Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova,
anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi
ndi kuona anthu onse;
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira
onse amene amakhala pa dziko lapansi.
15 Iye amene amapanga mitima ya onse,
amaona zonse zimene akuchita.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo;
palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso,
ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye;
amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
19 kuwawombola iwo ku imfa
ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo;
Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera,
pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
22 Chikondi chanu chosatha
chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
6 Yehova, dzanja lanu lamanja
ndi laulemerero chifukwa cha mphamvu zake.
Ndithu Yehova, dzanja lanu lamanja
linaphwanya mdani.
7 Ndi ulemerero wanu waukulu,
munagonjetsa okutsutsani.
Inu munatumiza mkwiyo wanu waukulu;
ndipo unawapsereza ngati udzu.
8 Ndi mpweya wotuluka mʼmphuno mwanu
madzi anawunjikana pamodzi.
Nyanja yakuya ija inasanduka
madzi owuma gwaa kufika pansi.
9 Mdaniyo anati,
“Ine ndidzawalondola, ndipo ndidzawagwira.
Ndidzagawa chuma chawo;
ndiye chokhumba changa chidzakwaniritsidwa.
Ine ndidzasolola lupanga langa,
ndi mkono wanga ndidzawawononga.”
10 Koma Inu munawuzira mphepo yanu,
ndipo nyanja inawaphimba.
Iwo anamira ngati chitsulo
mʼmadzi amphamvu.
11 Ndithu Yehova, pakati pa milungu,
ndani afanana nanu? Inu amene muli woyera,
ndiponso wotamandika wolemekezeka,
chifukwa cha ntchito zanu,
zazikulu ndi zodabwitsa?
Mitsinje ya Madzi Opatsa Moyo
37 Pa tsiku lomaliza ndi lalikulu kwambiri laphwando, Yesu anayimirira nafuwula nati, “Ngati munthu ali ndi ludzu, abwere kwa Ine kuti adzamwe. 38 Malemba kuti ‘Aliyense amene akhulupirira Ine, mitsinje yamadzi amoyo idzatuluka kuchokera mʼkati mwake.’ ” 39 Ponena izi Iye amatanthauza Mzimu Woyera, amene adzalandire amene amakhulupirira Iye. Pa nthawiyi nʼkuti Mzimu Woyera asanaperekedwe, pakuti Yesu anali asanalemekezedwe.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.