Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 1

BUKU LOYAMBA

Masalimo 1–41

Wodala munthu
    amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,
kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,
    kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova
    ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,
    umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake
ndipo masamba ake safota.
    Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
Sizitero ndi anthu oyipa!
    Iwo ali ngati mungu
    umene umawuluzidwa ndi mphepo.
Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,
    kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.

Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,
    koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.

Yeremiya 17:1-4

17 “Tchimo la Yuda lazokotedwa ndi cholembera cha chitsulo,
    lalembedwa ndi msonga ya mwala wadayimondi.
Uchimowo walembedwa pa mitima yawo
    ndiponso pa nyanga za maguwa awo.
Ngakhale ana awo amakumbukira
    maguwa awo ndi zoyimiritsa ngati zifanizo za mulungu wawo Asera,
pa tsinde la mitengo ya masamba ambiri,
    pa mapiri aatali mʼdzikomo.
Chuma chanu ndiponso katundu wanu yense
    ndidzazipereka kwa ofunkha
kuti zikhale dipo lawo
    chifukwa cha machimo
    ochitika mʼdziko lonse.
Mudzataya dziko limene ndinakupatsani
    kuti likhale cholowa chanu.
Ndidzakusandutsani akapolo otumikira adani anu
    mʼdziko limene inu simukulidziwa,
chifukwa mwabutsa mkwiyo wanga ngati moto,
    ndipo udzayaka mpaka muyaya.”

Luka 11:24-28

Za Mzimu Woyipa

24 “Mzimu woyipa ukatuluka mwa munthu, umakayendayenda ku malo owuma, kufunafuna malo opumulirako ndipo suwapeza. Kenaka umati, ‘Ndibwerera ku nyumba kwanga kumene ndachokera.’ 25 Ukafika umapeza mʼnyumba mosesedwa bwino ndi mokonza. 26 Pamenepo umakatenga mizimu ina isanu ndi iwiri yoyipa kwambiri kuposa iwowo ndipo imakalowa ndi kukhala mʼmenemo. Ndipo makhalidwe otsiriza a munthuyo amakhala oyipa kuposa oyamba aja.”

Munthu Wodala

27 Pamene Yesu ankanena zonsezi, mayi wina mʼgulu la anthuwo anafuwula nati, “Ndi wodala amayi amene anakubalani ndi kukulerani!”

28 Koma Yesu anayankha kuti, “Odala ndi amene amamva mawu a Mulungu ndi kuwasunga.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.