Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Beginning

Read the Bible from start to finish, from Genesis to Revelation.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Yobu 1-4

Mawu Oyamba

Mʼdziko la Uzi munali munthu wina, dzina lake Yobu. Munthu ameneyu anali wosalakwa ndi wolungama mtima, ankaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu, ndipo anali ndi nkhosa 7,000, ngamira 3,000, ngʼombe zantchito 1,000 ndi abulu aakazi 500, ndiponso anali ndi antchito ambiri. Iye anali munthu wotchuka kwambiri pakati pa anthu onse a mʼmayiko a kummawa.

Ana ake aamuna ankachita phwando mosinthanasinthana mʼnyumba zawo, ndipo ankayitana alongo awo atatu aja kudzadya ndi kumwa nawo. Masiku aphwandowo atatha, Yobu ankawayitana kuti adzawayeretse. Mmamawa iye ankapereka nsembe yopsereza kuperekera mwana aliyense, poganiza kuti, “Mwina ana anga achimwa ndi kutukwana Mulungu mʼmitima yawo.” Umu ndi mmene Yobu ankachitira nthawi zonse.

Yobu Ayesedwa Koyamba

Ana a Mulungu atabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anafika nawo limodzi. Yehova anati kwa Satanayo, “Kodi iwe ukuchokera kuti?”

Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”

Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.”

Satana anayankha kuti, “Kodi Yobu amaopa Mulungu popanda chifukwa?” 10 “Kodi Inu simumamuteteza iyeyo, nyumba yake ndi zonse zimene ali nazo? Mwadalitsa ntchito ya manja ake, kotero kuti nkhosa ndi ngʼombe zake zili ponseponse mʼdzikomo. 11 Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kukantha zonse ali nazo ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”

12 Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, tsono zonse zimene ali nazo ndaziyika mʼmanja mwako, koma iye yekhayo usamukhudze.”

Pamenepo Satana anachoka pamaso pa Yehova.

13 Tsiku lina pamene ana aamuna ndi ana aakazi a Yobu ankachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba mwa mkulu wawo, 14 wamthenga anabwera kwa Yobu ndipo anati, “Ngʼombe zanu zotipula ndipo abulu anu amadya chapafupi pomwepo, 15 tsono panabwera Aseba kudzatithira nkhondo ndi kutenga zonse. Apha antchito ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

16 Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Kunagwa mphenzi ndipo yapsereza nkhosa ndi antchito anu onse, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

17 Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Akasidi anadzigawa mʼmagulu atatu ankhondo ndipo anafika pa ngamira zanu ndi kuzitenga. Apha antchito anu onse ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

18 Iyeyo akuyankhulabe, panafikanso wamthenga wina nati, “Ana anu aamuna ndi aakazi amachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba ya mkulu wawo, 19 mwadzidzidzi chinayamba chimphepo champhamvu chochokera ku chipululu, nʼkudzawomba nyumba mbali zonse zinayi. Nyumbayo yawagwera ndipo afa, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

20 Atamva zimenezi, Yobu anayimirira nangʼamba mkanjo wake, ndi kumeta tsitsi lake. Kenaka anadzigwetsa pansi napembedza Mulungu, 21 nati,

“Ndinatuluka maliseche mʼmimba mwa amayi anga,
    namonso mʼmanda ndidzalowa wamaliseche.
Yehova ndiye anapereka ndipo Yehova watenga;
    litamandike dzina la Yehova.”

22 Mu zonsezi, Yobu sanachimwe kapena kunena kuti, “Mulungu walakwa.”

Yobu Ayesedwa Kachiwiri

Tsiku linanso pamene ana a Mulungu anabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anabwera nawo limodzi kudzadzionetsa pamaso pa Yehova. Ndipo Yehova anati kwa Satana, “Kodi iwe ukuchokera kuti?”

Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”

Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Ndipo iye akanalibe wangwiro, ngakhale iwe unandiwumiriza kuti ndikulole kuti umuvutitse popanda chifukwa.”

Satana anayankha kuti, “Iye ayesedwe mʼthupi mwake. Munthu angathe kupereka zonse ali nazo malingana iyeyo ali ndi moyo. Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kuwononga thupi lake, ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”

Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, iye ali mʼmanja mwako; koma moyo wake usawuchotse.”

Choncho Satana anachoka pamaso pa Yehova napita kukazunza Yobu ndi zilonda zaululu pa thupi lake lonse. Pamenepo Yobu anatenga phale ndi kumadzikanda nalo atakhala pa dzala la phulusa.

Mkazi wake anati kwa iye, “Kodi ukuwumirirabe kukhala wangwiro? Tukwana Mulungu kuti ufe!”

10 Yobu anayankha kuti, “Ukuyankhula ngati mkazi wopusa. Kodi tidzalandira zokoma zokhazokha kwa Mulungu, osalandiranso zowawa?”

Mu zonsezi, Yobu sanachimwe pa zimene anayankhula.

Abwenzi Atatu a Yobu

11 Abwenzi atatu a Yobu, Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama, atamva za tsoka lonse limene linamugwera iye, ananyamuka ku nyumba zawo nakumana malo amodzi mopangana kuti apite ndi kukamupepesa Yobu ndi kumutonthoza. 12 Atamuona Yobuyo, iwo ali chapatalipo, sanathe kumuzindikira. Choncho anayamba kulira mokweza mawu ndipo anangʼamba mikanjo yawo ndi kuwaza fumbi pa mitu yawo. 13 Tsono anakhala naye pamodzi pansi kwa masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku omwe. Palibe ndi mmodzi yemwe anayankhula naye, chifukwa anazindikira kuti Yobu amavutika kwambiri.

Mawu a Yobu

Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa. Ndipo Yobu anati:

“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe
    ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
Tsiku limenelo lisanduke mdima;
    Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso;
    kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli;
    mtambo uphimbe tsikuli;
    mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani;
    usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka,
    kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino;
    kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo,
    iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima;
    tsikulo liyembekezere kucha pachabe
    ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
10 Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga
    ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.

11 “Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa
    ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
12 Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo
    ndi mawere woti andiyamwitsepo?
13 Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere;
    ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
14 pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi,
    amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
15 pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide,
    amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
16 Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale,
    ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
17 Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto,
    ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
18 A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere;
    sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
19 Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko,
    ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.

20 “Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto,
    ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
21 kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera,
    amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
22 amene amakondwa ndi kusangalala
    akamalowa mʼmanda?
23 Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu
    amene njira yake yabisika,
    amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
24 Mʼmalo moti ndidye, ndimalira,
    ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
25 Chimene ndinkachiopa chandigwera;
    chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
26 Ndilibe mtendere kapena bata,
    ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”

Mawu a Elifazi

Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

“Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe?
    Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri,
    momwe walimbitsira anthu ofowoka.
Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa;
    unachirikiza anthu wotha mphamvu.
Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima,
    zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako?
    Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?

“Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse?
    Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa,
    ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu;
    amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
10 Mikango imabangula ndi kulira,
    komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
11 Mkango umafa chifukwa chosowa nyama,
    ndipo ana amkango amamwazikana.

12 “Mawu anabwera kwa ine mwamseri,
    makutu anga anamva kunongʼona kwake.
13 Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku,
    nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
14 ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera
    ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
15 Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga,
    ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
16 Chinthucho chinayimirira
    koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani.
Chinthu chinayima patsogolo panga,
    kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
17 ‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu?
    Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
18 Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe,
    ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
19 nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi,
    amene maziko awo ndi fumbi,
    amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
20 Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa;
    mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
21 Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu,
    kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.