Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide.
22 Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya?
Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe?
Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
2 Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha,
usikunso, ndipo sindikhala chete.
3 Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu;
ndinu matamando a Israeli.
4 Pa inu makolo athu anadalira;
iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
5 Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa.
Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
6 Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu,
wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
7 Onse amene amandiona amandiseka;
amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
8 “Iyeyu amadalira Yehova,
musiyeni Yehovayo amulanditse.
Musiyeni Yehova amupulumutse
popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
9 Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga.
Munachititsa kuti ndizikudalirani
ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
10 Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu;
kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
11 Musakhale kutali ndi ine,
pakuti mavuto ali pafupi
ndipo palibe wina wondipulumutsa.
12 Ngʼombe zazimuna zandizungulira;
ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
13 Mikango yobangula pokadzula nyama,
yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
14 Ine ndatayika pansi ngati madzi
ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake.
Mtima wanga wasanduka phula;
wasungunuka mʼkati mwanga.
15 Mphamvu zanga zauma ngati phale,
ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada;
mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
Mawu a Zofari
20 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe
chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza,
ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale,
kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha,
chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba
ndipo mutu wake uli nengʼaa,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe;
iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso,
adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso;
sadzapezekanso pamalo pake.
10 Ana ake adzabwezera zonse
zimene iyeyo analanda anthu osauka;
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake
zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake
ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
13 ngakhale salola kuzilavula,
ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake;
chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza;
Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo
ululu wa mphiri udzamupha.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje,
mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya;
sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo;
iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha,
sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
21 Palibe chatsala kuti iye adye;
chuma chake sichidzachedwa kutha.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera;
mavuto aakulu adzamugwera.
23 Akadya nʼkukhuta,
Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto
ngati mvula yosalekeza.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo,
muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana,
songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake.
Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake.
Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza
ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake;
dziko lapansi lidzamuwukira.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake,
katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa,
mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
Miyambo ya Makolo
15 Pamenepo Afarisi ena ndi aphunzitsi amalamulo anabwera kwa Yesu kuchokera ku Yerusalemu ndipo anamufunsa kuti, 2 “Chifukwa chiyani ophunzira anu amaphwanya mwambo wa akuluakulu? Iwo sasamba mʼmanja pakudya!”
3 Yesu anayankha kuti, “Nanga chifukwa chiyani inu mumaphwanya lamulo la Mulungu chifukwa cha mwambo wa makolo anu? 4 Pakuti Mulungu anati, ‘Lemekeza abambo ako ndi amayi ako’ ndipo ‘aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.’ 5 Koma inu mumati, ngati munthu anena kwa abambo ake kapena amayi ake kuti, ‘Thandizo lililonse mukalirandira kuchokera kwa ine ndi mphatso yoperekedwa kwa Mulungu,’ 6 iye sakulemekeza nayo abambo ake ndipo ndi khalidwe lotere inu mumapeputsa nalo Mawu a Mulungu chifukwa cha mwambo wanu. 7 Inu anthu achiphamaso, Yesaya ananenera za inu kuti,
8 “ ‘Anthu awa amandilemekeza Ine ndi milomo yawo,
koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.
9 Amandilambira Ine kwachabe
ndi kuphunzitsa malamulo ndi malangizo a anthu.’ ”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.