Old/New Testament
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga.
57 Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo,
pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo.
Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu
mpaka chiwonongeko chitapita.
2 Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba,
kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
3 Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa,
kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri.
Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
4 Ine ndili pakati pa mikango,
ndagona pakati pa zirombo zolusa;
anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi,
malilime awo ndi malupanga akuthwa.
5 Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba;
mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
6 Iwo anatchera mapazi anga ukonde
ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa.
Anakumba dzenje mʼnjira yanga
koma agweramo okha mʼmenemo.
7 Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu
mtima wanga ndi wokhazikika.
Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
8 Dzuka moyo wanga!
Dzukani zeze ndi pangwe!
Ndidzadzuka mʼbandakucha.
9 Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu,
ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
10 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba;
kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
11 Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba,
mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide.
58 Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama?
Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
2 Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama,
ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
3 Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera;
kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
4 Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka,
ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
5 Imene simva liwu la munthu wamatsenga,
ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
6 Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu,
Yehova khadzulani mano a mikango!
7 Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda
pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
8 Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda;
ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
9 Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku,
kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango,
pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 Ndipo anthu adzanena kuti,
“Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho;
zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe.
59 Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu;
munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
2 Landitseni kwa anthu ochita zoyipa
ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.
3 Onani momwe iwo akundibisalira!
Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane;
osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
4 Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo.
Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
5 Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,
dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse;
musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.
6 Iwo amabweranso madzulo
akuchita phokoso ngati agalu
ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
7 Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo;
iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo,
ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
8 Koma Inu Yehova, mumawaseka,
mumayinyoza mitundu yonseyo.
9 Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu;
Inu Mulungu, ndinu linga langa. 10 Mulungu wanga wachikondi.
Mulungu adzapita patsogolo panga
ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
11 Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu,
kuopa kuti anthu anga angayiwale.
Mwa mphamvu zanu,
lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
12 Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo
chifukwa cha mawu a milomo yawo,
iwo akodwe mʼkunyada kwawo.
Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
13 muwawononge mu ukali (wanu)
muwawononge mpaka atheretu.
Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi
kuti Mulungu amalamulira Yakobo.
14 Iwo amabweranso madzulo,
akuchita phokoso ngati agalu
ndi kumangoyenda mu mzinda.
15 Iwo amayendayenda kufuna chakudya
ndipo amawuwa ngati sanakhute.
16 Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu,
mmawa ndidzayimba zachikondi chanu;
pakuti ndinu linga langa,
pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.
17 Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu;
Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.
Abrahamu Analungamitsidwa Mwachikhulupiriro
4 Nanga tsono tidzati chiyani za Abrahamu kholo lathu, iyeyu anapezana ndi zotani pa nkhani imeneyi? 2 Kunena zoona, Abrahamu akanalungamitsidwa ndi ntchito zake, akanakhala nako kanthu kodzitamandira, koma osati pamaso pa Mulungu. 3 Kodi Malemba akuti chiyani? “Abrahamu anakhulupirira Mulungu, ndipo ichi chinamuchititsa kukhala wolungama.”
4 Tsopano munthu amene wagwira ntchito, malipiro ake satengedwa kukhala ngati mphatso koma zimene anayenera kulandira. 5 Koma kwa munthu amene sanagwire ntchito ndipo akhulupirira Mulungu amene amalungamitsa ochimwa, chikhulupiriro chakecho chimatengedwa kukhala chilungamo. 6 Davide ponena zomwezi pamene anayankhula za kudala kwa munthu amene Mulungu amulungamitsa osati chifukwa cha ntchito zake akuti,
7 “Odala ndi amene
zoyipa zawo zakhululukidwa;
amene machimo awo afafanizidwa.
8 Ngodala munthu amene
machimo ake Ambuye sadzawakumbukiranso.”
9 Kodi madalitso amenewa ali kwa ochita mdulidwe okha kapena kwa amene sanachitepo mdulidwe? Ife takhala tikunena kuti chikhulupiriro cha Abrahamu chinamuchititsa kukhala wolungama. 10 Kodi chinatengedwa bwanji? Kodi nʼkuti iye atachita mdulidwe kapena asanachite? Osati atachita mdulidwe koma asanachite! 11 Ndipo iye anachita mdulidwe ngati chizindikiro ndi chitsimikizo cha kulungama kumene anali nako mwachikhulupiriro pomwe anali asanachite mdulidwe. Choncho, iye ndi kholo la onse amene akhulupirira koma sanachite mdulidwe, ndi cholinga chakuti alungamitsidwe. 12 Ndipo iyenso ndiyenso kholo la ochita mdulidwe osati amene anangochita mdulidwe kokha koma amene amatsata chitsanzo cha chikhulupiriro chimene kholo lathu Abrahamu anali nacho asanachite mdulidwe.
13 Abrahamu ndi zidzukulu zake sanalandire lonjezano lakuti adzalandira dziko lapansi kudzera mu Malamulo, koma kudzera mu chilungamo chimene chimabwera ndi chikhulupiriro. 14 Pakuti ngati amene amadalira Malamulo ndiye olowa mʼmalo, ndiye kuti chikhulupiriro nʼchopanda pake ndipo lonjezano ndi lopanda phindu 15 chifukwa Malamulo anabweretsa chilango. Ndipo kumene kulibe Malamulo kulibenso kuwalakwitsa.
16 Motero, timalandira lonjezo mwachikhulupiriro. Laperekedwa mwachisomo kuti patsimikizidwe kuti lonjezolo liperekedwa kwa ana ndi zidzukulu zonse za Abrahamu, osati kwa iwo okha amene amatsatira Malamulo komanso kwa iwo amene ali ndi chikhulupiriro cha Abrahamu. Iye ndiye kholo la ife tonse. 17 Monga kwalembedwa kuti, “Ine ndakusandutsa kukhala kholo la mitundu yambiri.” Iye ndiye kholo lathu pamaso pa Mulungu, amene anamukhulupirira, Mulungu amene amapereka moyo kwa akufa ndipo amapereka moyo kwa zinthu zopanda moyo.
18 Ngakhale zinali zosayembekezeka, Abrahamu anakhulupirira ndi chiyembekezo kuti adzakhala kholo la mitundu yambiri. Izi ndi monga zinanenedwa kwa iye kuti, “Ndi mmene adzakhalire ana ako ndi zidzukulu zako.” 19 Iye sanafowoke mʼchikhulupiriro. Anadziwa choonadi cha thupi lake kuti linali lakufa popeza anali ndi zaka pafupifupi 100 ndiponso mimba ya Sara inali yowuma. 20 Komabe iye sanagwedezeke chifukwa chosakhulupirira pa zokhudzana ndi lonjezo la Mulungu. Iye analimbikitsidwa mʼchikhulupiriro chake ndi kupereka ulemerero kwa Mulungu. 21 Anatsimikiza mu mtima mwake kuti Mulungu anali ndi mphamvu yochita chomwe analonjeza. 22 Nʼchifukwa chake “chinamuchititsa kukhala wolungama.” 23 Mawu akuti, “chinatengedwa kwa iye” sanalembedwe chifukwa cha iye yekha, 24 komanso chifukwa ife amene Mulungu adzatiyesa olungama, ife amene tikhulupirira mwa Iye amene anamuukitsa kwa akufa, Yesu Ambuye athu. 25 Iye anaperekedwa kuti aphedwe chifukwa cha machimo athu ndipo anaukitsidwa ndi kukhala ndi moyo kuti tilungamitsidwe.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.