Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Chronological

Read the Bible in the chronological order in which its stories and events occurred.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Zefaniya 1-3

Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.

Yehova Adzaweruza Dziko Lapansi

“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse
    pa dziko lapansi,”
            akutero Yehova.
“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe;
    ndidzawononga mbalame zamlengalenga
    ndi nsomba za mʼnyanja.
Ndidzawononga anthu oyipa,
    ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,”
            akutero Yehova.

Chenjezo kwa Yuda

Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda
    ndi onse okhala mu Yerusalemu.
Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala,
    mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
amene amagwada pa madenga a nyumba zawo
    kupembedza zolengedwa zamumlengalenga,
amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova,
    komanso mʼdzina la Moleki,
amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova,
    osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova,
    chifukwa tsiku la Yehova layandikira.
Yehova wakonzekera kupereka nsembe;
    wapatula iwo amene wawayitana.
Pa tsiku la nsembe ya Yehova
    ndidzalanga akalonga
    ndi ana aamuna a mfumu
ndi onse amene amavala
    zovala zachilendo.
Pa tsiku limenelo ndidzalanga
    onse amene safuna kuponda pa chiwundo,
amene amadzaza nyumba ya ambuye awo
    ndi chiwawa ndi chinyengo.

10 “Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova,
    “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba,
    kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano,
    ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
11 Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika;
    a malonda anu onse adzapululidwa,
    ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
12 Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale
    ndi kulanga onse amene sakulabadira,
    amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa,
amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse,
    chabwino kaya choyipa.’
13 Chuma chawo chidzafunkhidwa,
    nyumba zawo zidzagwetsedwa.
Adzamanga nyumba,
    koma osakhalamo;
adzadzala minda ya mpesa
    koma sadzamwako vinyo wake.”

Tsiku Lalikulu la Yehova

14 Tsiku lalikulu la Yehova layandikira,
    layandikira ndipo lifika msanga.
Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa,
    ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
15 Tsiku limenelo lidzakhala la ukali,
    tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni,
tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko,
    tsiku la mdima ndi lachisoni,
    tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
16 Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo,
    tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa
    ndi nsanja za pa ngodya.
17 Ndidzabweretsa msautso pa anthu
    ndipo adzayenda ngati anthu osaona,
    chifukwa achimwira Yehova,
magazi awo adzamwazika ngati fumbi
    ndi mnofu wawo ngati ndowe.
18 Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo
    sadzatha kuwapulumutsa
    pa tsiku la ukali wa Yehova.
Dziko lonse lapansi lidzanyeka
    mʼmoto wa nsanje yake
chifukwa adzakantha modzidzimutsa
    onse okhala pa dziko lapansi.
Sonkhanani pamodzi, sonkhanani pamodzi,
    inu mtundu wochititsa manyazi,
isanafike nthawi yachiweruzo,
    nthawi yanu isanawuluke ngati mungu,
usanakufikeni mkwiyo woopsa wa Yehova,
    tsiku la ukali wa Yehova lisanafike pa inu.
Funafunani Yehova, inu nonse odzichepetsa a mʼdziko,
    inu amene mumachita zimene amakulamulani.
Funafunani chilungamo, funafunani kudzichepetsa;
    mwina mudzatetezedwa
    pa tsiku la mkwiyo wa Yehova.

Za Afilisti

Gaza adzasiyidwa
    ndipo Asikeloni adzasanduka bwinja.
Nthawi yamasana Asidodi adzakhala wopanda anthu
    ndipo Ekroni adzazulidwa.
Tsoka inu okhala mʼmbali mwa nyanja,
    inu mtundu wa Akereti;
mawu a Yehova akutsutsa
    iwe Kanaani, dziko la Afilisti.
“Ndidzakuwononga
    ndipo palibe amene adzatsale.”

Dziko la mʼmbali mwa nyanja, kumene kumakhala Akereti,
    lidzakhala malo a abusa ndi la makola a nkhosa.
Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda;
    adzapezako msipu.
Nthawi ya madzulo adzagona
    mʼnyumba za Asikeloni.
Yehova Mulungu wawo adzawasamalira;
    adzabwezeretsa mtendere wawo.

Za Mowabu ndi Amoni

“Ndamva kunyoza kwa Mowabu
    ndi chipongwe cha Amoni,
amene ananyoza anthu anga
    ndi kuopseza kuti alanda dziko lawo.
Choncho, pali Ine Wamoyo,”
    akutero Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,
“Ndithu, Mowabu adzasanduka ngati Sodomu,
    Amoni adzasanduka ngati Gomora;
malo a zomeramera ndi maenje a mchere,
    dziko la bwinja mpaka muyaya.
Anthu anga otsala adzawafunkha;
    opulumuka a mtundu wanga adzalandira dziko lawo.”

10 Ichi ndi chimene adzalandire chifukwa cha kunyada kwawo,
    chifukwa chonyoza ndi kuchitira chipongwe anthu a Yehova Wamphamvuzonse.
11 Yehova adzawachititsa mantha kwambiri
    pamene adzawononga milungu yonse ya mʼdzikomo.
Ndipo mitundu ya anthu pa dziko lonse idzamulambira,
    uliwonse ku dziko la kwawo.

Za Kusi

12 “Inunso anthu a ku Kusi,
    mudzaphedwa ndi lupanga.”

Za Asiriya

13 Yehova adzatambasulira dzanja lake kumpoto
    ndi kuwononga Asiriya,
kusiya Ninive atawonongekeratu
    ndi owuma ngati chipululu.
14 Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko,
    pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse.
Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu
    adzakhala pa nsanamira zake.
Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera,
    mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha,
    nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.
15 Umenewu ndiye mzinda wosasamala
    umene kale unali wotetezedwa.
Unkanena kuti mu mtima mwake,
    “Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.”
Taonani lero wasanduka bwinja,
    kokhala nyama zakutchire!
Onse owudutsa akuwunyoza
    ndi kupukusa mitu yawo.

Tsogolo la Yerusalemu

Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza,
    owukira ndi odetsedwa!
Sumvera aliyense,
    sulandira chidzudzulo.
Sumadalira Yehova,
    suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma,
    olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo,
    zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
Aneneri ake ndi odzikuza;
    anthu achinyengo.
Ansembe ake amadetsa malo opatulika
    ndipo amaphwanya lamulo.
Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama;
    Iye salakwa.
Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama,
    ndipo tsiku lililonse salephera,
    komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
“Ndachotseratu mitundu ya anthu;
    ndagwetsa malinga awo.
Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo,
    popanda aliyense wodutsa.
Mizinda yawo yawonongedwa;
    palibe aliyense adzatsalemo.
Ndinati,
    ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa
    ndi kumvera kudzudzula kwanga!’
Ndipo sindidzawononga nyumba zawo,
    kapena kuwalanganso.
Koma iwo anali okonzeka
    kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
Choncho mundidikire,” akutero Yehova,
    “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni.
Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu,
    kusonkhanitsa maufumu
ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo;
    mkwiyo wanga wonse woopsa.
Dziko lonse lidzatenthedwa
    ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.

“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse
    kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova
    ndi kumutumikira Iye pamodzi.
10 Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi
    anthu anga ondipembedza, omwazikana,
    adzandibweretsera zopereka.
11 Tsiku limenelo simudzachita manyazi
    chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira,
popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu
    amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo.
Simudzakhalanso odzikuza
    mʼphiri langa lopatulika.
12 Koma ndidzasiya pakati panu
    anthu ofatsa ndi odzichepetsa,
    amene amadalira dzina la Yehova.
13 Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika;
    sadzayankhulanso zonama,
    ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo.
Adzadya ndi kugona
    ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”

14 Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni;
    fuwula mokweza, iwe Israeli!
Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse,
    iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
15 Yehova wachotsa chilango chako,
    wabweza mdani wako.
Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako;
    sudzaopanso chilichonse.
16 Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti,
    “Usaope, iwe Ziyoni;
    usafowoke.
17 Yehova Mulungu wako ali pakati pako,
    ali ndi mphamvu yopulumutsa.
Adzakondwera kwambiri mwa iwe,
    adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake,
    adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”

18 “Ndidzakuchotserani zowawa
    za pa zikondwerero zoyikika;
    nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
19 Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi
    onse amene anakuponderezani;
ndidzapulumutsa olumala
    ndi kusonkhanitsa amene anamwazika.
Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu
    mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
20 Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani;
    pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu.
Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu
    pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi
pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu
    inu mukuona,”
            akutero Yehova.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.