Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
6 Nsembe ndi zopereka Inu simuzifuna,
koma makutu anga mwawatsekula;
zopereka zopsereza ndi zopereka chifukwa cha tchimo
Inu simunazipemphe.
7 Kotero ndinati, “Ndili pano, ndabwera.
Mʼbuku mwalembedwa za ine.
8 Ndikufuna kuchita chifuniro chanu, Inu Mulungu wanga;
lamulo lanu lili mu mtima mwanga.”
9 Ndikulalikira uthenga wa chilungamo chanu mu msonkhano waukulu;
sinditseka milomo yanga
monga mukudziwa Inu Yehova.
10 Sindibisa chilungamo chanu mu mtima mwanga;
ndinayankhula za kukhulupirika kwanu ndi chipulumutso chanu.
Ine sindiphimba chikondi chanu ndi choonadi chanu
pa msonkhano waukulu.
11 Musandichotsere chifundo chanu Yehova;
chikondi chanu ndi choonadi chanu zinditeteze nthawi zonse.
12 Pakuti mavuto osawerengeka andizungulira;
machimo anga andigonjetsa, ndipo sindingathe kuona.
Alipo ambiri kuposa tsitsi la mʼmutu mwanga,
ndipo mtima wanga ukufowoka mʼkati mwanga.
13 Pulumutseni Yehova;
Bwerani msanga Yehova kudzandithandiza.
14 Onse amene akufunafuna kuchotsa moyo wanga
achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa;
onse amene amakhumba chiwonongeko changa
abwezedwe mwamanyazi.
15 Iwo amene amanena kwa ine kuti, “Hee! Hee!”
abwerere akuchita manyazi.
16 Koma iwo amene amafunafuna Inu
akondwere ndi kusangalala mwa Inu;
iwo amene amakonda chipulumutso chanu
nthawi zonse anene kuti, “Yehova akwezeke!”
17 Komabe Ine ndine wosauka ndi wosowa;
Ambuye andiganizire.
Inu ndinu thandizo langa ndi wondiwombola wanga;
Inu Mulungu wanga, musachedwe.
53 Ndani wakhulupirira zimene tanenazi;
kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
2 Iye anakula ngati mphukira pamaso pake,
ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma.
Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira,
analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
3 Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu,
munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa,
ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona.
Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
4 Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife;
ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu.
Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga,
kumukantha ndi kumusautsa.
5 Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu,
ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu;
iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere,
ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
6 Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera,
aliyense mwa ife akungodziyendera;
ndipo Yehova wamusenzetsa
zoyipa zathu zonse.
7 Anthu anamuzunza ndi kumusautsa,
koma sanayankhule kanthu.
Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira,
kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta,
momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
8 Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha.
Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake,
poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo?
Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
9 Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa
ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma,
ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa,
kapena kuyankhula za chinyengo.
10 Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa.
Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa.
Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali,
ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
11 Atatha mazunzo a moyo wake,
adzaona kuwala, ndipo adzakhutira.
Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri,
popeza adzasenza zolakwa zawo.
12 Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu,
adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu,
popeza anapereka moyo wake mpaka kufa,
ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe.
Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri,
ndipo anawapempherera anthu olakwa.
Yesu Nsembe ya Anthu Onse
10 Malamulo ndi chithunzithunzi cha zinthu zabwino zimene zikubwera, osati madalitso enieniwo. Pa chifukwa chimenechi sizingatheke konse kuti nsembe zimodzimodzi, zoperekedwa kawirikawiri, kosalekeza ndi chaka ndi chaka, kuti nʼkusandutsa angwiro amene amabwera kudzapembedza. 2 Ngati zikanamatero iwowo akanasiya kupereka nsembezo. Pakuti opembedzawo akanamayeretsedwa kamodzi kokha, sibwenzi chikumbumtima chawo chikuwatsutsabe chifukwa cha machimo awo. 3 Koma nsembezo zimawakumbutsa anthuwo machimo awo chaka ndi chaka. 4 Chifukwa nʼkosatheka kuti magazi angʼombe yayimuna ndi mbuzi yayimuna achotse machimo.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.