Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 115

115 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi
    koma ulemerero ukhale pa dzina lanu,
    chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.

Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti,
    “Mulungu wawo ali kuti?”
Mulungu wathu ali kumwamba;
    Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
Koma mafano awo ndi siliva ndi golide,
    opangidwa ndi manja a anthu.
Pakamwa ali napo koma sayankhula,
    maso ali nawo koma sapenya;
makutu ali nawo koma samva,
    mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu;
    mapazi ali nawo koma sayenda;
    kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo,
    chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.

Inu Aisraeli, dalirani Yehova;
    Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova;
    Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova;
    Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.

12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa:
    adzadalitsa nyumba ya Israeli,
    adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova;
    aangʼono ndi aakulu omwe.

14 Yehova akuwonjezereni madalitso;
    inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 Mudalitsidwe ndi Yehova,
    Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

16 Kumwamba ndi kwa Yehova,
    koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova,
    amene amatsikira kuli chete;
18 ndi ife amene timatamanda Yehova,
    kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Tamandani Yehova.

Oweruza 5:1-11

Nyimbo ya Debora

“Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:

“Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli;
    ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu,
    tamandani Yehova:

“Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu!
    Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova,
    Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.

“Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri,
    pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu,
dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka
    nigwetsa madzi.
Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova,
    Mulungu wa Israeli.

“Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati,
    pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa;
    alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.
Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi
    mpaka pamene iwe Debora unafika;
    unafika ngati mayi ku Israeli.
Pamene anasankha milungu ina,
    nkhondo inabwera ku zipata za mzinda,
ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke
    pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.
Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli,
    uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu.
    Tamandani Yehova!

10 “Inu okwera pa abulu oyera,
    okhala pa zishalo,
    ndi inu oyenda pa msewu,
yankhulani. 11 Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta;
    kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana;
    akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli.

“Choncho anthu a Yehova
    anasonkhana ku zipata za mzinda.

1 Akorinto 14:26-40

Kupembedza Mwadongosolo

26 Kodi tsono abale, tinene chiyani? Pamene musonkhana pamodzi, aliyense amakhala ali ndi nyimbo yoti ayimbe, kapena mawu oti alangize, vumbulutso, malilime, kapena kumasulira kwake. Zonsezi cholinga chake chikhale kulimbikitsa mpingo. 27 Ngati wina ayankhula malilime, awiri kapena akachulukapo atatu ndiye ayankhule mmodzimmodzi, ndipo wina ayenera kutanthauzira zimene ayankhulazo. 28 Ngati palibe wotanthauzira, woyankhulayo akhale chete mu mpingo ndipo adziyankhulire iye mwini ndi Mulungu.

29 Aneneri awiri kapena atatu anenere, ndipo enawo asanthule mosamalitsa zimene anenerazo. 30 Ndipo ngati vumbulutso labwera kwa munthu amene wakhala pansi, amene akuyankhulayo akhale chete. 31 Pakuti nonse mukhoza kunenera mmodzimmodzi motsatana kuti aliyense alangizidwe ndi kulimbikitsidwa. 32 Mizimu ya aneneri imamvera ulamuliro wa aneneri. 33 Pakuti Mulungu si Mulungu wachisokonezo koma wamtendere. Monga mwa mipingo yonse ya oyera mtima.

Amayi Akhale Chete mu Mpingo

34 Amayi akhale chete mʼmisonkhano ya mpingo. Iwo asaloledwe kuyankhula, koma azikhala omvera monga mmene lamulo linenera. 35 Ngati ali ndi mafunso, akafunse amuna awo ku nyumba. Nʼchochititsa manyazi kuti mkazi ayankhule mu msonkhano wa mpingo.

36 Kodi kapena mawu a Mulungu anachokera kwa inu? Kapena anafika kwa inu nokha? 37 Ngati wina aliyense akuganiza kuti ndi mneneri kapena kuti ali ndi mphatso za Mzimu, ayenera kudziwa kuti zimene ndikukulemberanizi ndi lamulo la Ambuye. 38 Ngati munthu savomereza zimenezi, iyeyonso sadzavomerezedwa.

39 Nʼchifukwa chake, abale anga, funitsitsani kunenera, ndipo musaletse anthu kuyankhula malilime. 40 Koma chilichonse chichitike moyenera ndi mwadongosolo.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.