Add parallel Print Page Options

Madengu Awiri a Nkhuyu

24 Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda pamodzi ndi nduna zake, anthu aluso ndi akatswiri a ku Yuda ndi kupita nawo ku Babuloni. Pambuyo pake Yehova anandionetsa madengu awiri a nkhuyu atayikidwa pa khomo pa Nyumba ya Yehova. Mʼdengu limodzi munali nkhuyu zabwino kwambiri, ngati nkhuyu zoyambirira kucha. Mʼdengu linalo munali nkhuyu zoyipa kwambiri zosati nʼkudya.

Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?”

Ndinayankha kuti, “Ndikuona nkhuyu zabwino kwambiri ndi nkhuyu zoyipa zosati nʼkudya.”

Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Anthu a ku Yuda amene ndinawachotsa ku malo ano nʼkupita nawo ku ukapolo ku dziko la Ababuloni ndikuwafanizira ndi nkhuyu zabwinozi. Ndidzaonetsesa kuti ndiwachitire zabwino ndipo ndidzabwera nawonso ku dziko lino. Ndidzawamanga osati kuwapasula; ndidzawadzala osati kuwazula. Ndidzawapatsa mtima woti andidziwe kuti ndine Yehova. Adzakhala anthu anga ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, chifukwa adzabwerera kwa Ine ndi mtima wawo wonse.

“ ‘Koma monga nkhuyu zoyipa zija, zomwe ndi zoyipa kwambiri zosati nʼkudya,’ Yehova akuti, ‘ndi mmene ndidzalangire Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi otsala a mu Yerusalemu, kaya adzakhala ali mʼdziko muno kapena mʼdziko la Igupto. Ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa maufumu onse a dziko lapansi, chinthu chonyozeka ndi chopandapake, chinthu chochitidwa chipongwe ndi chotembereredwa kulikonse kumene ndidzawabalalitsira. 10 Ndidzawatumizira nkhondo, njala ndi mliri mpaka atawonongedwa mʼdziko limene ndinawapatsa iwo ndi makolo awo.’ ”

Two Baskets of Figs

24 After Jehoiachin[a](A) son of Jehoiakim king of Judah and the officials, the skilled workers and the artisans of Judah were carried into exile from Jerusalem to Babylon by Nebuchadnezzar king of Babylon, the Lord showed me two baskets of figs(B) placed in front of the temple of the Lord. One basket had very good figs, like those that ripen early;(C) the other basket had very bad(D) figs, so bad they could not be eaten.

Then the Lord asked me, “What do you see,(E) Jeremiah?”

“Figs,” I answered. “The good ones are very good, but the bad ones are so bad they cannot be eaten.”

Then the word of the Lord came to me: “This is what the Lord, the God of Israel, says: ‘Like these good figs, I regard as good the exiles from Judah, whom I sent(F) away from this place to the land of the Babylonians.[b] My eyes will watch over them for their good, and I will bring them back(G) to this land. I will build(H) them up and not tear them down; I will plant(I) them and not uproot them. I will give them a heart to know(J) me, that I am the Lord. They will be my people,(K) and I will be their God, for they will return(L) to me with all their heart.(M)

“‘But like the bad(N) figs, which are so bad they cannot be eaten,’ says the Lord, ‘so will I deal with Zedekiah(O) king of Judah, his officials(P) and the survivors(Q) from Jerusalem, whether they remain in this land or live in Egypt.(R) I will make them abhorrent(S) and an offense to all the kingdoms of the earth, a reproach and a byword,(T) a curse[c](U) and an object of ridicule, wherever I banish(V) them. 10 I will send the sword,(W) famine(X) and plague(Y) against them until they are destroyed from the land I gave to them and their ancestors.(Z)’”

Footnotes

  1. Jeremiah 24:1 Hebrew Jeconiah, a variant of Jehoiachin
  2. Jeremiah 24:5 Or Chaldeans
  3. Jeremiah 24:9 That is, their names will be used in cursing (see 29:22); or, others will see that they are cursed.