Old/New Testament
Yehova Ayankhula
38 Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
2 “Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga
poyankhula mawu opanda nzeru?
3 Onetsa chamuna;
ndikufunsa
ndipo undiyankhe.
4 “Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi?
Ndiwuze ngati ukudziwa.
5 Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa!
Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
6 Kodi maziko ake anawakumba potani,
kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
7 pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi
ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
8 “Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa,
pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
9 pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake
ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
10 pamene ndinayilembera malire ake
ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
11 Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire
apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
12 “Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa,
kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
13 kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi
ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
14 Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo;
zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
15 Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa,
ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
16 “Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja
kapena pa magwero ake ozama?
17 Kodi anakuonetsapo zipata za imfa?
Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
18 Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa?
Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
19 “Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti?
Nanga mdima umakhala kuti?
20 Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi?
Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
21 Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale!
Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
22 “Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana
kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
23 zimene ndazisungira nthawi ya mavuto
ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
24 Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani
kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
25 Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula,
nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
26 kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu,
chipululu chopandamo munthu,
27 kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa
ndi kumeretsamo udzu?
28 Kodi mvula ili ndi abambo ake?
Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
29 Kodi madzi owundana anawabereka ndani?
Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
30 pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala,
pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
31 “Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi?
Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
32 Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake
kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
33 Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa?
Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
34 “Kodi iwe ungathe kulamula mitambo
kuti igwetse mvula ya chigumula?
35 Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime?
Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
36 Kodi ndani anayika nzeru mu mtima,
ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
37 Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo?
Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
38 pamene fumbi limasanduka matope,
ndipo matopewo amawumbika?
39 “Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi
ndi kukhutitsa misona ya mikango
40 pamene ili khale mʼmapanga mwawo
kapena pamene ikubisala pa tchire?
41 Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani
pamene ana ake akulirira kwa Mulungu
ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?
39 “Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera?
Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere?
Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo;
pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo;
kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 “Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera?
Ndani amamasula zingwe zake?
6 Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake,
nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda;
ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu
ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 “Kodi njati ingavomere kukutumikira?
Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima?
Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake?
Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako
ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 “Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira,
koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi
ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa,
ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake;
Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 Chifukwa Mulungu anayimana nzeru,
simvetsa kanthu kalikonse.
18 Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga,
imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 “Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo
kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira,
ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake,
ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 Iye sachita mantha, saopa chilichonse;
sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake
pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha;
satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 Lipenga likalira amati, ‘Twee!’
Amamva fungo la nkhondo ali patali,
kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 “Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako,
ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka
ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku;
chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye;
maso ake amachionera patali chinthucho.
30 Ana ake amayamwa magazi,
ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”
40 Yehova anati kwa Yobu:
2 “Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse?
Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 “Ine sindili kanthu konse,
kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho,
ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 “Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna;
ndikufunsa mafunso
ndipo iwe undiyankhe.
8 “Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama?
Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu,
ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola,
ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 Tsanula ukali wako wosefukirawo,
uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse,
uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi;
ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 Ukatero Ine ndidzakuvomereza
kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 “Taganiza za mvuwu,
imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe,
ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri,
thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza;
mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa,
nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu,
komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 Imapeza chakudya chake ku mtunda
ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta,
imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta;
imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha,
iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza
kapena kuyikola mu msampha?
Timoteyo Atsagana ndi Paulo ndi Sila
16 Paulo anafika ku Derbe ndi Lusitra, kumene kumakhala ophunzira wina dzina lake Timoteyo. Amayi ake anali Myuda wokhulupirira, koma abambo ake anali Mgriki. 2 Abale a ku Lusitra ndi Ikoniya anamuchitira iye umboni wabwino. 3 Paulo anafuna kumutenga pa ulendo, kotero anachita mdulidwe chifukwa cha Ayuda amene amakhala mʼderalo pakuti onse amadziwa kuti abambo ake anali Mgriki. 4 Pamene amayenda mzinda ndi mzinda, amafotokoza zimene atumwi ndi akulu ampingo ku Yerusalemu anagwirizana kuti anthu azitsatire. 5 Kotero mipingo inalimbikitsidwa mʼchikhulupiriro ndipo anthu amachulukirachulukirabe tsiku ndi tsiku.
Paulo Awona Masomphenya
6 Paulo ndi anzake anadutsa mayiko a Frugiya ndi Galatiya, Mzimu Woyera atawaletsa kulalikira Mawu a Mulungu ku Asiya. 7 Atafika ku malire a Musiya, anayesa kulowa ku Bituniya, koma Mzimu wa Yesu sunawalole kutero. 8 Ndipo iwo anadutsa Musiya ndipo anapita ku Trowa. 9 Nthawi ya usiku Paulo anaona masomphenya, munthu wa ku Makedoniya atayimirira ndi kumupempha kuti, “Bwerani ku Makedoniya, mudzatithandize.” 10 Paulo ataona masomphenyawa, tinakonzeka kupita ku Makedoniya, kutsimikiza kuti Mulungu anatiyitana kuti tikalalikire Uthenga Wabwino.
Lidia Atembenuka Mtima ku Filipi
11 Kuchokera ku Trowa tinakwera sitima ya pamadzi kupita ku Samotrake ndipo mmawa mwake tinapitirira mpaka ku Neapoli. 12 Kuchokera kumeneko tinapita ku Filipi, boma la Aroma ndiponso mzinda waukulu wa dera la Makedoniya. Tinakhala kumeneko masiku owerengeka.
13 Pa tsiku la Sabata tinatuluka mu mzindawo kupita ku mtsinje kumene timayembekezera kukapeza malo opempherera. Tinakhala pansi ndipo tinayamba kuyankhula ndi amayi amene anasonkhana pamenepo. 14 Mmodzi wa amayi amene amamvetserawo ndi Lidiya amene amagulitsa nsalu zofiira, wochokera ku mzinda wa Tiyatira, ndipo amapembedza Mulungu. Ambuye anatsekula mtima wake kuti amve mawu a Paulo. 15 Iye ndi a mʼbanja lake atabatizidwa, anatiyitana kuti tipite ku nyumba yake. Iye anati, “Ngati mwanditenga ine kukhala wokhulupirira mwa Ambuye, bwerani mudzakhale mʼnyumba mwanga.” Ndipo anatiwumiriza ife kwambiri.
Paulo ndi Sila Mʼndende
16 Tsiku lina pamene timapita kumalo wopempherera, tinakumana ndi mtsikana wina amene anali ndi mzimu woyipa umene umanena zamʼtsogolo. Iye amapezera ndalama zambiri ambuye ake pa ulosi wake. 17 Mtsikanayu anatsatira Paulo ndi ife, akufuwula kuti, “Anthu awa ndi atumiki a Mulungu Wammwambamwamba, amene akukuwuzani inu njira yachipulumutso.” 18 Iye anachita izi masiku ambiri. Kenaka Paulo anavutika mu mtima, natembenuka ndipo anati kwa mzimuwo, “Ndikukulamula iwe mʼdzina la Yesu Khristu kuti utuluke mwa iye!” Nthawi yomweyo mzimuwo unatuluka.
19 Pamene ambuye a mtsikana uja anazindikira kuti chiyembekezo chawo chopezera ndalama chatha, anagwira Paulo ndi Sila nawakokera ku bwalo la akulu. 20 Anawabweretsa iwo kwa oweruza milandu ndipo anati, “Anthu awa ndi Ayuda, iwo akuvutitsa mu mzinda wathu. 21 Ndipo akuphunzitsa miyambo imene ife Aroma sitiloledwa kuyilandira kapena kuyichita.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.