Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Kuyitanidwa kwa Womva Ludzu
55 “Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu,
bwerani madzi alipo;
ndipo inu amene mulibe ndalama
bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye!
Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka
osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
2 Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya,
ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa?
Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino;
ndipo mudzisangalatse.
3 Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine;
mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo.
Ndidzachita nanu pangano losatha,
chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
4 Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu,
kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
5 Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa,
ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu.
Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu,
Woyerayo wa Israeli,
wakuvekani ulemerero.”
6 Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka.
Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
7 Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa,
ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa.
Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo,
ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.
8 “Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu,
ngakhale njira zanu si njira zanga,”
akutero Yehova.
9 “Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi,
momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu,
ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda.
63 Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga,
moona mtima ine ndimakufunafunani;
moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu,
thupi langa likulakalaka inu,
mʼdziko lowuma ndi lotopetsa
kumene kulibe madzi.
2 Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika
ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 Chifukwa chikondi chanu
ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga,
ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona.
Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6 Pa bedi panga ndimakumbukira inu;
ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 Chifukwa ndinu thandizo langa,
ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 Moyo wanga umakangamira Inu;
dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
Chenjezo Kuchokera Mʼmbiri ya Israeli
10 Pakuti sindikufuna kuti inu mukhale osadziwa zenizeni, abale, kuti makolo athu anatsogozedwa ndi mtambo ndikuti onse anawoloka nyanja. 2 Ndipo onse anabatizidwa mwa Mose mu mtambo ndi mʼnyanja. 3 Onse anadya chakudya chimodzi chauzimu 4 ndipo anamwa chakumwa chimodzi chauzimu; popeza anamwa kuchokera mʼthanthwe lomwe anayenda nalo, ndipo thanthwe limeneli linali Khristu. 5 Ngakhale zinali choncho, Mulungu sanakondwere ndi ambiri a iwo, motero ambiri mwa iwo anafera mʼchipululu.
6 Tsono zinthu izi zinachitika kuti zikhale chitsanzo, kuti ife tisayike mitima yathu pa zinthu zoyipa monga anachitira makolo athuwo. 7 Musakhale anthu opembedza mafano, monga analili ena mwa iwo. Pakuti zalembedwa kuti, “Anthuwo anakhala pansi nayamba kudya ndi kumwa. Kenaka anayimirira nayamba kuvina mwachilendo.” 8 Tisachite chigololo monga ena mwa iwo anachitira ndipo tsiku limodzi anafapo anthu 23,000. 9 Tisamuyese Khristu, monga ena mwa iwo anachitira ndipo anaphedwa ndi njoka. 10 Ndipo osamawiringula, monga ena mwa iwo anachitira naphedwa ndi mngelo wowononga.
11 Zinthu izi zinawachitikira kuti zikhale chitsanzo ndipo zinalembedwa kuti zikhale chenjezo kwa ife, amene tiyandikira nthawi ya kutha kwa zonse. 12 Choncho, ngati mukuganiza kuti mwayima mwamphamvu, samalani mungagwe! 13 Palibe mayesero amene mwakumana nawo oposa amene anthu ena onse anakumana nawo. Mulungu ngokhulupirika; sadzalola kuti inu muyesedwe koposa muyeso umene mutha kupirira. Koma pamene mwayesedwa, Iyenso adzakupatsani njira yopambanira mayeserowo.
Za Kutembenuka Mtima
13 Nthawi yomweyo panali ena amene analipo omwe amamuwuza Yesu za Agalileya amene magazi awo Pilato anawasakaniza ndi nsembe zawo. 2 Yesu anayankha kuti, “Kodi mukuganiza kuti Agalileya amenewa anali ochimwa kwambiri kuposa Agalileya ena onse chifukwa anavutika mʼnjira iyi? 3 Ine ndikuti, ayi! Koma ngati inu simutembenuka mtima, inunso mudzawonongeka nonse. 4 Kapena anthu 18 aja amene anafa nsanja ya Siloamu itawagwera, kodi mukuganiza kuti iwo aja anali ochimwa kwambiri kuposa onse amene amakhala mu Yerusalemu? 5 Ine ndikuti, ayi! Koma ngati inu simutembenuka mtima, inunso mudzawonongeka nonse.”
6 Kenaka Iye anawawuza fanizo kuti, “Munthu wina anali ndi mtengo wamkuyu, umene anadzala mʼmunda wamphesa, ndipo Iye anapita kukayangʼana zipatso, koma sanazipeze. 7 Tsono kwa munthu amene amasamalira munda wamphesawo anati, ‘Kwa zaka zitatu tsopano ndakhala ndikubwera kudzafuna chipatso pa mtengo uwu ndipo sindinachipeze. Udule! Nʼchifukwa chiyani ukuwononga nthaka?’
8 “Munthuyo anayankha kuti, ‘Bwana, tawusiyani kwa chaka chimodzi chokha ndipo ine ndikumba ngalande mozungulira ndi kuthira manyowa. 9 Ngati udzabale zipatso chaka chamawa, zili bwino! Koma ngati sudzabala, pamenepo mudzawudule.’ ”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.