya 22:11-17

11 Pakuti zimene Yehova akunena za Yehowahazi mwana wa Yosiya, amene anatenga mpando waufumu wa Yuda mʼmalo mwa abambo ake koma nʼkuwusiya ndi izi: “Iye sadzabwereranso. 12 Iyeyo adzafera ku ukapoloko. Sadzalionanso dziko lino.”

13 “Tsoka kwa munthu womanga nyumba yake mopanda chilungamo,
    womanga zipinda zake zosanja monyenga,
pogwiritsa ntchito abale ake mwathangata,
    osawapatsa malipiro a ntchito yawo.
14 Munthuyo amati, ‘Ndidzadzimangira nyumba yayikulu
    ya zipinda zikuluzikulu zamʼmwamba.’
Kotero ndidzapanga mazenera akuluakulu,
    ndi kukhomamo matabwa a mkungudza
    ndi kukongoletsa ndi makaka ofiira.

15 “Kodi kukhala ndi nyumba ya mkungudza wambiri
    zingachititse iwe kukhala mfumu?
Ganiza za abambo ako. Suja anali ndi zonse zakudya ndi zakumwa.
    Abambo ako ankaweruza molungama ndi mosakondera,
    ndipo zonse zinkawayendera bwino.
16 Iye ankateteza anthu osauka ndi osowa,
    ndipo zonse zinkamuyendera bwino.
Kodi zimenezi sindiye tanthauzo la kudziwa Ine?”
    akutero Yehova.
17 “Koma maso ako ndi mtima sizili penanso,
    koma zili pa phindu lachinyengo,
pa zopha anthu osalakwa
    ndi pa kuzunza ndi pakulamulira mwankhanza.”

Luka 11:37-52

Tsoka la Afarisi ndi Alembi Amalamulo

37 Yesu atamaliza kuyankhula, Mfarisi wina anamuyitana kuti akadye naye. Tsono Yesu analowa mʼnyumba ndi kukhala podyera. 38 Mfarisiyo anadabwa atazindikira kuti Yesu anayamba kudya wosatsata mwambo wawo wakasambidwe ka mʼmanja.

39 Kenaka Ambuye anamuwuza kuti, “Inu Afarisi mumatsuka kunja kwa chikho ndi mbale, koma mʼkati mwanu ndi modzaza ndi kudzikonda ndi zoyipa. 40 Anthu opusa inu! Kodi amene anapanga zamʼkati sanapangenso zakunja? 41 Koma popereka kwa osauka, perekani chimene chili mʼkati ndipo chilichonse chidzakhala choyera.

42 “Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa mumapereka kwa Mulungu chakhumi cha timbewu tonunkhira, ndi timbewu tokometsera chakudya ndi mbewu zina zonse za mʼmunda, koma mumakana chilungamo ndi chikondi cha Mulungu. Mumayenera kuchita zomalizirazi osalekanso kuchita zoyambazi.

43 “Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa mumakonda mipando yofunika kwambiri mʼmasunagoge ndi malonje mʼmalo a pa msika.

44 “Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa muli ngati manda osawaka, amene anthu amangoyendapo, osawadziwa.”

45 Mmodzi mwa akatswiri a Malamulo anamuyankha Iye nati, “Aphunzitsi, pamene mukunena zinthu izi, mukutinyoza ifenso?”

46 Yesu anayankha kuti, “Tsoka kwa inunso akatswiri a Malamulo chifukwa mumawalemetsa anthu ndi mtolo umene iwo sangathe kunyamula, ndipo inu eni ake simutenga chala chanu kuti muwathandize.

47 “Tsoka kwa inu, chifukwa mumawaka manda a aneneri, komatu ndi makolo anu amene anawapha. 48 Tsono potero mumachitira umboni za zimene makolo anu anachita. Anapha aneneri, ndipo inu mumawaka manda awo. 49 Chifukwa cha ichi, Mulungu mu nzeru zake anati, ‘Ine ndidzawatumizira aneneri ndi atumwi, ena mwa iwo adzawapha ndipo ena adzawazunza.’ 50 Choncho mʼbado uwu udzasenza magazi a aneneri onse amene anakhetsedwa kuyambira pachiyambi cha dziko, 51 kuyambira magazi a Abele kufikira magazi a Zakariya amene anaphedwa pakati pa guwa lansembe ndi malo opatulika. Inde, Ine ndikuwuzani inu, mʼbado uno udzasenza zonsezi.

52 “Tsoka kwa inu akatswiri a Malamulo, chifukwa mwachotsa kiyi wachidziwitso inu eni akenu musanalowemo, ndipo mwatsekerezanso iwo amene amalowa.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.