Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yesaya 52:7-10

Ngokongoladi mapazi a
    amithenga obweretsa nkhani yabwino amene akuyenda pa mapiri.
Iwo akukubweretserani nkhani zabwino za mtendere,
    chisangalalo ndi chipulumutso.
    Iwo akubwera kudzawuza anthu
a ku Ziyoni kuti,
    “Mulungu wako ndi mfumu!”
Mverani! Alonda anu akukweza mawu awo;
    akuyimba pamodzi mwachimwemwe.
Popeza akuona chamaso
    kubwera kwa Yehova ku Yerusalemu.
Imbani pamodzi mofuwula nyimbo zachimwemwe,
    inu mabwinja a Yerusalemu,
pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake,
    wapulumutsa Yerusalemu.
10 Yehova wagwiritsa ntchito mphamvu zake zopatulika
    pamaso pa anthu a mitundu yonse,
ndipo anthu onse a dziko lapansi
    adzaona chipulumutso cha Mulungu wathu.

Masalimo 98

Salimo.

98 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,
    pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa;
dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera
    zamuchitira chipulumutso.
Yehova waonetsa chipulumutso chake
    ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
Iye wakumbukira chikondi chake
    ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli;
malekezero onse a dziko lapansi aona
    chipulumutso cha Mulungu wathu.

Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi,
    muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze,
    ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna
    fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.

Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo,
    dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo,
    mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
izo ziyimbe pamaso pa Yehova,
    pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi.
Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo,
    ndi mitundu ya anthu mosakondera.

Ahebri 1:1-4

Khristu Mwana wa Mulungu Aposa Angelo

Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri. Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero. Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.

Ahebri 1:5-12

Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati,

“Iwe ndiwe mwana wanga;
    Ine lero ndakhala Atate ako.”

Kapena kunenanso kuti,

“Ine ndidzakhala abambo ake;
    iye adzakhala mwana wanga.”

Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati,

“Angelo onse a Mulungu amupembedze Iye.”

Iye ponena za angelo akuti,

“Mulungu amasandutsa angelo ake mphepo,
    amasandutsa atumiki ake malawi amoto.”

Koma za Mwana wake akuti,

“Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya,
    ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu.
Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;
    Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu
    pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”

10 Mulungu akutinso,

“Ambuye, pachiyambi Inu munayika maziko a dziko lapansi;
    ndipo zakumwambako ndi ntchito za manja anu.
11 Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire.
    Izo zidzatha ngati zovala.
12 Mudzazipindapinda ngati chofunda;
    ndipo zidzasinthidwa ngati chovala.
Koma Inu simudzasintha,
    ndipo zaka zanu sizidzatha.”

Yohane 1:1-14

Mawu Asandulika Thupi

Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu. Mawuwa anali ndi Mulungu pachiyambi.

Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa. Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu. Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.

Kunabwera munthu amene anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu; Iyeyo dzina lake linali Yohane. Iye anabwera ngati mboni kudzachitira umboni kuwunikako kuti kudzera mwa iye anthu onse akhulupirire. Iyeyu sanali kuwunika; koma anabwera ngati mboni ya kuwunika. Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.

10 Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye. 11 Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye. 12 Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu; 13 ana wobadwa osati monga mwachilengedwe, kapena chisankho cha munthu, kapena chifuniro cha mwamuna koma wobadwa mwa Mulungu.

14 Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.