Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 95

95 Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe,
    tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko
    ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.

Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu,
    mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi,
    ndipo msonga za mapiri ndi zake.
Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye,
    ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.

Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira,
    tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
pakuti Iye ndiye Mulungu wathu
    ndipo ife ndife anthu a pabusa pake,
    ndi nkhosa za mʼdzanja lake.

Lero ngati inu mumva mawu ake,
    musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba,
    monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa,
    ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
10 Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo;
    ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera
    ndipo sanadziwe njira zanga.”
11 Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti,
    “Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”

Mika 7:8-20

Kuuka kwa Israeli

Iwe mdani wanga, usandiseke!
    Ngakhale ndagwa, ndidzauka.
Ngakhale ndikukhala mu mdima,
    Yehova ndiye kuwunika kwanga.
Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova,
    chifukwa ndinamuchimwira,
mpaka ataweruza mlandu wanga
    ndi kukhazikitsa chilungamo changa.
Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika;
    ndidzaona chilungamo chake.
10 Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi
    nadzagwidwa ndi manyazi,
iye amene anandifunsa kuti,
    “Ali kuti Yehova Mulungu wako?”
Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga;
    ngakhale tsopano adzaponderezedwa
    ngati matope mʼmisewu.

11 Idzafika nthawi yomanganso makoma anu,
    nthawi yokulitsanso malire anu.
12 Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu
    kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto,
ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate
    ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso
    kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
13 Dziko lapansi lidzasanduka chipululu
    chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.

Pemphero ndi Matamando

14 Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza,
    nkhosa zimene ndi cholowa chanu,
zimene zili zokha mʼnkhalango,
    mʼdziko la chonde.
Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi
    monga masiku akale.

15 “Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga,
    ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”

16 Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi,
    ngakhale ali ndi mphamvu zotani.
Adzagwira pakamwa pawo
    ndipo makutu awo adzagontha.
17 Adzabwira fumbi ngati njoka,
    ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi.
Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo;
    mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu
    ndipo adzachita nanu mantha.
18 Kodi alipo Mulungu wofanana nanu,
    amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa
    za anthu otsala amene ndi cholowa chake?
Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya
    koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
19 Inu mudzatichitiranso chifundo;
    mudzapondereza pansi machimo athu
    ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
20 Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo,
    ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu,
monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu
    masiku amakedzana.

Marko 14:26-31

26 Atayimba nyimbo, anapita ku phiri la Olivi.

Yesu Aneneratu zakuti Petro Adzamukana

27 Yesu anati, “Nonse mudzandithawa, pakuti kwalembedwa:

“ ‘Kantha Mʼbusa,
    ndipo nkhosa zidzabalalika.’

28 Koma ndikadzauka, ndidzatsogola kupita ku Galileya.”

29 Petro anati, “Ngakhale onse adzakuthaweni, ine sindidzatero.”

30 Yesu anayankha kuti, “Zoona ndikukuwuza kuti lero lino, usiku uno, tambala asanalire kawiri, iweyo udzandikana katatu.”

31 Koma Petro ananenetsa kuti, “Ngakhale kutakhala kufa nanu, ine sindidzakukanani.” Ndipo ena onse ananena chimodzimodzi.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.