Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
115 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi
koma ulemerero ukhale pa dzina lanu,
chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
2 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti,
“Mulungu wawo ali kuti?”
3 Mulungu wathu ali kumwamba;
Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
4 Koma mafano awo ndi siliva ndi golide,
opangidwa ndi manja a anthu.
5 Pakamwa ali napo koma sayankhula,
maso ali nawo koma sapenya;
6 makutu ali nawo koma samva,
mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
7 manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu;
mapazi ali nawo koma sayenda;
kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
8 Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo,
chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
9 Inu Aisraeli, dalirani Yehova;
Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova;
Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova;
Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa:
adzadalitsa nyumba ya Israeli,
adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova;
aangʼono ndi aakulu omwe.
14 Yehova akuwonjezereni madalitso;
inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 Mudalitsidwe ndi Yehova,
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Kumwamba ndi kwa Yehova,
koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova,
amene amatsikira kuli chete;
18 ndi ife amene timatamanda Yehova,
kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Tamandani Yehova.
Asiriya, Chida cha Yehova
8 Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira. 2 Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
3 Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’ 4 Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
5 Yehova anayankhulanso ndi Ine;
6 “Popeza anthu a dziko ili akana
madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu,
ndipo akukondwerera Rezini
ndi mwana wa Remaliya,
7 nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa
madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo;
mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo.
Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse
ndi mʼmagombe ake onse.
8 Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira,
adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi.
Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse,
iwe Imanueli!”
9 Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere!
Tamverani, inu mayiko onse akutali.
Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
10 Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu,
kambiranani zochita, koma zidzalephereka,
pakuti Mulungu ali nafe.
Yehova Achenjeza Mneneri
11 Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
12 “Usamanene kuti ndi chiwembu,
chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu
usamaope zimene anthuwa amaziopa,
ndipo usamachite nazo mantha.
13 Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera,
ndiye amene uyenera kumuopa,
ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
14 ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika;
koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala
mwala wopunthwitsa,
mwala umene umapunthwitsa anthu,
thanthwe limene limagwetsa anthu.
Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
15 Anthu ambiri adzapunthwapo
adzagwa ndi kuthyokathyoka,
adzakodwa ndi kugwidwa.”
Kuyitanidwa kwa Levi
27 Zitatha izi, Yesu anachoka ndipo anaona wolandira msonkho dzina lake Levi atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anati kwa iye, “Nditsate Ine.” 28 Ndipo Levi anayimirira, nasiya zonse ndi kumutsata Iye.
29 Kenaka Levi anakonzera Yesu phwando lalikulu ku nyumba yake ndipo gulu lalikulu la amisonkho ndi ena ankadya naye pamodzi. 30 Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amene anali a gulu lawo anadandaula kwa ophunzira ake, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukudya ndi kumwa pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”
31 Yesu anawayankha kuti, “Amene sakudwala safuna singʼanga, koma odwala. 32 Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa kuti atembenuke mtima.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.