Beginning
1 Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha,
umene kale unali wodzaza ndi anthu!
Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu!
Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye.
Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi,
tsopano wasanduka kapolo.
2 Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse,
misozi ili pa masaya pake.
Mwa abwenzi ake onse,
palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza.
Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu;
onse akhala adani ake.
3 Yuda watengedwa ku ukapolo,
kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa.
Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina;
ndipo alibe malo opumulira.
Onse omuthamangitsa iye amupitirira,
ndipo alibe kwina kothawira.
4 Misewu yopita ku Ziyoni ikulira,
chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake.
Zipata zake zonse zili pululu,
ansembe akubuwula.
Anamwali ake akulira,
ndipo ali mʼmasautso woopsa.
5 Adani ake asanduka mabwana ake;
odana naye akupeza bwino.
Yehova wamubweretsera mavuto
chifukwa cha machimo ake ambiri.
Ana ake atengedwa ukapolo
pamaso pa mdani.
6 Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni
wachokeratu.
Akalonga ake ali ngati mbawala
zosowa msipu;
alibe mphamvu zothawira
owathamangitsa.
7 Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake,
Yerusalemu amakumbukira chuma chonse
chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake.
Anthu ake atagwidwa ndi adani ake,
panalibe aliyense womuthandiza.
Adani ake ankamuyangʼana
ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.
8 Yerusalemu wachimwa kwambiri
ndipo potero wakhala wodetsedwa.
Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza,
chifukwa aona umaliseche wake.
Iye mwini akubuwula
ndipo akubisa nkhope yake.
9 Uve wake umaonekera pa zovala zake;
iye sanaganizire za tsogolo lake.
Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu;
ndipo analibe womutonthoza.
“Inu Yehova, taonani masautso anga,
pakuti mdani wapambana.”
10 Adani amulanda
chuma chake chonse;
iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika,
amene Inu Mulungu munawaletsa
kulowa mu msonkhano wanu.
11 Anthu ake onse akubuwula
pamene akufunafuna chakudya;
asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya
kuti akhale ndi moyo.
“Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani,
chifukwa ine ndanyozeka.”
12 “Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa?
Yangʼanani ndipo muone.
Kodi pali mavuto ofanana ndi
amene andigwerawa,
amene Ambuye anandibweretsera
pa tsiku la ukali wake?
13 “Anatumiza moto kuchokera kumwamba,
unalowa mpaka mʼmafupa anga.
Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga
ndipo anandibweza.
Anandisiya wopanda chilichonse,
wolefuka tsiku lonse.
14 “Wazindikira machimo anga onse
ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi.
Machimowa afika pakhosi panga,
ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu.
Iye wandipereka
kwa anthu amene sindingalimbane nawo.
15 “Ambuye wakana
anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane:
wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane,
kuti litekedze anyamata anga;
mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza
anamwali a Yuda.
16 “Chifukwa cha zimenezi ndikulira
ndipo maso anga adzaza ndi misozi.
Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze,
palibe aliyense wondilimbitsa mtima.
Ana anga ali okhaokha
chifukwa mdani watigonjetsa.
17 “Ziyoni wakweza manja ake,
koma palibe aliyense womutonthoza.
Yehova walamula kuti abale ake
a Yakobo akhale adani ake;
Yerusalemu wasanduka
chinthu chodetsedwa pakati pawo.
18 “Yehova ndi wolungama,
koma ndine ndinawukira malamulo ake.
Imvani inu anthu a mitundu yonse;
onani masautso anga.
Anyamata ndi anamwali anga
agwidwa ukapolo.
19 “Ndinayitana abwenzi anga
koma anandinyenga.
Ansembe ndi akuluakulu anga
anafa mu mzinda
pamene ankafunafuna chakudya
kuti akhale ndi moyo.
20 “Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira!
Ndikuzunzika mʼkati mwanga,
ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa
chifukwa ndakhala osamvera.
Mʼmisewu anthu akuphedwa,
ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.
21 “Anthu amva kubuwula kwanga,
koma palibe wonditonthoza.
Adani anga onse amva masautso anga;
iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita.
Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija
kuti iwonso adzakhale ngati ine.
22 “Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu;
muwalange
ngati mmene mwandilangira ine
chifukwa cha machimo anga onse.
Ndikubuwula kwambiri
ndipo mtima wanga walefuka.”
2 Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni
ndi mtambo wa mkwiyo wake!
Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli
kuchoka kumwamba.
Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso
popondapo mapazi ake.
2 Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo;
mu mkwiyo wake anagwetsa
malinga a mwana wamkazi wa Yuda.
Anagwetsa pansi mochititsa manyazi
maufumu ndi akalonga ake.
3 Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola
nyanga iliyonse ya Israeli.
Anabweza dzanja lake lamanja
pamene mdani anamuyandikira.
Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa
umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.
4 Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani;
wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani,
ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira.
Ukali wake ukuyaka ngati moto
pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.
5 Ambuye ali ngati mdani;
wawonongeratu Israeli;
wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu
ndipo wawononga malinga ake.
Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira
kwa mwana wamkazi wa Yuda.
6 Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda;
wawononga malo ake a msonkhano.
Yehova wayiwalitsa Ziyoni
maphwando ake oyikika ndi masabata ake.
Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza
mfumu ndi wansembe.
7 Ambuye wakana guwa lake la nsembe
ndipo wasiya malo ake opatulika.
Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu
kwa mdani wake;
adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova
ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.
8 Yehova anatsimikiza kugwetsa
makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni.
Anawayesa ndi chingwe
ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa.
Analiritsa malinga ndi makoma;
onse anawonongeka pamodzi.
9 Zipata za Yerusalemu zalowa pansi;
wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake.
Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu,
palibenso lamulo,
ndipo aneneri ake sakupeza
masomphenya kuchokera kwa Yehova.
10 Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni
akhala chete pansi;
awaza fumbi pa mitu yawo
ndipo avala ziguduli.
Anamwali a Yerusalemu
aweramitsa mitu yawo pansi.
11 Maso anga atopa ndi kulira,
ndazunzika mʼmoyo mwanga,
mtima wanga wadzaza ndi chisoni
chifukwa anthu anga akuwonongeka,
chifukwa ana ndi makanda akukomoka
mʼmisewu ya mu mzinda.
12 Anawo akufunsa amayi awo kuti,
“Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?”
pamene akukomoka ngati anthu olasidwa
mʼmisewu ya mʼmizinda,
pamene miyoyo yawo ikufowoka
mʼmanja mwa amayi awo.
13 Ndinganene chiyani za iwe?
Ndingakufanizire ndi chiyani,
iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu?
Kodi ndingakufanizire ndi yani
kuti ndikutonthoze,
iwe namwali wa Ziyoni?
Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja,
kodi ndani angakuchiritse?
14 Masomphenya a aneneri ako
anali abodza ndi achabechabe.
Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo
poyika poyera mphulupulu zako.
Mauthenga amene anakupatsa
anali achabechabe ndi osocheretsa.
15 Onse oyenda mʼnjira yako
akukuwombera mʼmanja;
akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola
iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu:
“Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa
wokongola kotheratu,
chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”
16 Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza;
iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo,
ndipo akuti, “Tamumeza.
Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera;
tili ndi moyo kuti tilione.”
17 Yehova wachita chimene anakonzeratu;
wakwaniritsa mawu ake,
amene anatsimikiza kale lomwe.
Wakuwononga mopanda chifundo,
walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako,
wakweza mphamvu za adani ako.
18 Mitima ya anthu
ikufuwulira Ambuye.
Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni,
misozi yako itsike ngati mtsinje
usana ndi usiku;
usadzipatse wekha mpumulo,
maso ako asaleke kukhetsa misozi.
19 Dzuka, fuwula usiku,
pamene alonda ayamba kulondera;
khuthula mtima wako ngati madzi
pamaso pa Ambuye.
Kweza manja ako kwa Iye
chifukwa cha miyoyo ya ana ako,
amene akukomoka ndi njala
mʼmisewu yonse ya mu mzinda.
20 Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani:
kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi?
Kodi amayi adye ana awo,
amene amawasamalira?
Kodi ansembe ndi aneneri awaphere
mʼmalo opatulika a Ambuye?
21 Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi
pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda;
anyamata anga ndi anamwali anga
aphedwa ndi lupanga.
Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu;
mwawapha mopanda chifundo.
22 Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando,
chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse.
Pa tsiku limene Yehova wakwiya
palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo;
mdani wanga wawononga
onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.
3 Ine ndine munthu amene ndaona masautso
ndi ndodo ya ukali wake.
2 Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa
mu mdima osati mʼkuwala;
3 zoonadi anandikantha ndi dzanja lake
mobwerezabwereza tsiku lonse.
4 Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga,
ndipo waphwanya mafupa anga.
5 Wandizinga ndi kundizungulira
ndi zowawa ndi zolemetsa.
6 Wandikhazika mu mdima
ngati amene anafa kale.
7 Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe,
wandimanga ndi maunyolo.
8 Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo,
amakana pemphero langa.
9 Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema;
ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10 Wandidikirira ngati chimbalangondo,
wandibisalira ngati mkango.
11 Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba,
ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 Wakoka uta wake
ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 Walasa mtima wanga
ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse;
amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 Wandidyetsa zowawa
ndipo wandimwetsa ndulu.
16 Wathyola mano anga ndi miyala;
wandiviviniza mʼfumbi;
17 Wandichotsera mtendere;
ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka
ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19 Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala,
zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 Ine ndikuzikumbukira bwino izi,
ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 Komabe ndimakumbukira zimenezi,
nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu,
ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse;
kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse;
motero ndimamuyembekezera.”
25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye,
kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha
Yehova modekha.
27 Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli
pamene ali wamngʼono.
28 Akhale chete pa yekha,
chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 Abise nkhope yake mʼfumbi
mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye,
ndipo amuchititse manyazi.
31 Chifukwa Ambuye satayiratu
anthu nthawi zonse.
32 Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo,
chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 Pakuti sabweretsa masautso mwadala,
kapena zowawa kwa ana a anthu.
34 Kuphwanya ndi phazi
a mʼndende onse a mʼdziko,
35 kukaniza munthu ufulu wake
pamaso pa Wammwambamwamba,
36 kumana munthu chiweruzo cholungama—
kodi Ambuye saona zonsezi?
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.