Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Salimo la Ana a Kora.
87 Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
2 Yehova amakonda zipata za Ziyoni
kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
3 Za ulemerero wako zimakambidwa,
Iwe mzinda wa Mulungu:
Sela
4 “Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni
pakati pa iwo amene amandidziwa.
Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi,
ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’ ”
5 Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti,
“Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye,
ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
6 Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina:
“Uyu anabadwira mʼZiyoni.”
Sela
7 Oyimba ndi ovina omwe adzati,
“Akasupe anga onse ali mwa iwe.”
9 Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina:
Konzekerani nkhondo!
Dzutsani ankhondo amphamvu!
Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.
10 Sulani makasu anu kuti akhale malupanga
ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo.
Munthu wofowoka anene kuti,
“Ndine wamphamvu!”
11 Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse,
ndipo musonkhane kumeneko.
Tumizani ankhondo anu Yehova!
12 “Mitundu ya anthu idzuke;
ipite ku Chigwa cha Yehosafati,
pakuti kumeneko Ine ndidzakhala
ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.
13 Tengani chikwakwa chodulira tirigu,
pakuti mbewu zakhwima.
Bwerani dzapondeni mphesa,
pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza
ndipo mitsuko ikusefukira;
kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”
14 Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu,
mʼchigwa cha chiweruzo!
Pakuti tsiku la Yehova layandikira
mʼchigwa cha chiweruzo.
15 Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa,
ndipo nyenyezi sizidzawalanso.
16 Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni
ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu;
dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka.
Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake,
linga la anthu a ku Israeli.
Akulu Ampingo ndi Anyamata mu Mpingo
5 Ine ndikupempha akulu a mpingo amene ali pakati panu, monga inenso mkulu mnzawo, mboni ya zowawa za Khristu ndiponso amene ndidzalandira nawo ulemerero umene uti udzaonetsedwe. 2 Wetani gulu la Mulungu limene lili mʼmanja mwanu, muziliyangʼanira. Muzichita osati mowumirizidwa, koma mwakufuna kwanu, monga momwe Mulungu akufunira kuti mutero. Musachite chifukwa chadyera la ndalama, koma ndi mtima ofuna kutumikira. 3 Musakhale ngati mafumu pa amene mukuwayangʼanira, koma mukhale chitsanzo kwa gululo. 4 Ndipo Mʼbusa wamkulu akadzaonekera, mudzalandira chipewa cha ulemerero chosafota.
5 Momwemonso, inu anyamata gonjerani amene ndi akulu. Inu nonse mukhale odzichepetsa kuti mutumikirane, chifukwa,
“Mulungu amatsutsana nawo odzikuza,
koma amapereka chisomo kwa odzichepetsa.”
6 Choncho, mudzichepetse pamaso pa Mulungu wamphamvu, kuti pa nthawi yake adzakukwezeni. 7 Tayani pa Iye nkhawa zanu zonse chifukwa ndiye amakusamalani.
8 Khalani odziretsa ndi atcheru. Mdani wanu mdierekezi amayendayenda monga mkango wobangula kufunafuna wina kuti amumeze. 9 Mukaneni iye, ndipo mukhazikike mʼchikhulupiriro, chifukwa mukudziwa kuti abale anzanu pa dziko lonse lapansi nawonso akumva zowawa zomwezi.
10 Ndipo Mulungu wachisomo chonse, amene anakuyitanani ku ulemerero wake wamuyaya mwa Khristu, mutamva zowawa pa kanthawi, adzakukonzaninso ndi kukulimbitsani pa maziko olimba. 11 Kwa Iye kukhale mphamvu mpaka muyaya, Ameni.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.