Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 145

Salimo la matamando la Davide.

145 Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga;
    ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku
    ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.

Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse;
    ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina;
    Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu,
    ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri,
    ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu,
    ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.

Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo,
    wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Yehova ndi wabwino kwa onse;
    amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova;
    oyera mtima adzakulemekezani.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu
    ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu
    ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya,
    ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse.

Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse
    ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa
    ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu,
    ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Mumatsekula dzanja lanu
    ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.

17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse,
    ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana,
    onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa;
    amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda
    koma adzawononga anthu onse oyipa.

21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova.
    Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera
    ku nthawi za nthawi.

Yesaya 54:1-8

Ulemerero Wamʼtsogolo wa Ziyoni

54 “Sangalala, iwe mayi wosabala,
    iwe amene sunabalepo mwana;
imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe,
    iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka;
chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri
    kuposa mkazi wokwatiwa,”
            akutero Yehova.
Kulitsa malo omangapo tenti yako,
    tambasula kwambiri nsalu zake,
    usaleke;
talikitsa zingwe zako,
    limbitsa zikhomo zako.
Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere;
    ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina
    ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.

“Usachite mantha; sadzakunyozanso.
    Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso.
Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako
    ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako,
    dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu;
    dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
Yehova wakuyitananso,
    uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima,
mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,”
    akutero Mulungu wako.
“Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya,
    koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa
    ndili wokwiya kwambiri.
Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya,
    ndidzakuchitira chifundo,”
    akutero Yehova Mpulumutsi wako.

Aroma 12:9-21

Chikondi

Chikondi chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choyipa; gwiritsitsa chabwino. 10 Mukondane kwathunthu monga abale. Lemekezanani wina ndi mnzake kuposa inu eni. 11 Musakhale aulesi mʼmachitidwe anu. Khalani achangu mu mzimu ndipo tumikirani Ambuye. 12 Kondwerani mʼchiyembekezo, pirirani mʼmasautso ndiponso khulupirikani mʼpemphero. 13 Gawanani ndi anthu a Mulungu amene ali ndi chosowa. Cherezani alendo.

14 Adalitseni amene akuzunzani. Adalitseni ndipo musawatemberere. 15 Kondwani pamodzi ndi amene akukondwa ndipo lirani ndi amene akulira. 16 Muyanjane wina ndi mnzake. Musakhale onyada, koma lolani kuyanjana ndi anthu wamba. Musaganize kuti mumadziwa zonse.

17 Musabwezere choyipa ndi choyipa kwa aliyense. Samalitsani kuchita chabwino pamaso pa aliyense. 18 Ngati nʼkotheka, khalani mwamtendere ndi aliyense monga momwe mungathere. 19 Okondedwa anga, musabwezere choyipa, koma lekerani Mulungu. Pakuti kwalembedwa, “Kubwezera chilango nʼkwanga. Ndidzawalanga ndine,” akutero Ambuye. 20 Koma,

“Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya.
    Ngati ali ndi ludzu, mupatse kanthu kakumwa.
Pochita ichi, udzamuwunjikira makala amoto pamutu pake.”

21 Musagonjetsedwe ndi choyipa, koma gonjetsani choyipa pochita chabwino.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.