Add parallel Print Page Options

Kuyitanidwa kwa Womva Ludzu

55 “Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu,
    bwerani madzi alipo;
ndipo inu amene mulibe ndalama
    bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye!
Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka
    osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya,
    ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa?
Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino;
    ndipo mudzisangalatse.
Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine;
    mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo.
Ndidzachita nanu pangano losatha,
    chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu,
    kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa,
    ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu.
Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu,
    Woyerayo wa Israeli,
    wakuvekani ulemerero.”

Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka.
    Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa,
    ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa.
Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo,
    ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.

“Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu,
    ngakhale njira zanu si njira zanga,”
            akutero Yehova.
“Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi,
    momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu,
    ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
10 Monga mvula ndi chisanu chowundana
    zimatsika kuchokera kumwamba,
ndipo sizibwerera komweko
    koma zimathirira dziko lapansi.
Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera
    kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
11 Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga.
    Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake,
koma adzachita zonse zimene ndifuna,
    ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
12 Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe
    ndipo adzakutsogolerani mwamtendere;
mapiri ndi zitunda
    zidzakuyimbirani nyimbo,
ndipo mitengo yonse yamʼthengo
    idzakuwombereni mʼmanja.
13 Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini,
    ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu.
Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova,
    ngati chizindikiro chamuyaya,
    chimene sichidzafafanizika konse.”

Invitation to the Thirsty

55 “Come, all you who are thirsty,(A)
    come to the waters;(B)
and you who have no money,
    come, buy(C) and eat!
Come, buy wine and milk(D)
    without money and without cost.(E)
Why spend money on what is not bread,
    and your labor on what does not satisfy?(F)
Listen, listen to me, and eat what is good,(G)
    and you will delight in the richest(H) of fare.
Give ear and come to me;
    listen,(I) that you may live.(J)
I will make an everlasting covenant(K) with you,
    my faithful love(L) promised to David.(M)
See, I have made him a witness(N) to the peoples,
    a ruler and commander(O) of the peoples.
Surely you will summon nations(P) you know not,
    and nations you do not know will come running to you,(Q)
because of the Lord your God,
    the Holy One(R) of Israel,
    for he has endowed you with splendor.”(S)

Seek(T) the Lord while he may be found;(U)
    call(V) on him while he is near.
Let the wicked forsake(W) their ways
    and the unrighteous their thoughts.(X)
Let them turn(Y) to the Lord, and he will have mercy(Z) on them,
    and to our God, for he will freely pardon.(AA)

“For my thoughts(AB) are not your thoughts,
    neither are your ways my ways,”(AC)
declares the Lord.
“As the heavens are higher than the earth,(AD)
    so are my ways higher than your ways
    and my thoughts than your thoughts.(AE)
10 As the rain(AF) and the snow
    come down from heaven,
and do not return to it
    without watering the earth
and making it bud and flourish,(AG)
    so that it yields seed(AH) for the sower and bread for the eater,(AI)
11 so is my word(AJ) that goes out from my mouth:
    It will not return to me empty,(AK)
but will accomplish what I desire
    and achieve the purpose(AL) for which I sent it.
12 You will go out in joy(AM)
    and be led forth in peace;(AN)
the mountains and hills
    will burst into song(AO) before you,
and all the trees(AP) of the field
    will clap their hands.(AQ)
13 Instead of the thornbush will grow the juniper,
    and instead of briers(AR) the myrtle(AS) will grow.
This will be for the Lord’s renown,(AT)
    for an everlasting sign,
    that will endure forever.”