Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 129

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

129 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,”
    anene tsono Israeli;
“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,
    koma sanandipambane.
Anthu otipula analima pa msana panga
    ndipo anapangapo mizere yayitali:
Koma Yehova ndi wolungama;
    Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”

Onse amene amadana ndi Ziyoni
    abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba,
    umene umafota usanakule;
sungadzaze manja a owumweta
    kapena manja a omanga mitolo.
Odutsa pafupi asanene kuti,
    “Dalitso la Yehova lili pa inu;
    tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”

Yeremiya 50:1-7

Uthenga Wonena za Babuloni

50 Uthenga umene Yehova anayankhula ndi mneneri Yeremiya wonena za mzinda wa Babuloni ndi anthu ake ndi uwu:

“Lengeza ndi kulalika pakati pa anthu a mitundu ina,
    kweza mbendera ndipo ulengeze;
    usabise kanthu, koma uwawuze kuti,
‘Babuloni wagwa;
    mulungu wawo Beli wachititsidwa manyazi,
    nayenso Mariduku wagwidwa ndi mantha.
Milungu yake yagwidwa ndi mantha
    ndipo mafano ake adzagwidwa ndi mantha.’
Mtundu wa anthu wochokera kumpoto wadzathira nkhondo Babuloni
    ndi kusandutsa bwinja dziko lake.
Kumeneko sikudzakhalanso
    munthu kapena nyama.

“Masiku amenewo, nthawi imeneyo,”
    akutero Yehova,
“anthu a ku Israeli ndi anthu a ku Yuda
    onse pamodzi adzabwera akulira. Adzafunitsitsa kuchita zimene Yehova Mulungu wawo akufuna.
Adzafunsa njira ya ku Ziyoni
    ndi kuyamba ulendo wopita kumeneko.
Iwo adzadzipereka kwa Yehova
    pochita naye pangano lamuyaya
    limene silidzayiwalika.

“Anthu anga ali ngati nkhosa zotayika;
    abusa awo
    anawasocheretsa mʼmapiri.
Iwo anayendayenda mʼmapiri ndi mʼzitunda
    mpaka kuyiwala kwawo.
Aliyense amene anawapeza anawawononga;
    adani awo anati, ‘Ife si olakwa,
chifukwa iwo anachimwira Yehova, amene ali mpumulo wawo weniweni
    ndi amene makolo awo anamukhulupirira.’

Yeremiya 50:17-20

17 “Aisraeli ali ngati nkhosa zomwe zabalalika
    pothamangitsidwa ndi mikango.
Mfumu ya ku Asiriya ndiye inayamba kuwapha Aisraeliwo.
    Wotsiriza anali Nebukadinezara
mfumu ya ku Babuloni
    amene anachita ngati kuphwanya mafupa ake.”

18 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti,

“Ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi dziko lake
    monga momwe ndinalangira mfumu ya ku Asiriya.
19 Koma ndidzabwezera Israeli ku msipu wake
    ndipo adzadya mʼminda ya ku Karimeli ndi Basani;
adzadya nakhuta ku mapiri
    a ku Efereimu ndi Giliyadi.
20 Masiku amenewo, nthawi imeneyo,”
    akutero Yehova,
“anthu adzafunafuna zolakwa za Israeli
    koma sadzapeza nʼchimodzi chomwe,
ndipo adzafufuza machimo a Yuda,
    koma sadzapeza ndi limodzi lomwe,
    chifukwa otsala amene ndawasiya ndidzawakhululukira.

Luka 22:39-46

Yesu Apemphera ku Phiri la Olivi

39 Yesu anapitanso monga mwa masiku onse ku Phiri la Olivi, ndipo ophunzira ake anamutsatira Iye. 40 Atafika pamalopo, Iye anawawuza kuti, “Pempherani kuti musagwe mʼmayesero.” 41 Iye anapita patsogolo pangʼono patali ngati kuponya mwala, anagwada napephera kuti, 42 “Atate ngati mukufuna chotsereni chikho ichi. Komatu muchite zimene mukufuna osati zimene ndikufuna ine.” 43 Mngelo wochokera kumwamba anafika namulimbikitsa. 44 Ndipo mopsinjika mtima, anapemphera moona mtima, ndipo thukuta lake linali ngati madontho a magazi akugwera pansi.

45 Iye atamaliza kupemphera, ndi kubwerera kwa ophunzira ake, anawapeza atagona atafowoka ndi chisoni. 46 Iye anafunsa kuti, Nʼchifukwa chiyani mukugona? “Dzukani ndipo pempherani kuti inu musagwe mʼmayesero.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.