Add parallel Print Page Options

Yehova Akubwera ndipo Akulamulira

14 Taonani tsiku la Yehova likubwera pamene zinthu zimene adani ako anakulanda azidzagawana iwe ukuona.

Ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse kuti adzathire nkhondo Yerusalemu; mzindawu udzalandidwa, nyumba zidzaphwasulidwa, ndipo akazi adzagwiriridwa. Theka la anthu a mu mzindamu lidzapita ku ukapolo, koma ena onse otsala mu mzindamu sadzachotsedwa.

Pamenepo Yehova adzabwera kudzamenyana ndi mitundu ya anthu imeneyi, ngati mmene amachitira pa nthawi ya nkhondo. Tsiku limenelo adzayimirira pa Phiri la Olivi, kummawa kwa Yerusalemu, ndipo Phiri la Olivilo lidzagawikana pawiri kuyambira kummawa mpaka kumadzulo, kupanga chigwa chachikulu, kuchititsa kuti theka la phiri lisunthire kumpoto ndi linalo kummwera. Inu mudzathawa podzera mʼchigwa chapakati pa phirilo, pakuti chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa monga munachitira pa tsiku la chivomerezi nthawi ya Uziya mfumu ya Yuda. Kenaka Yehova Mulungu wanga adzabwera, pamodzi ndi oyera ake onse.

Tsiku limenelo sipadzakhala kuwala, kuzizira kapena chisanu. Lidzakhala tsiku lapaderadera, silidzakhala usana kapena usiku; tsiku limeneli akulidziwa ndi Yehova yekha. Ikadzafika nthawi ya madzulo, kudzakhala kukuwalabe.

Tsiku limenelo madzi amoyo adzatuluka mu Yerusalemu, theka lidzapita ku nyanja ya kummawa ndipo theka lina ku nyanja ya kumadzulo, nthawi yachilimwe ndi nthawi yozizira yomwe.

Ndipo Yehova adzakhala mfumu pa dziko lonse lapansi. Tsiku limenelo padzakhala Ambuye mmodzi yekha, ndipo dzina lidzakhala limodzi lomwelo.

10 Dziko lonse, kuyambira ku Geba mpaka ku Rimoni, kummwera kwa Yerusalemu, lidzakhala ngati Araba. Koma Yerusalemu adzakwezedwa ndipo adzakhala pamalo pakepo, kuyambira ku Chipata cha Benjamini mpaka ku malo amene ali ku Chipata Choyamba, ku Chipata Chapangodya, ndipo kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku malo opsinyira mphesa za mfumu. 11 Mʼmenemo mudzakhala anthu; sadzawonongedwanso. Yerusalemu adzakhala pa mtendere.

12 Mliri umene Yehova adzakanthire nawo mitundu yonse ya anthu imene inkamenyana ndi Yerusalemu ndi uwu: Matupi awo adzawola iwo eni akuyenda, maso awo adzawola ali mʼmalo mwake, ndipo malilime awo adzawola ali mʼkamwa mwawo. 13 Pa tsiku limenelo Yehova adzasokoneza anthu akuluakulu. Munthu aliyense adzagwira dzanja la mnzake, ndi kuyamba kumenyana okhaokha. 14 Yuda nayenso adzachita nkhondo ku Yerusalemu. Chuma chonse cha anthu a mitundu yozungulira adzachisonkhanitsa pamodzi; golide, siliva ndi zovala zochuluka kwambiri. 15 Mliri womwewo udzapha akavalo ndi nyulu, ngamira ndi abulu, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku misasako.

16 Kenaka opulumuka ochokera mwa mitundu yonse ya anthu amene anathira nkhondo Yerusalemu, azidzapita chaka ndi chaka kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, ndiponso kukachita Chikondwerero cha Misasa. 17 Ngati mitundu ina ya anthu pa dziko lapansi sidzapita ku Yerusalemu kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, idzakhala wopanda mvula. 18 Ndipo ngati anthu a ku Igupto sadzapita ndi kukakhala nawo kumeneko, adzakhala wopanda mvula. Yehova adzabweretsa pa iwo mliri umene analangira mitundu ina ya anthu imene sinapite ku Chikondwerero cha Misasa. 19 Chimenechi chidzakhala chilango cha Igupto ndiponso mitundu ina yonse imene sidzapita ku Chikondwerero cha Misasa.

20 Pa tsiku limenelo pa maberu a akavalo padzalembedwa mawu oti wopatulikira Yehova, ndipo miphika ya mʼNyumba ya Yehova idzakhala yopatulika ngati mbale za ku guwa. 21 Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.

The Lord Comes and Reigns

14 A day of the Lord(A) is coming, Jerusalem, when your possessions(B) will be plundered and divided up within your very walls.

I will gather all the nations(C) to Jerusalem to fight against it;(D) the city will be captured, the houses ransacked, and the women raped.(E) Half of the city will go into exile, but the rest of the people will not be taken from the city.(F) Then the Lord will go out and fight(G) against those nations, as he fights on a day of battle.(H) On that day his feet will stand on the Mount of Olives,(I) east of Jerusalem, and the Mount of Olives will be split(J) in two from east to west, forming a great valley, with half of the mountain moving north and half moving south. You will flee by my mountain valley, for it will extend to Azel. You will flee as you fled from the earthquake[a](K) in the days of Uzziah king of Judah. Then the Lord my God will come,(L) and all the holy ones with him.(M)

On that day there will be neither sunlight(N) nor cold, frosty darkness. It will be a unique(O) day—a day known only to the Lord—with no distinction between day and night.(P) When evening comes, there will be light.(Q)

On that day living water(R) will flow(S) out from Jerusalem, half of it east(T) to the Dead Sea and half of it west to the Mediterranean Sea, in summer and in winter.(U)

The Lord will be king(V) over the whole earth.(W) On that day there will be one Lord, and his name the only name.(X)

10 The whole land, from Geba(Y) to Rimmon,(Z) south of Jerusalem, will become like the Arabah. But Jerusalem will be raised up(AA) high from the Benjamin Gate(AB) to the site of the First Gate, to the Corner Gate,(AC) and from the Tower of Hananel(AD) to the royal winepresses, and will remain in its place.(AE) 11 It will be inhabited;(AF) never again will it be destroyed. Jerusalem will be secure.(AG)

12 This is the plague with which the Lord will strike(AH) all the nations that fought against Jerusalem: Their flesh will rot while they are still standing on their feet, their eyes will rot in their sockets, and their tongues will rot in their mouths.(AI) 13 On that day people will be stricken by the Lord with great panic.(AJ) They will seize each other by the hand and attack one another.(AK) 14 Judah(AL) too will fight at Jerusalem. The wealth of all the surrounding nations will be collected(AM)—great quantities of gold and silver and clothing. 15 A similar plague(AN) will strike the horses and mules, the camels and donkeys, and all the animals in those camps.

16 Then the survivors(AO) from all the nations that have attacked Jerusalem will go up year after year to worship(AP) the King,(AQ) the Lord Almighty, and to celebrate the Festival of Tabernacles.(AR) 17 If any of the peoples of the earth do not go up to Jerusalem to worship(AS) the King, the Lord Almighty, they will have no rain.(AT) 18 If the Egyptian people do not go up and take part, they will have no rain. The Lord[b] will bring on them the plague(AU) he inflicts on the nations that do not go up to celebrate the Festival of Tabernacles.(AV) 19 This will be the punishment of Egypt and the punishment of all the nations that do not go up to celebrate the Festival of Tabernacles.(AW)

20 On that day holy to the Lord(AX) will be inscribed on the bells of the horses, and the cooking pots(AY) in the Lord’s house will be like the sacred bowls(AZ) in front of the altar. 21 Every pot in Jerusalem and Judah will be holy(BA) to the Lord Almighty, and all who come to sacrifice will take some of the pots and cook in them. And on that day(BB) there will no longer be a Canaanite[c](BC) in the house(BD) of the Lord Almighty.(BE)

Footnotes

  1. Zechariah 14:5 Or My mountain valley will be blocked and will extend to Azel. It will be blocked as it was blocked because of the earthquake
  2. Zechariah 14:18 Or part, then the Lord
  3. Zechariah 14:21 Or merchant