Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
41 Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka;
Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
2 Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake;
Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko
ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
3 Yehova adzamuthandiza pamene akudwala
ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.
4 Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo;
chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
5 Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti,
“Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
6 Pamene wina abwera kudzandiona,
amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe;
kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.
7 Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane,
iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
8 “Matenda owopsa amugwira;
sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
9 Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira,
iye amene amadya pamodzi ndi ine
watukula chidendene chake kulimbana nane.
10 Koma Yehova mundichititre chifundo,
dzutseni kuti ndiwabwezere.
11 Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane,
pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
12 Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga
ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.
13 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli
kuchokera muyaya mpaka muyaya.
Ameni ndi Ameni.
Nthumwi Zochokera ku Babuloni
39 Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira. 2 Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.
3 Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?”
Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
4 Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?”
Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”
5 Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse: 6 Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe. 7 Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”
8 Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”
Yesu Achiritsa Anthu Ambiri
38 Yesu anatuluka mʼsunagoge ndipo anapita kwa Simoni. Tsopano mpongozi wake wa Simoni amadwala malungo akulu, ndipo anamupempha Yesu kuti amuthandize. 39 Ndipo anawerama nadzudzula malungowo ndipo anamusiya. Anadzuka nthawi yomweyo nayamba kuwatumikira.
40 Pamene dzuwa linkalowa, anthu anabweretsa kwa Yesu onse amene anali ndi matenda osiyanasiyana, ndipo atasanjika manja ake pa aliyense, anachiritsidwa. 41 Komanso ziwanda zinkatuluka mwa anthu ambiri, zikufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!” Koma Iye anazidzudzula ndipo sanazilole kuyankhula chifukwa zimadziwa kuti Iye ndi Khristu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.