Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Old/New Testament

Each day includes a passage from both the Old Testament and New Testament.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 77-78

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu.

77 Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo;
    ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye;
    usiku ndinatambasula manja mosalekeza
    ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.

Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula;
    ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka.
            Sela
Munagwira zikope zanga kuti ndisagone
    ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
Ndinaganizira za masiku akale,
    zaka zamakedzana;
Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku.
    Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,

“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya?
    Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu?
    Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima?
    Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”

10 Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso:
    zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
11 Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova;
    Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
12 Ndidzakumbukira ntchito zanu
    ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”

13 Njira zanu Mulungu ndi zoyera.
    Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
14 Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa;
    Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
15 Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu,
    zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe.
            Sela

16 Madzi anakuonani Mulungu,
    madzi anakuonani ndipo anachita mantha;
    nyanja yozama inakomoka.
17 Mitambo inakhuthula madzi ake pansi,
    mu mlengalenga munamveka mabingu;
    mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
18 Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu,
    mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse;
    dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
19 Njira yanu inadutsa pa nyanja,
    njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu,
    ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.

20 Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa
    mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.

Ndakatulo ya Asafu.

78 Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa;
    mvetserani mawu a pakamwa panga.
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo,
    ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
zimene tinazimva ndi kuzidziwa,
    zimene makolo athu anatiwuza.
Sitidzabisira ana awo,
    tidzafotokozera mʼbado wotsatira
ntchito zotamandika za Yehova,
    mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo
    ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli,
zimene analamulira makolo athu
    kuphunzitsa ana awo,
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa,
    ngakhale ana amene sanabadwe,
    ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu
    ndipo sadzayiwala ntchito zake
    koma adzasunga malamulo ake.
Iwo asadzakhale monga makolo awo,
    mʼbado wosamvera ndi wowukira,
umene mitima yake inali yosamvera Mulungu,
    umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.

Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta,
    anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 iwo sanasunge pangano la Mulungu
    ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 Anayiwala zimene Iye anachita,
    zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona,
    mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo,
    Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 Anawatsogolera ndi mtambo masana
    ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu
    ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala
    ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.

17 Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye,
    kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 Ananyoza Mulungu mwadala
    pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti,
    “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 Iye atamenya thanthwe
    madzi anatuluka,
    ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi.
Koma iye angatipatsenso ife chakudya?
    Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 Yehova atawamva anakwiya kwambiri;
    moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo,
    ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu
    kapena kudalira chipulumutso chake.
23 Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba
    ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 anagwetsa mana kuti anthu adye,
    anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 Anthu anadya buledi wa angelo,
    Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba,
    ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi,
    mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo,
    kuzungulira matenti awo onse.
29 Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka
    pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho,
    chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 mkwiyo wa Mulungu unawayakira;
    Iye anapha amphamvu onse pakati pawo,
    kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.

32 Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa;
    ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya.
    Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo;
    iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo,
    kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo,
    kumunamiza ndi malilime awo;
37 Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye,
    iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 Komabe Iye anali wachifundo;
    anakhululukira mphulupulu zawo
    ndipo sanawawononge.
Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake
    ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe,
    mphepo yopita imene sibwereranso.

40 Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu
    ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu;
    ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 Sanakumbukire mphamvu zake,
    tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto,
    zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi;
    Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga,
    ndiponso achule amene anawasakaza.
46 Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala,
    zokolola zawo kwa dzombe.
47 Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala
    ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala,
    zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo,
    anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso.
    Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 Analolera kukwiya,
    sanawapulumutse ku imfa
    koma anawapereka ku mliri.
51 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto,
    zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto;
    anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha
    koma nyanja inamiza adani awo.
54 Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera,
    ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo
    ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo;
    Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.

56 Koma iwo anayesa Mulungu
    ndi kuwukira Wammwambamwamba;
    sanasunge malamulo ake.
57 Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo,
    anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano;
    anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri;
    Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 Anasiya nyumba ya ku Silo,
    tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo,
    ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 Anapereka anthu ake ku lupanga;
    anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 Moto unanyeketsa anyamata awo,
    ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 ansembe awo anaphedwa ndi lupanga,
    ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.

65 Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo,
    ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 Iye anathamangitsa adani ake;
    anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe,
    sanasankhe fuko la Efereimu;
68 Koma anasankha fuko la Yuda,
    phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda,
    dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 Anasankha Davide mtumiki wake
    ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa
    kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo,
    wa Israeli cholowa chake.
72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama;
    ndi manja aluso anawatsogolera.

Aroma 10

10 Abale, chokhumba cha mtima wanga ndi pemphero langa kwa Mulungu ndi chakuti Aisraeli apulumutsidwe. Popeza ndiwachitira umboni kuti ndi achangu pa zinthu za Mulungu koma osati mwachidziwitso. Pakuti sanadziwe chilungamo chochokera kwa Mulungu ndipo anafuna kukhazikitsa chawochawo. Iwo sanagonjere chilungamo cha Mulungu. Khristu ndiye mathero amalamulo kuti aliyense amene akhulupirira akhale olungama pamaso pa Mulungu.

Mose akulemba motere zachilungamo cha malamulo, “Munthu amene achita zinthu izi adzakhala ndi moyo pozichita.” Koma chilungamo cha chikhulupiriro chikuti, “Usanene mu mtima mwako kuti, ‘Kodi ndani amene akwere kumwamba?’ ” (ndiko, kukatsitsa Khristu) “kapena ‘Ndani adzatsikira ku dziko la anthu akufa?’ ” (ndiko, kukamutenga Khristu kwa akufa). Nanga akuti chiyani? “Mawu ali pafupi ndi inu. Ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu.” Ndiwo mawu achikhulupiriro amene ife tikuwalalikira, kuti ngati udzavomereza ndi pakamwa pako kuti, “Yesu ndiye Ambuye,” ndi kukhulupirira mu mtima mwako kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka. 10 Pakuti ndi mtima wanu mukhulupirira ndi kulungamitsidwa, ndipo ndi pakamwa panu muvomereza ndi kupulumutsidwa. 11 Pakuti Malemba akuti, “Aliyense amene akhulupirira Iye, sadzachititsidwa manyazi.” 12 Pakuti palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, pakuti Ambuye mmodzi yemweyo ndi Ambuye wa onse ndipo amadalitsa mochuluka onse amene ayitana pa Iye 13 pakuti, “Aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.”

14 Kodi adzayitana bwanji amene sanamukhulupirire? Ndipo adzakhulupirira bwanji asanamve za Iye? Ndipo adzamva bwanji popanda wina kulalikira kwa iwo? 15 Ndipo iwo adzalalikira bwanji osatumidwa? Kwalembedwa kuti, “Akongoladi mapazi a iwo amene amabweretsa Uthenga Wabwino!”

16 Koma si onse amene anavomereza Uthenga Wabwino. Pakuti Yesaya akuti, “Ambuye, ndani amene wakhulupirira uthenga wathu?” 17 Motero, chikhulupiriro chimabwera pamene timva uthenga ndipo uthenga umamveka kuchokera ku mawu a Khristu. 18 Koma ndikufunsa kuti kodi iwo anamva? Inde, iwo anamva kuti,

“Liwu lawo linamveka ponseponse pa dziko lapansi.
    Mawu awo anafika ku malekezero a dziko lonse.”

19 Ine ndifunsanso kuti, kodi Israeli sanazindikire? Poyamba Mose akuti,

“Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake.
    Ine ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.”

20 Ndipo Yesaya molimba mtima akuti,

“Anandipeza anthu amene sanali kundifunafuna.
    Ndinadzionetsera kwa amene sanafunse za Ine.”

21 Koma zokhudzana ndi Aisraeli akuti,

“Tsiku lonse ndinatambasulira manja anga
    kwa anthu osandimvera ndi okanika.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.