Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Revised Common Lectionary (Semicontinuous)

Daily Bible readings that follow the church liturgical year, with sequential stories told across multiple weeks.
Duration: 1245 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 110

Salimo la Davide.

110 Yehova akuwuza Mbuye wanga kuti,
    “Khala ku dzanja langa lamanja
mpaka nditasandutsa adani ako
    kukhala chopondapo mapazi ako.”

Yehova adzakuza ndodo yamphamvu ya ufumu wako kuchokera mʼZiyoni;
    udzalamulira pakati pa adani ako.
Ankhondo ako adzakhala odzipereka
    pa tsiku lako la nkhondo.
Atavala chiyero chaulemerero,
    kuchokera mʼmimba ya mʼbandakucha,
    udzalandira mame a unyamata wako.

Yehova walumbira
    ndipo sadzasintha maganizo ake:
“Ndiwe wansembe mpaka muyaya
    monga mwa unsembe wa Melikizedeki.”

Ambuye ali kudzanja lako lamanja;
    Iye adzaponda mafumu pa tsiku la ukali wake.
Adzaweruza anthu a mitundu ina,
    adzadzaza dziko lapansi ndi mitembo ndipo adzaphwanya olamulira a pa dziko lonse lapansi.
Iye adzamwa mu mtsinje wa mʼmbali mwa njira;
    choncho adzaweramutsa mutu wake.

Miyambo 3:1-12

Phindu Lina la Nzeru

Mwana wanga, usayiwale malangizo anga,
    mtima wako usunge malamulo anga.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka
    ndipo udzakhala pa mtendere.

Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere.
    Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda
    ndi kuwalemba pa mtima pako.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino
    pamaso pa Mulungu ndi anthu.

Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse
    ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo,
    ndipo Iye adzawongola njira zako.

Usamadzione ngati wa nzeru.
    Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino
    ndi mafupa ako adzakhala olimba.

Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse;
    zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri,
    ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.

11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova,
    ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda,
    monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.

Yakobo 4:11-17

11 Abale musamanenane. Aliyense wonenera zoyipa mʼbale wake kapena kumuweruza, akusinjirira ndi kuweruza Malamulo. Pamene muweruza malamulo, ndiye kuti simukusunga malamulowo, koma mukuwaweruza. 12 Pali mmodzi yekha Wopereka Malamulo ndi Woweruza. Ndiye amene akhoza kupulumutsa ndi kuwononga. Kodi ndiwe yani kuti uziweruza mnzako?

Kunyadira za Mawa

13 Tsono tamverani, inu amene mumati, “Lero kapena mawa tipita ku mzinda wakutiwakuti, tikatha chaka chimodzi tikuchita malonda ndi kupanga ndalama.” 14 Chifukwa chiyani mukutero? Inu simukudziwa zimene ziti zichitike mawa. Kodi moyo wanu ndi wotani? Inu muli ngati nkhungu imene imangooneka kwa kanthawi kochepa ndipo kenaka ndikuzimirira. 15 Koma inuyo muyenera kunena kuti, “Ambuye akalola, tikadzakhala ndi moyo, tidzachita zakutizakuti.” 16 Koma mmene zililimu mumangodzitama ndi kudzikuza. Kudzitama konse kotereku ndi koyipa. 17 Aliyense amene amadziwa zabwino zimene amayenera kuchita koma osazichita, ndiye kuti wachimwa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.