Old/New Testament
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda.
63 Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga,
moona mtima ine ndimakufunafunani;
moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu,
thupi langa likulakalaka inu,
mʼdziko lowuma ndi lotopetsa
kumene kulibe madzi.
2 Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika
ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 Chifukwa chikondi chanu
ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga,
ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona.
Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6 Pa bedi panga ndimakumbukira inu;
ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 Chifukwa ndinu thandizo langa,
ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 Moyo wanga umakangamira Inu;
dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
9 Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa;
adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 Iwo adzaperekedwa ku lupanga
ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu;
onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo,
koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
64 Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga;
tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
2 Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa,
ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
3 Iwo amanola malilime awo ngati malupanga,
amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
4 Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa;
amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
5 Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa,
amayankhula zobisa misampha yawo;
ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
6 Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati,
“Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!”
Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
7 Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi;
mwadzidzidzi adzakanthidwa.
8 Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa
ndi kuwasandutsa bwinja;
onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
9 Anthu onse adzachita mantha;
adzalengeza ntchito za Mulungu
ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
10 Lolani wolungama akondwere mwa Yehova
ndi kubisala mwa Iye,
owongoka mtima onse atamande Iye!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo.
65 Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni;
kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
2 Inu amene mumamva pemphero,
kwa inu anthu onse adzafika.
3 Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo,
Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
4 Odala iwo amene inu muwasankha
ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu!
Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu,
za mʼNyumba yanu yoyera.
5 Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo,
Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,
chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi
ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
6 amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu,
mutadziveka nokha ndi mphamvu.
7 Amene munakhalitsa bata nyanja
kukokoma kwa mafunde ake,
ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
8 Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu;
kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera.
Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.
9 Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira;
Inuyo mumalilemeretsa kwambiri.
Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi
kuti upereke tirigu kwa anthu,
pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
10 Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake,
mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
11 Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka,
ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
12 Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira;
mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
13 Madambo akutidwa ndi zoweta
ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu;
izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.
Kufa ku Tchimo, Kukhala ndi Moyo mwa Khristu
6 Nanga tinene chiyani? Kodi tipitirire kuchimwa kuti chisomo chichulukebe? 2 Ayi. Mʼnjira iliyonse! Popeza tinafa ku tchimo, nanga tidzapitirira bwanji kukhalabe mʼmenemo? 3 Kodi simukudziwa kuti tonse amene tinabatizidwa mwa Khristu Yesu tinabatizidwa mu imfa yake? 4 Chifukwa chake ife tinayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Iye mwa ubatizo. Tinalowa mu imfa ndi cholinga choti monga momwe Khristu anaukitsidwa kwa akufa ndi ulemerero wa Atate, ifenso tikakhale mʼmoyo watsopano.
5 Pakuti ngati ife tinakhala amodzi ndi Iye mu imfa yake, tidzakhalanso ndithu amodzi ndi Iye mu kuuka kwake. 6 Ife tikudziwa kuti umunthu wathu wakale unapachikidwa pamodzi ndi Iye kuti thupi la uchimo likhale lopanda mphamvu ndi kuti tisakakhalenso akapolo a tchimo 7 chifukwa aliyense amene anafa anamasuka ku tchimo.
8 Koma ngati tinafa pamodzi ndi Khristu, tikhulupirira kuti tidzakhalanso ndi moyo pamodzi ndi Iye. 9 Pakuti tikudziwa kuti popeza Khristu anaukitsidwa kwa akufa, Iye sangafenso. Imfa ilibenso mphamvu pa Iye. 10 Imfa imene Iye anafa, anafa ku tchimo kamodzi kokha, koma moyo umene akhala ndi wa kwa Mulungu.
11 Kotero inunso, mudzione nokha ngati akufa ku tchimo koma a moyo kwa Mulungu mwa Khristu Yesu. 12 Nʼchifukwa chake, musalole tchimo lilamulire matupi anu amene anafa kuti mumvere zilakolako zonyansa. 13 Musapereke ziwalo zathupi lanu ku tchimo, ngati zipangizo zamakhalidwe oyipa. Mʼmalo mwake, mudzipereke kwa Mulungu, ngati amene achoka ku imfa kupita ku moyo. Ndipo mupereke ziwalo zathupi lanu ngati zipangizo zachilungamo. 14 Tchimo silidzakhalanso ndi mphamvu pa inu, chifukwa Malamulo sakulamulira moyo wanu koma chisomo.
Ife Ndife Akapolo a Mulungu
15 Nʼchiyani tsono? Kodi tidzichimwa chifukwa sitikulamulidwa ndi Malamulo koma chisomo? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! 16 Kodi inu simudziwa kuti pamene mudzipereka kwa wina wake, kumumvera ngati akapolo, ndinu akapolo a amene mumumvera? Ngati ndinu akapolo a tchimo mudzafa. Koma ngati ndinu akapolo akumvera, mudzakhala olungama pamaso pake. 17 Koma ayamikidwe Mulungu pakuti ngakhale munali akapolo a tchimo, munamvera ndi mtima wonse chiphunzitso chimene munalandira. 18 Inu munamasulidwa ku tchimo ndipo tsopano mwasanduka akapolo achilungamo.
19 Ine ndikufanizira zinthu za tsiku ndi tsiku chifukwa chikhalidwe chanu nʼchofowoka. Monga momwe munkapereka ziwalo za matupi kukhala akapolo a zonyansa ndi makhalidwe oyipa, zimene zimanka zichulukirabe, choncho tsopano dziperekeni ziwalozo kuti zikhale akapolo achilungamo ndi a kuyera mtima. 20 Pomwe munali akapolo atchimo, simunkalabadira za chilungamo. 21 Kodi munapeza phindu lanji pochita zinthu zimenezi, zomwe tsopano mukuchita nazo manyazi? Zinthu zimenezo zotsatira zake ndi imfa! 22 Koma tsopano pakuti inu mwamasulidwa ku tchimo ndipo mwasanduka akapolo a Mulungu, phindu lomwe mulipeza ndi kuyera mtima ndipo chotsatira chake ndi moyo wosatha. 23 Pakuti malipiro a tchimo ndi imfa, koma mphatso yaulere imene Mulungu amapereka ndi moyo wosatha mwa Khristu Yesu Ambuye athu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.