Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
124 Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
anene tsono Israeli,
2 akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
potiwukira anthuwo,
3 iwo atatipsera mtima,
akanatimeza amoyo;
4 chigumula chikanatimiza,
mtsinje ukanatikokolola,
5 madzi a mkokomo
akanatikokolola.
6 Atamandike Yehova,
amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
7 Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame
yokodwa mu msampha wa mlenje;
msampha wathyoka,
ndipo ife tapulumuka.
8 Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova
wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Za Mkazi Wachigololo
7 Mwana wanga, mvera mawu anga;
usunge bwino malamulo angawa.
2 Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo;
samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
3 Uchite ngati wawamangirira pa zala zako,
ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
4 Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,”
ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
7 Koma aliyense wa ife wapatsidwa chisomo molingana ndi muyeso wa mphatso ya Khristu. 8 Nʼchifukwa chake akunena kuti,
“Iye atakwera kumwamba,
anatenga chigulu cha a mʼndende
ndipo anapereka mphatso kwa anthu.”
9 Kodi mawu akuti, “Iye anakwera” akutanthauza chiyani, ngati Iyeyo sanatsikire kunsi kwa dziko lapansi? 10 Iye amene anatsika ndi yemweyo anakwera koposa mʼmayiko a kumwamba onse, ndi cholinga choti zinthu zonse zikhale zodzaza ndi Iye. 11 Iye ndiye amene anapereka mphatso kwa ena kuti akhale atumwi ndi ena aneneri, ena alaliki, ndi ena abusa ndi aphunzitsi. 12 Ntchito yawo ndi kukonza oyera mtima kuti agwire ntchito ya utumiki kuti thupi la Khristu lilimbikitsidwe. 13 Izi zidzatifikitsa tonse ku umodzi wachikhulupiriro, kumudziwa Mwana wa Mulungu, kukhwima msinkhu ndi kufika pa muyeso wangwiro weniweni wopezeka mwa Khristu.
14 Motero sitidzakhalanso makanda, ogwedezekagwedezeka ndi mafunde, otengekatengeka ndi mphepo iliyonse ya chiphunzitso ndi kuchenjera kwa anthu achinyengo amene amasocheretsa anthu ndi kuchenjera kwawo. 15 Mʼmalo mwake, poyankhula choonadi mwachikondi, tidzakula mu zinthu zonse ndi kukhala thupi la Khristu, amene ndi Mutu, omwe ndi mpingo. 16 Mwa Iye thupi lonse lalumikizidwa ndi kugwirana pamodzi ndi mitsempha yothandizira. Likukula ndi kudzilimbitsa lokha mwachikondi, pomwe chiwalo chilichonse chikugwira ntchito yake.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.