Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 85

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.

85 Yehova munakomera mtima dziko lanu;
    munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
Munakhululukira mphulupulu za anthu anu
    ndi kuphimba machimo awo onse.
            Sela
Munayika pambali ukali wanu wonse
    ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.

Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,
    ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
Kodi mudzatikwiyira mpaka liti?
    Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
Kodi simudzatitsitsimutsanso,
    kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova,
    ndipo tipatseni chipulumutso chanu.

Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena;
    Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake,
    koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye,
    kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.

10 Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi;
    chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi,
    ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino,
    ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
13 Wolungama amapita patsogolo pake
    ndi kukonza njira za mapazi ake.

Hoseya 5

Chiweruzo cha Israeli

“Ansembe inu, imvani izi!
    Inu Aisraeli, tcherani khutu!
Inu nyumba yaufumu, mvetserani!
    Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu:
Inu munali ngati msampha ku Mizipa,
    munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
Owukira azama mʼmoyo wakupha,
    Ine ndidzawalanga onsewo.
Ndimadziwa zonse za Efereimu;
    Aisraeli ndi osabisika kwa Ine.
Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere;
    Israeli wadziyipitsa.

“Ntchito zawo siziwalola
    kubwerera kwa Mulungu wawo.
Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere;
    Iwo sadziwa Yehova.
Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa;
    Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo;
    Yudanso anagwa nawo pamodzi.
Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo
    kukapereka nsembe kwa Yehova,
iwo sadzamupeza;
    Iye wawachokera.
Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova;
    amabereka ana amʼchigololo
ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano
    chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.

“Womba lipenga mu Gibeya,
    liza mbetete mu Rama.
Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni;
    iwe Benjamini tsogolera.
Efereimu adzasanduka bwinja
    pa tsiku la chilango.
Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi
    pakati pa mafuko a Israeli.
10 Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu
    amene amasuntha miyala ya mʼmalire.
Ndidzawakhutulira ukali wanga
    ngati madzi a chigumula.
11 Efereimu waponderezedwa,
    akulangidwa chifukwa chotsatira
    mafano.
12 Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu,
    ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.

13 “Efereimu ataona nthenda yake,
    ndi Yuda ataona zilonda zake,
pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya,
    ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza.
Koma mfumuyo singathe kukuchizani,
    singathe kuchiritsa mabala anu.
14 Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu.
    Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda.
Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo;
    ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
15 Ndipo ndidzabwerera ku malo anga
    mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo.
Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga;
    mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”

Machitidwe a Atumwi 2:22-36

22 “Inu Aisraeli mverani mawu awa; Yesu wa ku Nazareti anali munthu amene anaperekedwa kwa inu ndi Mulungu. Ndipo Mulungu anakutsimikizirani zimenezi ndi zamphamvu, zodabwitsa ndi zizindikiro zimene anachita mwa Iye pakati panu, monga inu mukudziwa. 23 Yesu ameneyu anaperekedwa kwa inu mwa kufuna ndi kudziwiratu kwa Mulungu; ndipo inu mothandizidwa ndi anthu oyipa, munamupha Iye pomupachika pa mtanda. 24 Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa, kumumasula Iye ku zowawa za imfa, chifukwa kunali kosatheka kuti agwiridwe ndi imfa. 25 Pakuti Davide ananena za Iye kuti,

“ ‘Ndinaona Ambuye pamaso panga nthawi zonse.
    Chifukwa Iye ali kudzanja langa lamanja,
    Ine sindidzagwedezeka.
26 Chifukwa chake mtima wanga ndi wokondwa ndipo lilime langa likukondwera;
    thupi langanso lidzakhala ndi chiyembekezo.
27 Chifukwa simudzasiya moyo wanga kumalo a anthu akufa, ku manda,
    kapena kulekerera Woyerayo kuti awole.
28 Inu munandidziwitsa ine njira zamoyo;
    Inu mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu.’

29 “Abale, ine ndikuwuzani motsimikiza kuti kholo lathu Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda, ndipo manda ake alipo lero lino. 30 Koma iye anali mneneri ndipo anadziwa kuti Mulungu analonjeza ndi lumbiro kuti adzayika mmodzi wa zidzukulu zake pa mpando waufumu. 31 Davide ataoneratu zimene zinali mʼtsogolo anayankhula za kuuka kwa Khristu, kuti Iye sanasiyidwe mʼmanda, ndipo thupi lake silinawole. 32 Mulungu wamuukitsa Yesu ameneyu, ndipo ife ndife mboni za zimenezi. 33 Khristu anakwezedwa kukhala kudzanja lamanja la Mulungu, nalandira Mzimu Woyera amene Atate anamulonjeza, ndipo watipatsa ife zimene mukuona ndi kumvazi. 34 Pakuti si Davide anakwera kumwamba koma iye akuti,

“ ‘Ambuye anawuza Ambuye anga kuti:
    Khala kudzanja langa lamanja
35 mpaka nditasandutsa adani ako
    kukhala chopondapo mapazi ako.’

36 “Nʼchifukwa chake, Aisraeli onse adziwe ndithu kuti, Yesu amene inu munamupachika, Mulungu wamuyika kukhala Ambuye ndiponso Mpulumutsi.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.