Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
18 “Iwalani zinthu zakale;
ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.
19 Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano!
Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona?
Ine ndikulambula msewu mʼchipululu
ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.
20 Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi
zinandilemekeza.
Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma
kuti ndiwapatse madzi anthu anga
osankhidwa.
21 Anthu amene ndinadziwumbira ndekha
kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.
22 “Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo,
munatopa nane, Inu Aisraeli.
23 Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza,
kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu.
Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya
kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.
24 Simunandigulire bango lonunkhira
kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu.
Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu
ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.
25 “Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza
zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini,
ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
41 Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka;
Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
2 Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake;
Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko
ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
3 Yehova adzamuthandiza pamene akudwala
ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.
4 Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo;
chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
5 Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti,
“Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
6 Pamene wina abwera kudzandiona,
amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe;
kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.
7 Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane,
iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
8 “Matenda owopsa amugwira;
sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
9 Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira,
iye amene amadya pamodzi ndi ine
watukula chidendene chake kulimbana nane.
10 Koma Yehova mundichititre chifundo,
dzutseni kuti ndiwabwezere.
11 Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane,
pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
12 Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga
ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.
13 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli
kuchokera muyaya mpaka muyaya.
Ameni ndi Ameni.
18 Koma zoona monga Mulungu ali wokhulupirika, uthenga wathu kwa inu siwakuti, “Inde” nʼkutinso “Ayi.” 19 Pakuti Yesu Khristu mwana wa Mulungu amene ine, Silivano ndi Timoteyo tinamulalikira pakati panu sali “Inde” yemweyonso “Ayi.” Koma nthawi zonse mwa Iye muli “Inde.” 20 Pakuti ngakhale malonjezo a Mulungu atachuluka chotani, onsewo ndi “Inde” mwa Khristu. Kotero kuti mwa Iye, ife timati “Ameni” kuchitira Mulungu ulemu. 21 Tsono ndi Mulungu amene anachititsa kuti inu ndi ife tiyime molimba mwa Khristu. Anatidzoza ife, 22 nayikanso Mzimu wake mʼmitima mwathu kutitsimikizira za mʼtsogolo.
Yesu Achiritsa Munthu Wofa Ziwalo
2 Patapita masiku pangʼono, Yesu atalowanso mu Kaperenawo, zinamveka kuti wabwera ali mʼnyumba. 2 Choncho anthu ambiri anasonkhana kotero kuti panalibenso malo, ngakhale ndi pa khomo pomwe, ndipo Iye anawalalikira mawu. 3 Amuna anayi anabwera, atanyamula munthu wofa ziwalo. 4 Popeza sakanatha kufika naye kwa Yesu chifukwa cha gulu la anthu, anasasula denga chapamwamba pamene panali Yesu, ndipo atabowoleza, anatsitsa mphasa yomwe munthu wofa ziwaloyo anagonapo. 5 Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati kwa wofa ziwaloyo, “Mwana, machimo ako akhululukidwa.”
6 Ndipo ena mwa aphunzitsi amalamulo anakhala pansi pomwepo, namaganiza mʼmitima mwawo kuti, 7 “Nʼchifukwa chiyani munthuyu ayankhula chotere? Iye akuchitira mwano Mulungu! Ndani angakhululukire munthu machimo kupatula Mulungu yekha?”
8 Nthawi yomweyo Yesu anadziwa mu mzimu wake kuti izi ndi zimene ankaganiza mʼmitima yawo, ndipo anawawuza kuti, “Chifukwa chiyani mukuganiza zinthu izi? 9 Chapafupi nʼchiyani; kunena kwa wofa ziwaloyu kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kuti, ‘Imirira, tenga mphasa yako ndipo yenda?’ 10 Koma kuti mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo.” Anati kwa wofa ziwaloyo, 11 “Ndikuwuza iwe, imirira, tenga mphasa yako ndipo pita kwanu.” 12 Anayimirira, nanyamula mphasa yake natuluka onse akumuona. Izi zinadabwitsa aliyense ndipo anayamika Mulungu nati, “Sitinaonepo zinthu ngati izi!”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.