Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
147 Tamandani Yehova.
Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu,
nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
2 Yehova akumanga Yerusalemu;
Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
3 Akutsogolera anthu osweka mtima
ndi kumanga mabala awo.
4 Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi,
ndipo iliyonse amayitchula dzina.
5 Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri;
nzeru zake zilibe malire.
6 Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa,
koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
7 Imbirani Yehova ndi mayamiko;
imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
8 Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo;
amapereka mvula ku dziko lapansi
ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
9 Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe
ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
10 Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo,
kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 Yehova amakondwera ndi amene amamuopa,
amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
20 Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu;
anthu enawo sadziwa malamulo ake.
Tamandani Yehova.
Za Kupasuka kwa Babuloni ndi Mafano Ake
46 Beli wagwada pansi, Nebo wawerama;
nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo.
Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe.
Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.
2 Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo;
sizikutha kupulumutsa katunduyo,
izo zomwe zikupita ku ukapolo.
3 Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo,
inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli,
Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu,
ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.
4 Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi
ndidzakusamalirani ndithu.
Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani,
ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.
5 “Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani?
Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?
6 Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo
ndipo amayeza siliva pa masikelo;
amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu,
kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.
7 Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo;
amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo.
Singathe kusuntha pamalo pakepo.
Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha;
kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.
8 “Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi,
Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.
9 Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana;
chifukwa Ine ndine Mulungu
ndipo palibe wina ofanana nane.
10 Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe.
Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike.
Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi.
Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.
11 Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa.
Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa.
Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi;
zimene ndafuna ndidzazichitadi.
12 Ndimvereni, inu anthu owuma mtima,
inu amene muli kutali ndi chipulumutso.
13 Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa;
sichili kutali.
Tsikulo layandikira
ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani
ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.
Yesu Achiritsa Munthu Wolumala Dzanja
9 Atachoka kumeneko anakalowa mʼsunagoge mwawo. 10 Ndipo mʼmenemo munali munthu wolumala dzanja. Pofuna chifukwa chokamunenezera, iwo anamufunsa Yesu kuti, “Kodi nʼkololedwa kuchiritsa munthu tsiku la Sabata?”
11 Iye anawawuza kuti, “Ngati wina wa inu ali ndi nkhosa nigwera mʼdzenje tsiku la Sabata, kodi simudzayigwira ndi kuyitulutsa kunja? 12 Nanga munthu sali oposa nkhosa kwambiri! Chifukwa chake nʼkololedwa kuchita zabwino pa Sabata.”
13 Pamenepo Yesu anati kwa munthuyo, “Wongola dzanja lako.” Iye analiwongola ndipo linakhala monga linalili kale. 14 Koma Afarisi anatuluka kunja ndi kukonza njira yoti amuphere.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.