Add parallel Print Page Options

Mose Amwalira

34 Ndipo Mose anakwera Phiri la Nebo kuchokera ku chigwa cha Mowabu ndi kukafika pamwamba pa Phiri la Pisiga, kummawa kwa Yeriko. Kumeneko Yehova anamuonetsa dziko lonse; kuchokera ku Giliyadi mpaka ku Dani. Dera lonse la Nafutali, dziko lonse la Efereimu ndi Manase, dziko lonse la Yuda mpaka kukafika kumadzulo kwa nyanja, Negevi ndi chigawo chonse kuchokera ku Chigwa cha Yeriko, Mzinda wa mitengo ya migwalangwa, mpaka ku Zowari. Kenaka Yehova anawuza Mose kuti, “Limenelo ndi dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo pamene ndinanena kuti, ‘Ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’ Ndakulola kuti ulione, koma sudzawoloka kuti ukalowemo.”

Choncho Mose mtumiki wa Yehova anamwalira kumeneko ku Mowabu, monga momwe ananenera Yehova. Yehova anamuyika mʼmanda ku Mowabu, mʼchigwa choyangʼanana ndi Beti-Peori, koma mpaka lero palibe amene amadziwa pamene pali manda ake. Mose anamwalira ali ndi zaka 120, koma maso ake ankaonabe ndipo anali amphamvu. Aisraeli analira maliro a Mose mʼchikhwawa cha Mowabu kwa masiku makumi atatu mpaka nthawi ya kulira maliro ndi kukhuza inatha.

Tsono Yoswa, mwana wa Nuni anadzazidwa ndi mzimu wanzeru chifukwa nʼkuti Mose atamusanjika manja. Choncho Aisraeli anamumvera ndipo anachita zomwe Yehova analamula Mose.

10 Kuyambira nthawi imeneyi, mu Israeli simunakhalepo mneneri wina aliyense wofanana ndi Mose, amene Yehova amayankhula naye maso ndi maso. 11 Amene anachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi ndi zozizwitsa zimene Yehova anamutuma kuti achite mu Igupto, kwa Farao ndi kwa nduna zake zonse ndiponso mʼdziko lake lonse. 12 Ndithudi palibe mneneri wina aliyense amene anachita zinthu zazikulu ndi zoopsa zofanana ndi zomwe Mose anachita pamaso pa Aisraeli onse.

The Death of Moses

34 Then Moses climbed Mount Nebo(A) from the plains of Moab to the top of Pisgah,(B) across from Jericho.(C) There the Lord showed(D) him the whole land—from Gilead to Dan,(E) all of Naphtali, the territory of Ephraim and Manasseh, all the land of Judah as far as the Mediterranean Sea,(F) the Negev(G) and the whole region from the Valley of Jericho, the City of Palms,(H) as far as Zoar.(I) Then the Lord said to him, “This is the land I promised on oath(J) to Abraham, Isaac and Jacob(K) when I said, ‘I will give it(L) to your descendants.’ I have let you see it with your eyes, but you will not cross(M) over into it.”

And Moses the servant of the Lord(N) died(O) there in Moab, as the Lord had said. He buried him[a] in Moab, in the valley opposite Beth Peor,(P) but to this day no one knows where his grave is.(Q) Moses was a hundred and twenty years old(R) when he died, yet his eyes were not weak(S) nor his strength gone.(T) The Israelites grieved for Moses in the plains of Moab(U) thirty days,(V) until the time of weeping and mourning(W) was over.

Now Joshua son of Nun was filled with the spirit[b] of wisdom(X) because Moses had laid his hands on him.(Y) So the Israelites listened to him and did what the Lord had commanded Moses.

10 Since then, no prophet(Z) has risen in Israel like Moses,(AA) whom the Lord knew face to face,(AB) 11 who did all those signs and wonders(AC) the Lord sent him to do in Egypt—to Pharaoh and to all his officials(AD) and to his whole land. 12 For no one has(AE) ever shown the mighty power or performed the awesome deeds(AF) that Moses did in the sight of all Israel.

Footnotes

  1. Deuteronomy 34:6 Or He was buried
  2. Deuteronomy 34:9 Or Spirit