Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 16

Mikitamu ya Davide.

16 Ndisungeni Inu Mulungu,
    pakuti ine ndimathawira kwa Inu.

Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga;
    popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”
Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko,
    amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.
Anthu amene amathamangira kwa milungu ina
    mavuto awo adzachulukadi.
Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi
    kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.

Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa;
    mwateteza kolimba gawo langa.
Malire a malo anga akhala pabwino;
    ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.

Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu;
    ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.
Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse.
    Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja,
    sindidzagwedezeka.

Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera;
    thupi langanso lidzakhala pabwino,
10 chifukwa Inu simudzandisiya ku manda,
    simudzalola kuti woyera wanu avunde.
11 Inu mwandidziwitsa njira ya moyo;
    mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu,
    ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.

Nyimbo ya Solomoni 8:6-7

Undiyike pamtima pako ngati chidindo,
    ngati chidindo cha pa dzanja lako;
pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa,
    nsanje ndiyaliwuma ngati manda.
Chikondi chimachita kuti lawilawi
    ngati malawi a moto wamphamvu.
Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi,
    mitsinje singachikokolole chikondicho.
Ngati wina apereka chuma chonse
    cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi,
    adzangonyozeka nazo kotheratu.

Yohane 20:11-20

11 koma Mariya anayima kunja kwa manda akulira. Pamene akulira, anawerama ndi kusuzumira mʼmanda 12 ndipo anaona angelo awiri atavala zoyera, atakhala pamene panali mtembo wa Yesu, mmodzi kumutu ndi wina kumapazi.

13 Iwo anamufunsa iye kuti, “Amayi, nʼchifukwa chiyani mukulira?”

Iye anati, “Amuchotsa Mbuye wanga, ndipo ine sindikudziwa kumene iwo amuyika.” 14 Atanena izi, iye anatembenuka ndipo anaona Yesu atayima potero koma iye sanazindikire kuti anali Yesu.

15 Iye anati, “Amayi, mukulira chifukwa chiyani? Ndani amene mukumufunafuna?”

Poganiza kuti anali mwini munda, iye anati, “Bwana, ngati inu mwamuchotsa, ndiwuzeni kumene mwamuyika, ndipo ine ndikamutenga.”

16 Yesu anati kwa iye, “Mariya.”

Anatembenukira kwa Iye nafuwula mu Chiaramaiki kuti, “Raboni!” (kutanthauza Mphunzitsi).

17 Yesu anati, “Usandigwire Ine, pakuti sindinapite kwa Atate. Mʼmalo mwake pita kwa abale anga ndikukawawuza kuti, ndikupita kwa Atate ndi kwa Atate anunso, kwa Mulungu wanga ndi Mulungu wanunso.”

18 Mariya wa ku Magadala anapita kwa ophunzira ndi uthenga wakuti, “Ndamuona Ambuye!” Iye anawawuza iwo kuti Yesu ananena zinthu izi kwa iye.

Yesu Aonekera kwa Ophunzira ake Tomasi Palibe

19 Madzulo a tsiku limenelo limene linali loyamba la Sabata ophunzira ake ali pamodzi, atatseka ndi kukhoma zitseko chifukwa choopa Ayuda, Yesu anabwera ndi kuyima pakati pawo nati, “Mtendere ukhale nanu!” 20 Iye atatha kunena izi, anawaonetsa manja ake ndi mʼnthiti mwake. Ophunzira anasangalala kwambiri pamene anaona Ambuye.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.