Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Chronological

Read the Bible in the chronological order in which its stories and events occurred.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Ezekieli 18-19

Munthu Wochimwa Adzafa

18 Yehova anandiyankhula nati: “Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti:

“ ‘Nkhuyu zodya akulu zimapota
    ndi ana omwe?’ ”

“Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli. Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.

“Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama
    amene amachita zolungama ndi zolondola.
Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo
    kapena kupembedza mafano a Aisraeli.
Iye sayipitsa mkazi wa mnzake
    kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
Iye sapondereza munthu wina aliyense,
    koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake.
Iye salanda zinthu za osauka,
    koma amapereka chakudya kwa anthu anjala,
    ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira,
    kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu.
Amadziletsa kuchita zoyipa
    ndipo sakondera poweruza milandu.
Iye amatsatira malangizo anga,
    ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika.
Munthu ameneyo ndi wolungama;
    iye adzakhala ndithu ndi moyo,
            akutero Ambuye Yehova.

10 “Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere. 11 Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo.

“Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo.
Amayipitsa mkazi wa mnzake.
12 Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa.
Amalanda zinthu za osauka.
Sabweza chikole cha munthu wa ngongole.
Iye amatembenukira ku mafano
nachita zonyansa.
13 Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu.

Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.

14 “Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.

15 “Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo.
    Sapembedza mafano a ku Israeli.
Sayipitsa mkazi wa mnzake.
16 Sapondereza munthu wina aliyense.
    Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka.
Salanda zinthu za munthu.
    Amapereka chakudya kwa anthu anjala.
    Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
17 Amadziletsa kuchita zoyipa.
    Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja.
Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga.

Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu. 18 Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.

19 “Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse. 20 Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.

21 “ ‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi. 22 Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo. 23 Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.

24 “ ‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.

25 “Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama? 26 Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo. 27 Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake. 28 Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa. 29 Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?

30 “Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo. 31 Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli? 32 Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”

Nyimbo ya Maliro a Akalonga a Israeli

19 “Imba nyimbo ya madandawulo, kuyimbira akalonga a ku Israeli. Uzinena kuti,

“ ‘Amayi ako anali ndani?
    Anali ngati mkango waukazi!
Iwo unabwatama pakati pa mikango yayimuna;
    unkalera ana ake pakati pa misona.
Unalera mmodzi mwa ana ake,
    ndipo mwanayo anasanduka mkango wamphamvu.
Unaphunzira kugwira nyama,
    ndipo unayamba kudya anthu.
Anthu amitundu anamva za mkangowo,
    ndipo tsiku lina unagwa mʼmbuna mwawo.
Iwo anawukoka ndi ngowe
    kupita nawo ku dziko la Igupto.

“ ‘Amayi aja ataona kuti mwana ankamukhulupirira uja wagwidwa ndi kuti chiyembekezo chake chapita padera,
amayiwo anatenganso mwana wina
    namusandutsa mkango wamphamvu.
Unkayendayenda pakati pa mikango inzake,
    pakuti tsopano unali mkango wamphamvu.
Unaphunzira kugwira nyama
    ndipo unayamba kudya anthu.
Unagwetsa malinga awo,
    ndikuwononga mizinda yawo.
Onse a mʼdzikomo
    anachita mantha chifukwa cha kubangula kwake.
Pamenepo mitundu ya anthu, makamaka ochokera madera ozungulira,
    inabwera kudzalimbana nawo.
Anawutchera ukonde wawo,
    ndipo tsiku lina unagwera mʼmbuna mwawo.
Anawukoka ndi ngowe nawuponya mʼchitatanga.
    Anabwera nawo kwa mfumu ya ku Babuloni
ndipo mfumuyo inawuponya mʼndende
    ndi cholinga choti liwu lake lisamamvekenso
    ku mapiri a Israeli.

10 “ ‘Amayi ako anali ngati mpesa mʼmunda wamphesa
    wodzalidwa mʼmbali mwa madzi.
Unabereka bwino ndipo unali ndi nthambi zambiri
    chifukwa cha kuchuluka kwa madzi.
11 Nthambi zake zinali zolimba,
    zoyenera kupangira ndodo yaufumu.
Unatalika nusomphoka pakati pa
    zomera zina.
Unkaoneka bwino chifukwa cha kutalika kwake,
    ndi nthambi zake zambiri.
12 Koma unazulidwa mwaukali
    ndipo unagwetsedwa pansi.
Unawuma ndi mphepo ya kummawa,
    zipatso zake zinayoyoka;
nthambi zake zolimba zinafota
    ndipo moto unapsereza mtengo wonse.
13 Ndipo tsopano anawuwokeranso ku chipululu,
    dziko lowuma ndi lopanda madzi.
14 Moto unatulukanso mu mtengomo
    ndi kupsereza nthambi ndi zipatso zake.
Palibe nthambi yolimba inatsala pa mtengowo
    yoyenera kupangira ndodo yaufumu.

Imeneyi ndi nyimbo yachisoni ndipo yasanduka nyimbo ya pa maliro.’ ”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.