Revised Common Lectionary (Semicontinuous)
7 Yehova akuti,
“Imbani mosangalala chifukwa cha Yakobo,
fuwulani chifukwa cha mtundu wopambana mitundu yonse.
Matamando anu amveke, ndipo munene kuti,
‘Yehova wapulumutsa anthu ake
otsala a Israeli.’
8 Taonani, ndidzabwera nawo kuchokera ku dziko la kumpoto,
ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku malekezero a dziko lapansi.
Anthu osaona, olumala, amayi oyembekezera
ndi amene ali pa nthawi yawo yochira adzabwera nawo pamodzi.
Chidzakhala chikhamu cha anthu obwerera kuno.
9 Adzabwera akulira;
koma Ine ndikuwatonthoza mtima, ndidzawaperekeza.
Ndidzawatsogolera ku mitsinje yamadzi
mʼnjira yosalala mmene sadzapunthwamo.
Chifukwa ndine abambo ake a Israeli,
ndipo Efereimu ndi mwana wanga woyamba.
10 “Imvani mawu a Yehova inu anthu a mitundu ina;
lalikirani mawuwa kwa anthu a mayiko akutali a mʼmbali mwa nyanja;
‘Iye amene anabalalitsa Israeli adzawasonkhanitsanso
ndipo adzayangʼanira nkhosa zake ngati mʼbusa.’
11 Pakuti Yehova wawombola fuko la Yakobo
anawapulumutsa mʼdzanja la anthu owaposa mphamvu.
12 Anthuwo adzabwera akuyimba mofuwula pa mapiri a Ziyoni;
adzasangalala ndi zinthu zabwino zochokera kwa Yehova.
Zinthu zabwinozo ndi izi: tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta,
ana ankhosa ndi ana angʼombe.
Iwo adzakhala ngati munda wothiriridwa bwino,
ndipo sadzamvanso chisoni.
13 Pamenepo anamwali adzavina ndi kusangalala.
Anyamata ndi okalamba nawonso adzasangalala.
Kulira kwawo ndidzakusandutsa chisangalalo;
ndidzawasangalatsa nʼkuchotsa chisoni chawo.
14 Ansembe ndidzawadyetsa chakudya chabwino,
ndipo anthu anga adzakhuta ndi zabwino zanga,”
akutero Yehova.
12 Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu;
tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
13 pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako
ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
14 Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako
ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
15 Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi;
mawu ake amayenda mwaliwiro.
16 Amagwetsa chisanu ngati ubweya
ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
17 Amagwetsa matalala ngati miyala.
Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
18 Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka;
amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
19 Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo,
malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
20 Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu;
anthu enawo sadziwa malamulo ake.
Tamandani Yehova.
Madalitso Auzimu mwa Khristu
3 Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, amene anatipatsa madalitso onse a uzimu kumwamba mwa Khristu. 4 Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake, 5 Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake. 6 Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda. 7 Mwa Yesu Khristu, chifukwa cha magazi ake, ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo athu molingana ndi kuchuluka kwa chisomo cha Mulungu 8 chimene anatipatsa mosawumira. Mwa nzeru zonse ndi chidziwitso, 9 Iye watiwululira chifuniro chake chimene chinali chobisika, chimene anachikonzeratu mwa Khristu, molingana ndi kukoma mtima kwake. 10 Chimene anakonza kuti chichitike nʼchakuti, ikakwana nthawi yake asonkhanitsa pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za kumwamba ndi pa dziko lapansi.
11 Iye anatisankhiratu mwa Khristu, atatikonzeratu molingana ndi machitidwe a Iye amene amachititsa zinthu zonse kuti zikwaniritse cholinga cha chifuniro chake, 12 nʼcholinga chakuti, ife amene tinali oyamba kukhala ndi chiyembekezo mwa Khristu, tiyamike ulemerero wake. 13 Ndipo inunso pamene munamva mawu a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, munayikidwanso mwa Khristu. Mutakhulupirira, anakusindikizani chizindikiro pokupatsani Mzimu Woyera amene Iye analonjeza. 14 Mzimu Woyerayo ndi chikole chotsimikizira kuti tidzalandira madalitso athu, ndipo kuti Mulungu anatiwombola kuti tikhale anthu ake. Iye anachita zimenezi kuti timuyamike ndi kumulemekeza.
Mawu Asandulika Thupi
1 Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu. 2 Mawuwa anali ndi Mulungu pachiyambi.
3 Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa. 4 Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu. 5 Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.
6 Kunabwera munthu amene anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu; Iyeyo dzina lake linali Yohane. 7 Iye anabwera ngati mboni kudzachitira umboni kuwunikako kuti kudzera mwa iye anthu onse akhulupirire. 8 Iyeyu sanali kuwunika; koma anabwera ngati mboni ya kuwunika. 9 Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.
10 Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye. 11 Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye. 12 Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu; 13 ana wobadwa osati monga mwachilengedwe, kapena chisankho cha munthu, kapena chifuniro cha mwamuna koma wobadwa mwa Mulungu.
14 Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.
15 Yohane achitira umboni za Iye. Iye akufuwula kuti, “Uyu ndi Iye amene ndinati, ‘Iye amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa, Iyeyo analipo ine ndisanabadwe.’ ” 16 Kuchokera mʼkuchuluka kwa chisomo chake ife tonse talandira madalitso pamwamba pa madalitso. 17 Pakuti lamulo linapatsidwa kudzera mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinabwera kudzera mwa Yesu Khristu. 18 Palibe munthu amene anaona Mulungu, koma Mwana mmodzi yekhayo amene ali wa pamtima pa Atate, ndiye anafotokoza za Iye.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.