Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
95 Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe,
tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
2 Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko
ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.
3 Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu,
mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
4 Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi,
ndipo msonga za mapiri ndi zake.
5 Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye,
ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.
6 Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira,
tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
7 pakuti Iye ndiye Mulungu wathu
ndipo ife ndife anthu a pabusa pake,
ndi nkhosa za mʼdzanja lake.
Lero ngati inu mumva mawu ake,
8 musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba,
monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
9 Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa,
ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
10 Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo;
ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera
ndipo sanadziwe njira zanga.”
11 Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti,
“Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”
Kuuka kwa Israeli
8 Iwe mdani wanga, usandiseke!
Ngakhale ndagwa, ndidzauka.
Ngakhale ndikukhala mu mdima,
Yehova ndiye kuwunika kwanga.
9 Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova,
chifukwa ndinamuchimwira,
mpaka ataweruza mlandu wanga
ndi kukhazikitsa chilungamo changa.
Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika;
ndidzaona chilungamo chake.
10 Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi
nadzagwidwa ndi manyazi,
iye amene anandifunsa kuti,
“Ali kuti Yehova Mulungu wako?”
Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga;
ngakhale tsopano adzaponderezedwa
ngati matope mʼmisewu.
11 Idzafika nthawi yomanganso makoma anu,
nthawi yokulitsanso malire anu.
12 Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu
kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto,
ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate
ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso
kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
13 Dziko lapansi lidzasanduka chipululu
chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.
Pemphero ndi Matamando
14 Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza,
nkhosa zimene ndi cholowa chanu,
zimene zili zokha mʼnkhalango,
mʼdziko la chonde.
Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi
monga masiku akale.
15 “Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga,
ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”
16 Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi,
ngakhale ali ndi mphamvu zotani.
Adzagwira pakamwa pawo
ndipo makutu awo adzagontha.
17 Adzabwira fumbi ngati njoka,
ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi.
Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo;
mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu
ndipo adzachita nanu mantha.
18 Kodi alipo Mulungu wofanana nanu,
amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa
za anthu otsala amene ndi cholowa chake?
Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya
koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
19 Inu mudzatichitiranso chifundo;
mudzapondereza pansi machimo athu
ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
20 Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo,
ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu,
monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu
masiku amakedzana.
26 Atayimba nyimbo, anapita ku phiri la Olivi.
Yesu Aneneratu zakuti Petro Adzamukana
27 Yesu anati, “Nonse mudzandithawa, pakuti kwalembedwa:
“ ‘Kantha Mʼbusa,
ndipo nkhosa zidzabalalika.’
28 Koma ndikadzauka, ndidzatsogola kupita ku Galileya.”
29 Petro anati, “Ngakhale onse adzakuthaweni, ine sindidzatero.”
30 Yesu anayankha kuti, “Zoona ndikukuwuza kuti lero lino, usiku uno, tambala asanalire kawiri, iweyo udzandikana katatu.”
31 Koma Petro ananenetsa kuti, “Ngakhale kutakhala kufa nanu, ine sindidzakukanani.” Ndipo ena onse ananena chimodzimodzi.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.