Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Chronological

Read the Bible in the chronological order in which its stories and events occurred.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Obadiya

Masomphenya a Obadiya

Masomphenya a Obadiya.

Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti,

Tamva uthenga wochokera kwa Yehova:
    Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti,
“Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”

“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina;
    udzanyozedwa kwambiri.
Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,
    iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe
    ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali,
iwe amene umanena mu mtima mwako kuti,
    ‘Ndani anganditsitse pansi?’
Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga
    ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi,
    ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”
            akutero Yehova.
“Anthu akuba akanabwera kwa iwe,
    kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku,
aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe!
    Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
Ngati anthu othyola mphesa akanafika,
    kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse,
    chuma chake chobisika chidzabedwa!
Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire;
    abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa;
amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha,
    koma iwe sudzazindikira zimenezi.”

Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo,
    kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu,
    anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?
Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha,
    ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau
    adzaphedwa pa nkhondo.
10 Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo,
    udzakhala wamanyazi;
    adzakuwononga mpaka muyaya.
11 Pamene adani
    ankamulanda chuma chake
pamene alendo analowa pa zipata zake
    ndi kuchita maere pa Yerusalemu,
    pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.
12 Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako
    pa nthawi ya tsoka lake,
kapena kunyogodola Ayuda
    chifukwa cha chiwonongeko chawo,
kapena kuwaseka pa nthawi ya
    mavuto awo.
13 Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga
    pa nthawi ya masautso awo,
kapena kuwanyogodola
    pa tsiku la tsoka lawo,
kapena kulanda chuma chawo
    pa nthawi ya masautso awo.
14 Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu
    kuti uphe Ayuda othawa,
kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka
    pa nthawi ya mavuto awo.”

15 “Tsiku la Yehova layandikira
    limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu.
Adzakuchitira zomwe unawachitira ena;
    zochita zako zidzakubwerera wekha.
16 Iwe unamwa pa phiri langa loyera,
    koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza;
iwo adzamwa ndi kudzandira
    ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
17 Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso;
    phirilo lidzakhala lopatulika,
ndipo nyumba ya Yakobo
    idzalandira cholowa chake.
18 Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto
    ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto;
nyumba ya Esau idzasanduka chiputu,
    ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza.
Sipadzakhala anthu opulumuka
    kuchokera mʼnyumba ya Esau.”
            Yehova wayankhula.

19 Anthu ochokera ku Negevi adzakhala
    ku mapiri a Esau,
ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri
    adzatenga dziko la Afilisti.
Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya,
    ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
20 Aisraeli amene ali ku ukapolo
    adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati;
a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi
    adzalandira mizinda ya ku Negevi.
21 Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni
    ndipo adzalamulira mapiri a Esau.
    Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.

Masalimo 82-83

Salimo la Asafu.

82 Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu;
    Iye akuweruza pakati pa “milungu.”

“Mudzateteza osalungama mpaka liti,
    ndi kukondera anthu oyipa?
Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye;
    mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
Landitsani anthu ofowoka ndi osowa;
    apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.

“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse.
    Amayendayenda mu mdima;
    maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu,
    nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
Koma mudzafa ngati anthu wamba;
    mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”

Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi,
    pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.

Nyimbo. Salimo la Asafu.

83 Inu Mulungu musakhale chete;
    musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
Onani adani anu akuchita chiwawa,
    amene amadana nanu autsa mitu yawo.
Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu;
    Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu
    kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”

Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu;
    Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
Matenti a Edomu ndi Aismaeli,
    Mowabu ndi Ahagiri,
Agebala, Aamoni ndi Aamaleki,
    Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo
    kupereka mphamvu kwa ana a Loti.
            Sela

Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani,
    monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
10 Amene anawonongedwa ku Endori
    ndi kukhala ngati zinyalala.
11 Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu
    ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
12 amene anati, “Tiyeni tilande dziko
    la msipu la Mulungu.”

13 Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga,
    ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
14 Monga moto umatentha nkhalango,
    kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
15 kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho,
    ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
16 Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi
    kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.

17 Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse;
    awonongeke mwa manyazi.
18 Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova,
    ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.