2 Samueli 7
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Lonjezo la Mulungu kwa Davide
7 Mfumu itakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, Yehova atayipatsa mpumulo kwa adani ake onse woyizungulira, 2 mfumuyo inawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Mulungu lili mu tenti.”
3 Natani anayankha mfumu kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu chifukwa Yehova ali nanu.”
4 Usiku umenewo mawu a Yehova anafika kwa Natani ndipo anati,
5 “Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti: kodi ndiwe amene udzandimangira Ine nyumba yokhalamo? 6 Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda uku ndi uku ndipo mokhala mwanga munali mu tenti. 7 Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense atsogoleri awo, amene ndinamulamula kuweta anthu anga Aisraeli kuti, nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’ ”
8 “Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli. 9 Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi. 10 Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja, 11 monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzakupatsaninso mpumulo kwa adani anu onse.
“ ‘Yehova akulengeza kwa iwe kuti Iye mwini adzakhazikitsa banja lako: 12 Masiku ako akadzatha ndipo ukadzakapuma ndi makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, imene idzachokera mʼthupi mwako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake. 13 Iye ndiye amene adzamangire nyumba Dzina langa, ndipo Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya. 14 Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Akadzachita choyipa, Ineyo ndidzamulanga ndi ndodo ndi zikwapu za anthu. 15 Koma sindidzasiya kumukonda, monga ndinachitira ndi Sauli, amene ndinamuchotsa iwe usanakhale mfumu. 16 Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhala zamuyaya pamaso panga. Mpando wako waufumu udzakhazikika kwamuyaya!’ ”
17 Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
Pemphero la Davide
18 Choncho Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati:
“Inu Yehova Wamphamvuzonse, ine ndine yani, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?” 19 Ndipo kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Kodi umu ndi mmene mumachitira ndi munthu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse?
20 Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu? Pakuti Inu Ambuye Wamphamvuzonse mukumudziwa mtumiki wanu. 21 Chifukwa cha mawu anu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwachiwulula kwa mtumiki wanu.
22 Inu ndinu wamkulu, Yehova Wamphamvuzonse! Palibe wina wofanana nanu, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha, monga tamvera ndi makutu athu. 23 Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina ndi milungu yawo pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto? 24 Inu mwawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
25 “Ndipo tsopano Yehova Mulungu, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake. Chitani monga mwalonjezera, 26 kotero dzina lanu lidzakhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
27 “Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, mwaululira mtumiki wanu ponena kuti, ‘Ine ndidzakumangira iwe nyumba!’ Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere. 28 Inu Ambuye Wamphamvuzonse, ndinu Mulungu! Mawu anu ndi odalirika, ndipo mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu. 29 Ndipo tsopano chikukomereni kudalitsa banja la mtumiki wanu, kuti likhale mpaka muyaya pamaso panu. Pakuti Inu, Yehova Wamphamvuzonse, mwayankhula, ndipo ndi mʼdalitso wanu banja la mtumiki wanu lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”
2 Samuel 7
New International Version
God’s Promise to David(A)
7 After the king was settled in his palace(B) and the Lord had given him rest from all his enemies(C) around him,(D) 2 he said to Nathan(E) the prophet, “Here I am, living in a house(F) of cedar, while the ark of God remains in a tent.”(G)
3 Nathan replied to the king, “Whatever you have in mind,(H) go ahead and do it, for the Lord is with you.”
4 But that night the word of the Lord came to Nathan, saying:
5 “Go and tell my servant David, ‘This is what the Lord says: Are you(I) the one to build me a house to dwell in?(J) 6 I have not dwelt in a house from the day I brought the Israelites up out of Egypt to this day.(K) I have been moving from place to place with a tent(L) as my dwelling.(M) 7 Wherever I have moved with all the Israelites,(N) did I ever say to any of their rulers whom I commanded to shepherd(O) my people Israel, “Why have you not built me a house(P) of cedar?(Q)”’
8 “Now then, tell my servant David, ‘This is what the Lord Almighty says: I took you from the pasture, from tending the flock,(R) and appointed you ruler(S) over my people Israel.(T) 9 I have been with you wherever you have gone,(U) and I have cut off all your enemies from before you.(V) Now I will make your name great, like the names of the greatest men on earth.(W) 10 And I will provide a place for my people Israel and will plant(X) them so that they can have a home of their own and no longer be disturbed.(Y) Wicked(Z) people will not oppress them anymore,(AA) as they did at the beginning 11 and have done ever since the time I appointed leaders[a](AB) over my people Israel. I will also give you rest from all your enemies.(AC)
“‘The Lord declares(AD) to you that the Lord himself will establish(AE) a house(AF) for you: 12 When your days are over and you rest(AG) with your ancestors, I will raise up your offspring to succeed you, your own flesh and blood,(AH) and I will establish his kingdom.(AI) 13 He is the one who will build a house(AJ) for my Name,(AK) and I will establish the throne of his kingdom forever.(AL) 14 I will be his father, and he will be my son.(AM) When he does wrong, I will punish him(AN) with a rod(AO) wielded by men, with floggings inflicted by human hands. 15 But my love will never be taken away from him,(AP) as I took it away from Saul,(AQ) whom I removed from before you. 16 Your house and your kingdom will endure forever before me[b]; your throne(AR) will be established(AS) forever.(AT)’”
17 Nathan reported to David all the words of this entire revelation.
David’s Prayer(AU)
18 Then King David went in and sat before the Lord, and he said:
“Who am I,(AV) Sovereign Lord, and what is my family, that you have brought me this far? 19 And as if this were not enough in your sight, Sovereign Lord, you have also spoken about the future of the house of your servant—and this decree,(AW) Sovereign Lord, is for a mere human![c]
20 “What more can David say(AX) to you? For you know(AY) your servant,(AZ) Sovereign Lord. 21 For the sake of your word and according to your will, you have done this great thing and made it known to your servant.
22 “How great(BA) you are,(BB) Sovereign Lord! There is no one like(BC) you, and there is no God(BD) but you, as we have heard with our own ears.(BE) 23 And who is like your people Israel(BF)—the one nation on earth that God went out to redeem as a people for himself, and to make a name(BG) for himself, and to perform great and awesome wonders(BH) by driving out nations and their gods from before your people, whom you redeemed(BI) from Egypt?[d] 24 You have established your people Israel as your very own(BJ) forever, and you, Lord, have become their God.(BK)
25 “And now, Lord God, keep forever the promise(BL) you have made concerning your servant and his house. Do as you promised, 26 so that your name(BM) will be great forever. Then people will say, ‘The Lord Almighty is God over Israel!’ And the house of your servant David will be established(BN) in your sight.
27 “Lord Almighty, God of Israel, you have revealed this to your servant, saying, ‘I will build a house for you.’ So your servant has found courage to pray this prayer to you. 28 Sovereign Lord, you are God! Your covenant is trustworthy,(BO) and you have promised these good things to your servant. 29 Now be pleased to bless the house of your servant, that it may continue forever in your sight; for you, Sovereign Lord, have spoken, and with your blessing(BP) the house of your servant will be blessed forever.”
Footnotes
- 2 Samuel 7:11 Traditionally judges
- 2 Samuel 7:16 Some Hebrew manuscripts and Septuagint; most Hebrew manuscripts you
- 2 Samuel 7:19 Or for the human race
- 2 Samuel 7:23 See Septuagint and 1 Chron. 17:21; Hebrew wonders for your land and before your people, whom you redeemed from Egypt, from the nations and their gods.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.