Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe.
55 Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu,
musakufulatire kupempha kwanga,
2 mverani ndipo mundiyankhe.
Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
3 chifukwa cha mawu a adani anga,
chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa;
pakuti andidzetsera masautso
ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
4 Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga;
mantha a imfa andigwera.
5 Mantha ndi kunjenjemera zandizinga;
mantha aakulu andithetsa nzeru.
6 Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda!
Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
7 Ndikanathawira kutali
ndi kukakhala mʼchipululu.
8 Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo;
kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
9 Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo;
pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
10 Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake;
nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
11 Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda;
kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
12 Akanakhala mdani akundinyoza, ine
ndikanapirira;
akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane,
ndikanakabisala.
13 Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye,
bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
14 Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala
pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
15 Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi;
alowe mʼmanda ali amoyo
pakuti choyipa chili pakati pawo.
Mawu a Zofari
11 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
2 “Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa?
Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
3 Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku?
Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
4 Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika
ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
5 Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula
kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
6 ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake,
pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri.
Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
7 “Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu?
Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
8 Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani?
Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani?
9 Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi
ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
10 “Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende
nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
11 Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo;
akaona choyipa, kodi sachizindikira?
12 Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru
monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
13 “Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye
ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
14 ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako
ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
15 udzatukula mutu wako wosachita manyazi;
udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
16 Udzayiwala ndithu zowawa zako,
zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
17 Moyo wako udzawala kupambana usana,
ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
18 Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo;
ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
19 Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza
ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
20 Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza,
ndipo adzasowa njira yothawirapo;
chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”
10 Kwa amene ali pa banja ndikupatsani lamulo ili (osati langa koma la Ambuye): Mkazi asalekane ndi mwamuna wake. 11 Koma ngati atatero, asakwatiwenso, apo ayi, abwerere kwa mwamuna wakeyo. Ndipo mwamuna asaleke mkazi wake.
12 Kwa ena onse ndikunena izi (ineyo osati Ambuye); ngati mʼbale wina ali ndi mkazi wosakhulupirira ndipo mkaziyo walola kukhala pa banja ndi mʼbaleyo, ameneyo asamuleke. 13 Ngati mayi wina ali ndi mwamuna wosakhulupirira ndipo mwamunayo walola kukhala pa banja ndi mayiyo, ameneyo asamuleke. 14 Pakuti mwamuna wosakhulupirirayo amayeretsedwa chifukwa cha mkazi wakeyo, ndipo mkazi wosakhulupirira amayeretsedwa chifukwa cha mwamuna wokhulupirirayo. Kupanda apo ana anu akanakhala odetsedwa, koma mmene zililimu ndi oyeretsedwa.
15 Koma ngati wosakhulupirira achoka, mulekeni achoke. Zikatero ndiye kuti mwamuna kapena mkazi wokhulupirirayo sali womangikanso. Mulungu anatiyitana kuti tikhale mu mtendere. 16 Kodi iwe, mkazi, ungadziwe bwanji kuti mwina nʼkupulumutsa mwamuna wako? Kapena iwe, mwamuna, ungadziwe bwanji kuti mwina nʼkupulumutsa mkazi wako?
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.