Print Page Options
Previous Prev Day Next DayNext

Beginning

Read the Bible from start to finish, from Genesis to Revelation.
Duration: 365 days
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)
Version
Masalimo 58-65

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide.

58 Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama?
    Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama,
    ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera;
    kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka,
    ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
Imene simva liwu la munthu wamatsenga,
    ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.

Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu,
    Yehova khadzulani mano a mikango!
Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda
    pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda;
    ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.

Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku,
    kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango,
    pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 Ndipo anthu adzanena kuti,
    “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho;
    zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe.

59 Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu;
    munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
Landitseni kwa anthu ochita zoyipa
    ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.

Onani momwe iwo akundibisalira!
    Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane;
    osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo.
    Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,
    dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse;
    musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.

Iwo amabweranso madzulo
    akuchita phokoso ngati agalu
    ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo;
    iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo,
    ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
Koma Inu Yehova, mumawaseka,
    mumayinyoza mitundu yonseyo.

Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu;
Inu Mulungu, ndinu linga langa. 10     Mulungu wanga wachikondi.

Mulungu adzapita patsogolo panga
    ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
11 Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu,
    kuopa kuti anthu anga angayiwale.
Mwa mphamvu zanu,
    lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
12 Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo
    chifukwa cha mawu a milomo yawo,
    iwo akodwe mʼkunyada kwawo.
Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
13     muwawononge mu ukali (wanu)
    muwawononge mpaka atheretu.
Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi
    kuti Mulungu amalamulira Yakobo.

14 Iwo amabweranso madzulo,
    akuchita phokoso ngati agalu
    ndi kumangoyenda mu mzinda.
15 Iwo amayendayenda kufuna chakudya
    ndipo amawuwa ngati sanakhute.
16 Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu,
    mmawa ndidzayimba zachikondi chanu;
pakuti ndinu linga langa,
    pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.

17 Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu;
    Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere.

60 Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza.
    Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba,
    konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto;
    inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.

Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera
    kuti tisonkhanireko pothawa uta.

Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja,
    kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:
    “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu
    ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;
    Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,
    Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
Mowabu ndi mbale yanga yosambira,
    pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga,
    pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”

Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa?
    Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife
    ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu,
    pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano
    ndipo tidzapondaponda adani athu.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe.

61 Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu;
    mvetserani pemphero langa.

Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu
    ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka;
    tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga,
    nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.

Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya
    ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga;
    mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.

Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu,
    zaka zake kwa mibado yochuluka.
Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya;
    ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.

Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu
    ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide.

62 Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha;
    chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;
    Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.

Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti?
    Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba,
    ngati mpanda wogwedezeka?
Iwo akufunitsitsa kumugwetsa
    kuti achoke pa malo ake apamwamba.
    Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza.
Ndi pakamwa pawo amadalitsa
    koma mʼmitima yawo amatemberera.

Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga;
    chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;
    Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu:
    Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu;
    khuthulani mitima yanu kwa Iye,
    pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu.
            Sela

Anthu wamba ndi mpweya chabe;
    anthu apamwamba ndi bodza chabe;
ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe;
    iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
10 Musadalire kulanda mwachinyengo
    kapena katundu wobedwa;
ngakhale chuma chanu chichuluke,
    musayike mtima wanu pa icho.

11 Mulungu wayankhula kamodzi,
    ine ndamvapo zinthu ziwiri;
choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
12     komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika.
Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu
    molingana ndi ntchito zake.

Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda.

63 Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga,
    moona mtima ine ndimakufunafunani;
moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu,
    thupi langa likulakalaka inu,
mʼdziko lowuma ndi lotopetsa
    kumene kulibe madzi.

Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika
    ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
Chifukwa chikondi chanu
    ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga,
    ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona.
    Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.

Pa bedi panga ndimakumbukira inu;
    ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
Chifukwa ndinu thandizo langa,
    ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
Moyo wanga umakangamira Inu;
    dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.

Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa;
    adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 Iwo adzaperekedwa ku lupanga
    ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.

11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu;
    onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo,
    koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

64 Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga;
    tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa,
    ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.

Iwo amanola malilime awo ngati malupanga,
    amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa;
    amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.

Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa,
    amayankhula zobisa misampha yawo;
    ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati,
    “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!”
    Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.

Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi;
    mwadzidzidzi adzakanthidwa.
Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa
    ndi kuwasandutsa bwinja;
    onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.

Anthu onse adzachita mantha;
    adzalengeza ntchito za Mulungu
    ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
10 Lolani wolungama akondwere mwa Yehova
    ndi kubisala mwa Iye,
    owongoka mtima onse atamande Iye!

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo.

65 Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni;
    kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
Inu amene mumamva pemphero,
    kwa inu anthu onse adzafika.
Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo,
    Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
Odala iwo amene inu muwasankha
    ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu!
Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu,
    za mʼNyumba yanu yoyera.

Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo,
    Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,
chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi
    ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu,
    mutadziveka nokha ndi mphamvu.
Amene munakhalitsa bata nyanja
    kukokoma kwa mafunde ake,
    ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu;
    kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera.
    Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.

Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira;
    Inuyo mumalilemeretsa kwambiri.
Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi
    kuti upereke tirigu kwa anthu,
    pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
10 Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake,
    mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
11 Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka,
    ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
12 Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira;
    mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
13 Madambo akutidwa ndi zoweta
    ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu;
    izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (CCL)

The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.