Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Beginning

Read the Bible from start to finish, from Genesis to Revelation.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
2 Samueli 22-24

Nyimbo ya Mayamiko ya Davide

22 Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Iye anati,

“Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
    Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo,
    chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa.
Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga.
    Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.

“Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando,
    ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.

“Mafunde a imfa anandizinga;
    mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
Anandimanga ndi zingwe za ku manda;
    misampha ya imfa inalimbana nane.

“Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova;
    ndinapemphera kwa Mulungu wanga.
Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga;
    kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.

“Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi,
    maziko a miyamba anagwedezeka;
    ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi;
    moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake,
    makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
10 Iye anangʼamba thambo natsika pansi;
    pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
11 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka;
    nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
12 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake,
    mitambo yakuda ya mlengalenga.
13 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake
    munkachokera makala amoto alawilawi.
14 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu,
    mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
15 Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake,
    ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
16 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera,
    ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera,
Yehova atabangula mwaukali,
    pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.

17 “Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira;
    anandivuwula mʼmadzi ozama.
18 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu,
    adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
19 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto,
    koma Yehova anali thandizo langa.
20 Iye anandipititsa kumalo otakasuka;
    anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.

21 “Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa;
    molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
22 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova;
    ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
23 Malamulo ake onse ali pamaso panga,
    sindinasiye malangizo ake.
24 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake
    ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
25 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa,
    molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.

26 “Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu,
    kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
27 Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu,
    koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
28 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa,
    koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
29 Inu Yehova, ndinu nyale yanga;
    Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
30 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo,
    ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.

31 “Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro;
    mawu a Yehova alibe cholakwika.
Iye ndi chishango
    kwa onse amene amathawira kwa iye.
32 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova?
    Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
33 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu
    ndi kulungamitsa njira yanga.
34 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi;
    Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
35 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;
    manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
36 Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso;
    mumawerama kuti mundikweze.
37 Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino,
    kuti mapazi anga asaterereke.

38 “Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha;
    sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
39 Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso;
    Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
40 Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo;
    munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
41 Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa;
    ndipo ndinawononga adani anga.
42 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa.
    Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
43 Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi;
    ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.

44 “Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu;
    Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina.
Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
45     Alendo amadzipereka okha pamaso panga;
    akangomva za ine, amandigonjera.
46 Iwo onse anataya mtima;
    anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.

47 “Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa.
    Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
48 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango,
    amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
49     amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga.
Inu munandikuza kuposa adani anga;
    munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
50 Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina;
    ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.

51 “Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake,
    amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake,
    kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”

Mawu Otsiriza a Davide

23 Nawa mawu otsiriza a Davide:

“Mawu a Davide mwana wa Yese,
    mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba,
munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo,
    woyimba nyimbo za Israeli:

“Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine;
    mawu ake anali pakamwa panga.
Mulungu wa Israeli anayankhula,
    Thanthwe la Israeli linati kwa ine:
‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo,
    pamene alamulira moopa Mulungu,
amakhala ngati kuwala kwa mmamawa,
    mmawa wopanda mitambo,
monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa
    imene imameretsa udzu mʼnthaka.’

“Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu?
    Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine,
    lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse?
Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa,
    ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?
Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga,
    imene sitengedwa ndi manja.
Aliyense amene wayikhudza mingayo
    amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo;
    nayitentha pa moto.”

Ankhondo Otchuka a Davide

Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide:

Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.

Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo. 10 Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.

11 Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo. 12 Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.

13 Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu. 14 Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu. 15 Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!” 16 Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova. 17 Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo.

Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.

18 Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja. 19 Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.

20 Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango. 21 Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe. 22 Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja. 23 Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.

24 Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa:

Asaheli mʼbale wa Yowabu,

Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,

25 Sama Mharodi,

Elika Mherodi,

26 Helezi Mpaliti,

Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,

27 Abiezeri wa ku Anatoti,

Sibekai Mhusati,

28 Zalimoni Mwahohi,

Maharai Mnetofa,

29 Heledi mwana wa Baana Mnetofa,

Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,

30 Benaya Mpiratoni,

Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.

31 Abi-Aliboni Mwaribati,

Azimaveti Mbarihumi,

32 Eliyahiba Msaaliboni,

ana a Yaseni,

Yonatani, 33 mwana wa Sama Mharari,

Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,

34 Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati,

Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,

35 Heziro wa ku Karimeli,

Paarai Mwaribi,

36 Igala mwana wa Natani wa ku Zoba,

mwana wa Hagiri,

37 Zeleki Mwamoni,

Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,

38 Ira Mwitiri,

Garebu Mwitiri,

39 ndi Uriya Mhiti.

Onse pamodzi analipo 37.

Davide Awerenga Ankhondo

24 Nthawi inanso Yehova anawakwiyira Aisraeli ndipo anawutsa mtima wa Davide kuti awavutitse ndipo anati, “Pita kawerenge Aisraeli ndi Ayuda.”

Choncho mfumu inati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali nawo. “Pitani pakati pa mafuko onse a Israeli kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba kuti mukawerenge anthu omenya nkhondo ndi cholinga choti ndidziwe chiwerengero chawo.”

Koma Yowabu anayankha mfumu kuti, “Yehova Mulungu wanu achulukitse ankhondo anu kukhala miyandamiyanda, ndipo alole inu mbuye wanga mfumu mudzazione zimenezi. Koma nʼchifukwa chiyani inu mbuye wanga mfumu mukufuna kuchita zimenezi?”

Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu ndi atsogoleri a ankhondo. Choncho anachoka pamaso pa mfumu kupita kukawerenga anthu omenya nkhondo mu Israeli.

Atawoloka Yorodani, iwo anamanga misasa yawo pafupi ndi Aroeri kummwera kwa mzinda wa ku chigwa ndipo kenaka iwo anapita ku dziko la Gadi mpaka ku Yazeri. Iwo anapita ku Giliyadi ndi ku chigwa cha Tahitimu Hodisi ndipo anapitirira mpaka ku Dani Yaani ndi madera ozungulira Sidoni. Kenaka iwo anapita molunjika linga la ku Turo ndi ku mizinda yonse ya Ahivi ndi Akanaani. Pomaliza anapita ku Beeriseba ku Negevi wa ku Yuda.

Atayendayenda mʼdziko lonse anabwerera ku Yerusalemu patapita miyezi isanu ndi inayi ndi masiku makumi awiri.

Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa mfumu: Mu Israeli munali anthu 800,000 amphamvu amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga ndipo mu Yuda munali anthu 500,000.

10 Davide anatsutsika mu mtima mwake atatha kuwerenga anthuwo ndipo anapemphera kwa Yehova kuti, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono Yehova, ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”

11 Davide asanadzuke mmawa mwake mawu a Yehova anafika kwa mneneri Gadi, mlosi wa Davide kuti, 12 “Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’ ”

13 Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa iye, “Kodi mungakonde kuti mʼdziko mwanu mukhale njala kwa zaka zitatu? Kapena kuti mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu? Kapena kuti mʼdziko muno mukhale mliri kwa masiku atatu? Tsopano, ganizirani bwino ndipo musankhe chomwe mudzamuyankhe amene wandituma.”

14 Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ife atilange ndi Yehova pakuti chifundo chake ndi chachikulu, koma ndisalangidwe ndi anthu.”

15 Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, kuyambira mmawa mpaka pa nthawi imene anafuna mwini wake, ndipo unapha anthu 70,000 kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba. 16 Pamene mngelo anatambasula dzanja lake kuti awononge Yerusalemu, Yehova anamva chisoni chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.

17 Davide ataona mngelo amene ankakantha anthu uja, anati kwa Yehova, “Ine ndi amene ndachimwa. Ine mʼbusa ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Langani ineyo pamodzi ndi banja langa.”

Davide Amanga Guwa la Nsembe

18 Tsiku limenelo Gadi anapita kwa Davide ndi kukanena kuti, “Pitani kamangeni guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.” 19 Ndipo Davide anapita monga momwe Yehova anamulamulira kudzera mwa Gadi. 20 Arauna atayangʼana ndi kuona mfumu ndi anthu ake akubwera kumene kunali iye, iyeyo anatuluka ndi kuwerama pamaso pa mfumu mpaka nkhope yake kugunda pansi.

21 Arauna anati, “Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mfumu mwabwera kwa mtumiki wanu?”

Davide anayankha kuti, “Kudzagula malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe kuti mliri uli pa anthuwa usiye.”

22 Arauna anati kwa Davide, “Mbuye wanga mfumu mutenge chilichonse chimene chikukondweretseni ndi kuchipereka nsembe. Nazi ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, nazi zopunthira tirigu ndi magoli angʼombe kuti zikhale nkhuni. 23 Inu mfumu, Arauna akupereka zonsezi kwa inu mfumu.” Arauna anatinso kwa iye, “Yehova Mulungu wanu akuvomerezeni.”

24 Koma mfumu inayankha Arauna kuti, “Ayi, Ine ndikunenetsa kuti ndikulipira. Sindidzapereka kwa Yehova Mulungu wanga nsembe yopsereza imene sindinavutikire.”

Kotero Davide anagula malo wopunthira tiriguwo ndi ngʼombe ndipo anapereka kwa Araunayo masekeli asiliva makumi asanu. 25 Davide anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Ndipo Yehova anayankha pempherolo mʼmalo mwa dziko lonse, ndipo mliri unatha pa Aisraeli.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.