Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
Salimo la Asafu.
50 Wamphamvuyo, Yehova Mulungu,
akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi
kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri
Mulungu akuwala.
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete;
moto ukunyeketsa patsogolo pake,
ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga
ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga,
amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake,
pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula,
iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa;
ndine Mulungu, Mulungu wako.
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako,
kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu
kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza,
ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse
chipulumutso cha Mulungu.”
18 Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto;
moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga,
umayatsa nkhalango yowirira,
ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.
19 Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse,
dziko lidzatenthedwa
ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto;
palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.
20 Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya,
koma adzakhalabe ndi njala;
kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya,
koma sadzakhuta.
Aliyense azidzadya ana ake omwe.
21 Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase;
onsewa pamodzi adzadya Yuda.
Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere,
mkono wake uli chitambasulire.
10 Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo,
kwa iwo amene amalemba zongovutitsa anzawo,
2 kuwalanda anthu osauka ufulu wawo
ndi kumana chilungamo osautsidwa pakati pa anthu anga,
amalanda zinthu za akazi amasiye
ndi kubera ana amasiye.
3 Kodi mudzatani pa tsiku la chilango,
pofika chiwonongeko chochokera kutali?
Kodi mudzathawira kwa yani kuti akuthandizeni?
Nanga chuma chanu mudzachisiya kuti?
4 Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa
kapena kufa pamodzi ndi ophedwa.
Komabe pa zonsezi mkwiyo wake sunawachokere,
mkono wake uli chitambasulire.
Mawu a Stefano
7 Kenaka mkulu wa ansembe anafunsa Stefano kuti, “Kodi zimene akukunenerazi ndi zoona?”
2 Stefano anayankha kuti, “Abale ndi makolo, tamverani! Mulungu waulemerero anaoneka kwa kholo lathu Abrahamu pamene ankakhala ku Mesopotamiya, asanakakhale ku Harani. 3 Mulungu anati, ‘Tuluka mʼdziko lako, siya abale ako, ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.’
4 “Ndipo iye anatulukadi mʼdziko la Akaldeya ndi kukakhala ku Harani. Atamwalira abambo ake, Mulungu anamuchotsa kumeneko ndi kumubweretsa mʼdziko lino limene inu mukukhalamo tsopano. 5 Mulungu sanamupatse cholowa kuno, ngakhale kadera kakangʼono kadziko. Koma Mulungu anamulonjeza kuti adzapereka dziko lino kwa iye ndi kwa zidzukulu zake, ngakhale kuti pa nthawi imeneyi analibe mwana. 6 Mulungu anayankhula motere kwa iye: ‘Zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo, ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.’ 7 Mulungu anati, ‘Ine ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo, ndipo pambuyo pake akadzatuluka mʼdzikolo adzandipembedza Ine pamalo pano.’ 8 Kenaka Mulungu anachita pangano la mdulidwe ndi Abrahamu. Ndipo Abrahamu, anabereka Isake, namudula ali ndi masiku asanu ndi atatu. Ndipo Isake anabereka Yakobo, Yakobo anabereka makolo khumi ndi awiri aja.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.