Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide.
22 Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya?
Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe?
Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
2 Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha,
usikunso, ndipo sindikhala chete.
3 Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu;
ndinu matamando a Israeli.
4 Pa inu makolo athu anadalira;
iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
5 Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa.
Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
6 Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu,
wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
7 Onse amene amandiona amandiseka;
amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
8 “Iyeyu amadalira Yehova,
musiyeni Yehovayo amulanditse.
Musiyeni Yehova amupulumutse
popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
9 Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga.
Munachititsa kuti ndizikudalirani
ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
10 Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu;
kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
11 Musakhale kutali ndi ine,
pakuti mavuto ali pafupi
ndipo palibe wina wondipulumutsa.
12 Ngʼombe zazimuna zandizungulira;
ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
13 Mikango yobangula pokadzula nyama,
yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
14 Ine ndatayika pansi ngati madzi
ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake.
Mtima wanga wasanduka phula;
wasungunuka mʼkati mwanga.
15 Mphamvu zanga zauma ngati phale,
ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada;
mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
Mawu a Bilidadi
18 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 “Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi?
Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
3 Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe
ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
4 Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako,
kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo?
Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
5 “Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa;
malawi a moto wake sakuwalanso.
6 Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima;
nyale ya pambali pake yazima.
7 Mayendedwe ake amgugu azilala;
fundo zake zomwe zamugwetsa.
8 Mapazi ake amulowetsa mu ukonde
ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
9 Msampha wamkola mwendo;
khwekhwe lamugwiritsitsa.
10 Amutchera msampha pansi mobisika;
atchera diwa pa njira yake.
11 Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse,
zikutsatira mayendedwe ake onse.
12 Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala,
tsoka likumudikira.
13 Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse;
miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
14 Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira,
ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
15 Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo;
awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
16 Mizu yake ikuwuma pansi
ndipo nthambi zake zikufota
17 Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi;
sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
18 Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima,
ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
19 Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake,
kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
20 Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake;
anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
21 Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa;
amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”
Mpumulo wa Anthu a Mulungu
4 Popeza lonjezo lakuti tidzalowe mu mpumulo umene anatilonjeza lilipobe, tiyeni tisamale kuti pasakhale wina aliyense mwa inu wodzalephera kulowamo. 2 Pakuti Uthenga Wabwino unalalikidwa kwa ife, monganso iwo aja; koma iwo sanapindule nawo uthengawo chifukwa anangomva koma osakhulupirira. 3 Tsono ife amene takhulupirira talowa mu mpumulo, monga momwe Mulungu akunenera kuti,
“Ndili wokwiya ndinalumbira kuti,
‘Iwo sadzalowa konse mu mpumulo wanga.’ ”
Ananena zimenezi ngakhale anali atatsiriza kale ntchito yolenga dziko lapansi. 4 Pena pake wayankhula za tsiku lachisanu ndi chiwiri mʼmawu awa: “Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, Mulungu anapumula ku ntchito zake zonse.” 5 Pa ndime inonso akunena za zomwezo pamene akuti, “Iwo sadzalowa konse mu mpumulo wanga.”
6 Popeza kwatsalabe kuti ena adzalowe mu mpumulowo, koma aja anayamba kumva Uthenga Wabwino sanalowe chifukwa cha kusamvera kwawo. 7 Nʼchifukwa chake Mulungu anayikanso tsiku lina limene analitcha “Lero.” Patapita nthawi yayitali Iye anayankhula za tsiku lomweli kudzera mwa Davide, monga ndinanena kale kuti,
“Lero mukamva mawu ake,
musawumitse mitima yanu.”
8 Ngati Yoswa akanalowetsa anthu mu mpumulo, Mulungu sakananena pambuyo pake za tsiku lina. 9 Kotero tsono kwatsala mpumulo wa Sabata kwa anthu a Mulungu; 10 Pakuti aliyense amene analowa mu mpumulo wa Mulungu anapuma pa ntchito zake, monga momwe Mulungu anachitira. 11 Tiyeni tsono tiyesetse kulowa mu mpumulo, kuti pasapezeke wina aliyense wolephera potsatira chitsanzo chawo cha kusamvera.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.