Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 87

Salimo la Ana a Kora.

87 Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
    Yehova amakonda zipata za Ziyoni
    kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
Za ulemerero wako zimakambidwa,
    Iwe mzinda wa Mulungu:
            Sela
“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni
    pakati pa iwo amene amandidziwa.
Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi,
    ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’ ”

Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti,
    “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye,
    ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina:
    “Uyu anabadwira mʼZiyoni.”
            Sela
Oyimba ndi ovina omwe adzati,
    “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”

Yoweli 3:17-20

Madalitso a Anthu a Mulungu

17 “Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu,
    ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika.
Yerusalemu adzakhala wopatulika;
    alendo sadzamuthiranso nkhondo.

18 “Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano,
    ndipo zitunda zidzayenderera mkaka;
    mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi.
Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova
    ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.
19 Koma Igupto adzasanduka bwinja,
    Edomu adzasanduka chipululu,
chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda
    mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.
20 Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya
    ndi Yerusalemu ku mibadomibado.

Mateyu 21:28-32

Fanizo la Ana Amuna Awiri

28 “Kodi muganiza bwanji? Panali munthu wina anali ndi ana aamuna awiri. Anapita kwa woyamba nati, ‘Mwanawe pita kagwire ntchito lero mʼmunda wamphesa.’

29 “Iye anayankha kuti, ‘Sindipita,’ koma pambuyo pake anasintha maganizo napita.

30 “Kenaka abambowo anapita kwa mwana winayo nanena chimodzimodzi. Iye anayankha kuti, ‘Ndipita abambo,’ koma sanapite.

31 “Ndani wa awiriwa anachita chimene abambo ake amafuna?”

Anamuyankha nati, “Woyambayo.”

Yesu anawawuza kuti, “Ndikuwuzani zoonadi, kuti amisonkho ndi adama akulowa mu ufumu wa Mulungu inu musanalowemo.” 32 Pakuti Yohane anabwera kwa inu kuti akuonetseni njira yachilungamo, koma inu simunakhulupirire iye, koma amisonkho ndi adama anamukhulupirira. Koma ngakhale munaona izi, simunatembenuke mtima ndi kumukhulupirira iye.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.