Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yeremiya 17:5-10

Yehova akuti,

“Ndi wotembereredwa munthu amene amadalira munthu mnzake,
    amene amatsamira pa munthu mnzake kuti amuthandize
    pamene mtima wake wafulatira Yehova.
Munthuyo adzakhala ngati chitsamba mʼchipululu;
    iye sadzapeza zabwino.
Adzakhala mʼchipululu mopanda madzi,
    mʼdziko lamchere limene munthu sangathe kukhalamo.

“Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova,
    amene amatsamira pa Iye.
Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi
    umene umatambalitsa mizu yake mʼmbali mwa mtsinje.
Mtengowo suopa pamene kukutentha;
    masamba ake amakhala obiriwira nthawi zonse.
Suchita mantha pa chaka cha chilala
    ndipo sulephera kubereka chipatso.”

Mtima wa munthu ndi wonyenga kupambana zinthu zonse
    ndipo kuyipa kwake nʼkosachizika.
    Ndani angathe kuwumvetsa?

10 “Ine Yehova ndimafufuza mtima
    ndi kuyesa maganizo,
ndimachitira munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake
    ndiponso moyenera ntchito zake.”

Masalimo 1

BUKU LOYAMBA

Masalimo 1–41

Wodala munthu
    amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,
kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,
    kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova
    ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,
    umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake
ndipo masamba ake safota.
    Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
Sizitero ndi anthu oyipa!
    Iwo ali ngati mungu
    umene umawuluzidwa ndi mphepo.
Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,
    kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.

Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,
    koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.

1 Akorinto 15:12-20

Kuuka kwa Oyera Mtima

12 Koma ngati timalalikira kuti Khristu anaukitsidwa kwa akufa, zikutheka bwanji kuti ena mwa inu azinena kuti kulibe kuuka kwa akufa? 13 Ngati kulibe kuuka kwa akufa, ndiye kuti ngakhale Khristu sanaukenso. 14 Ndipo ngati Khristu sanaukitsidwe, ndiye kuti kulalikira kwathu nʼkopanda ntchito, ndipo chikhulupiriro chanu nʼchopandanso ntchito. 15 Kuwonjezera pamenepa, ndiye kuti ndife mboni zabodza pa za Mulungu, pakuti tikuchita umboni kuti Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa. Ngati nʼzoona kuti akufa saukitsidwa, ndiye kuti Mulungu sanaukitsenso Khristu. 16 Pakuti ngati akufa saukitsidwa, ndiye kuti nayenso Khristu sanaukitsidwe. 17 Ndipo ngati Khristu sanaukitsidwe, chikhulupiriro chanu nʼchopanda ntchito; mukanali mu machimo anu. 18 Ndiye kuti nawonso amene agona tulo mwa Ambuye ndi otayika. 19 Ngati kukanakhala kuti tili ndi chiyembekezo mwa Khristu mʼmoyo uno wokha, tikanakhala omvetsa chisoni kuposa anthu ena onse.

20 Koma nʼzoonadi kuti Khristu anaukitsidwa kwa kufa, chipatso choyamba cha onse ogona tulo.

Luka 6:17-26

Madalitso ndi Tsoka

17 Iye anatsika pamodzi ndi atumwiwo ndipo anayima pamalo athyathyathya. Gulu lalikulu la ophunzira ake, gulu lalikulu la anthu ochokera ku Yudeya konse, ku Yerusalemu ndi ochokera mʼmphepete mwa nyanja ya Turo ndi Sidoni anali pomwepo. 18 Iwo anabwera kudzamvetsera ndi kuchiritsidwa ku matenda awo. Osautsidwa ndi mizimu yoyipa anachiritsidwa, 19 ndipo anthu ankayesetsa kuti amukhudze chifukwa mphamvu imatuluka mwa Iye ndi kuchiritsa onse.

20 Akuyangʼana ophunzira ake, Iye anati,

“Odala ndinu amene ndi osauka,
    chifukwa ufumu wa Mulungu ndi wanu.
21 Inu amene mukumva njala tsopano, ndinu odala
    chifukwa mudzakhutitsidwa.
Inu amene mukulira tsopano, ndinu odala
    chifukwa mudzasekerera.
22 Ndinu odala, anthu akamakudani,
    kukusalani ndi kukunyozani
    ndi kumayipitsa dzina lanu chifukwa cha Mwana wa Munthu.

23 “Nthawi imeneyo sangalalani ndipo lumphani ndi chimwemwe chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba. Pakuti ndi zomwezonso zimene makolo awo anachitira aneneri.

24 “Ndinu atsoka, anthu olemera,
    popeza mwalandiriratu zokusangalatsani.
25 Tsoka inu amene mukudya bwino tsopano,
    chifukwa mudzakhala ndi njala.
Ndinu atsoka, amene mukusekerera tsopano,
    chifukwa mudzabuma ndi kulira.
26 Ndinu atsoka, anthu akamakuyamikirani,
    popeza makolo anu anawachitira aneneri onama zomwezi.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.