Add parallel Print Page Options

10 Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo,
    kwa iwo amene amalemba zongovutitsa anzawo,
kuwalanda anthu osauka ufulu wawo
    ndi kumana chilungamo osautsidwa pakati pa anthu anga,
amalanda zinthu za akazi amasiye
    ndi kubera ana amasiye.
Kodi mudzatani pa tsiku la chilango,
    pofika chiwonongeko chochokera kutali?
Kodi mudzathawira kwa yani kuti akuthandizeni?
    Nanga chuma chanu mudzachisiya kuti?
Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa
    kapena kufa pamodzi ndi ophedwa.
Komabe pa zonsezi mkwiyo wake sunawachokere,
    mkono wake uli chitambasulire.

Chiweruzo cha Mulungu pa Asiriya

“Tsoka kwa mfumu ya ku Asiriya, chikwapu cha mkwiyo wanga,
    iye ndiye ndodo ya mkwiyo wanga!
Ndidzamutuma kukalimbana ndi mtundu wosapembedza Mulungu,
    ndidzamutumiza kukalimbana ndi anthu amene amandikwiyitsa Ine,
kukafunkha ndi kulanda chuma,
    ndi kuwapondereza pansi ngati matope a mʼmisewu.
Koma izi si zimene akufuna kukachita,
    izi si zimene zili mʼmaganizo mwake;
cholinga chake ndi kukawononga,
    kukapulula mitundu yambiri ya anthu.
Iye akuti, ‘Kodi atsogoleri anga ankhondo si mafumu okhaokha?’
    ‘Kodi Kalino sanagonjetsedwe monga Karikemesi?
Kodi Hamati sali ngati Aripadi,
    nanga Samariya sali ngati Damasiko?
10 Dzanja langa linakantha maufumu a anthu opembedza mafano,
    mafumu amene mafano awo ndi aakulu kupambana Yerusalemu ndi Samariya;
11 nanga Ine nʼkulephera kodi kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake
    monga ndinakanthira Samariya pamodzi ndi mafano ake?’ ”

12 Ambuye akadzamaliza ntchito yonse yolanga phiri la Ziyoni ndi Yerusalemu adzalanganso mfumu ya ku Asiriya chifukwa cha kudzitama ndi kunyada kwake. 13 Pakuti mfumuyo ikuti,

“ ‘Ndachita zimenezi ndi dzanja langa,
    ndiponso ndi nzeru zanga, chifukwa ndine wozindikira zinthu.
Ndinachotsa malire a mitundu ya anthu,
    ndinafunkha chuma chawo;
    ndinagonjetsa mafumu awo monga munthu wamphamvu.
14 Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu
    ngati momwe munthu amagwirira chisa cha mbalame,
ngati momwe anthu amatolera mazira osiyidwa,
    motero inenso ndinasonkhanitsa mayiko onse;
palibe mbalame imene inakupiza mapiko ake,
    kapena kuyasama kukamwa kuti ilire.’ ”

15 Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana woyigwiritsa ntchito,
    kapena macheka angathe kudzikuza kupambana wowagwiritsa ntchito?
Ndiye kukhala ngati kuti chikwapu chikuzunguza munthu amene wachinyamula,
    kapena ngati kuti ndodo ikuopseza amene wayinyamula!
16 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvuzonse
    adzatumiza matenda owondetsa kwa ankhondo amphamvu;
kunyada kwa mfumuyo kudzapsa
    ndi moto wosazima.
17 Mulungu, Kuwala kwa Israeli, adzakhala ngati moto,
    Woyera uja wa Israeli adzakhala ngati malawi a moto.
Motowo udzawatentha ndi kuwapsereza
    ngati minga ndi mkandankhuku pa tsiku limodzi.
18 Ankhondo ake adzawonongedwa
    ngati nkhalango yayikulu
    ndi ngati nthaka yachonde.
19 Mitengo yotsalira ya mʼnkhalango zake idzakhala yochepa kwambiri,
    yoti ndi mwana yemwe ndi kuyiwerenga.

Aisraeli Otsala

20 Tsiku limenelo otsalira a ku Israeli,
    opulumuka a nyumba ya Yakobo,
sadzadaliranso anthu
    amene anawakantha,
koma adzadalira Yehova,
    Woyerayo wa Israeli.
21 Otsalira adzabwerera, otsalira a Yakobo
    adzabwerera kwa Mulungu Wamphamvu.
22 Iwe Israeli, ngakhale anthu ako achuluke ngati mchenga wa ku nyanja,
    otsala okha ndiwo adzabwerere.
Chiwonongeko chalamulidwa,
    chidzaonetsa chilungamo chosefukira.
23 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzawononga ndithu dziko lonse
    monga momwe analamulira.

24 Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti,

“Inu anthu anga okhala mu Ziyoni,
    musawaope Asiriya,
amene amakukanthani ndi ndodo
    nakumenyani ndi zibonga monga mmene Igupto anachitira.
25 Patsala pangʼonongʼono kuti mkwiyo wanga uchoke pa inu
    ndipo ndidzaonetsa ukali wanga pa iwo mpaka kuwawononga.”

26 Yehova Wamphamvuzonse adzawakwapula ndi chikwapu,
    monga momwe anakwapulira Amidiyani ku thanthwe la Orebu;
ndipo adzatukula ndodo yake pa madzi
    ndikuwalanga monga analangira Igupto pa nyanja.
27 Tsiku limenelo katundu wawo adzachotsedwa pa mapewa anu,
    goli lawo lidzachoka mʼkhosi mwanu;
golilo lidzathyoka
    chifukwa cha kunenepa kwambiri.

28 Adani alowa mu Ayati
    apyola ku Migironi;
    asunga katundu wawo ku Mikimasi.
29 Adutsa pa mpata uja, ndipo akuti,
    “Tikagona ku Geba”
Rama akunjenjemera;
    Gibeya, mzinda wa Saulo ukuthawa.
30 Lilani mokweza, inu anthu a ku Galimu!
    Tchera khutu, iwe Laisa!
    Iwe Anatoti wosauka!
31 Anthu a ku Madimena akuthawa;
    anthu a ku Gebimu bisalani.
32 Lero lomwe lino adaniwo adzayima ku Nobu;
    adzagwedeza mikono yawo,
kuopseza anthu a ku Ziyoni,
    pa phiri la Yerusalemu.

33 Taonani, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse,
    adzadula mwamphamvu nthambi za mitengo,
mitengo yodzikweza idzadulidwa,
    mitengo yayitali idzagwetsedwa.
34 Yehova adzadula ndi nkhwangwa mitengo ya mʼnkhalango yowirira;
    Lebanoni adzagwa pamaso pa Wamphamvu.

10 Woe(A) to those who make unjust laws,
    to those who issue oppressive decrees,(B)
to deprive(C) the poor of their rights
    and withhold justice from the oppressed of my people,(D)
making widows their prey
    and robbing the fatherless.(E)
What will you do on the day of reckoning,(F)
    when disaster(G) comes from afar?
To whom will you run for help?(H)
    Where will you leave your riches?
Nothing will remain but to cringe among the captives(I)
    or fall among the slain.(J)

Yet for all this, his anger is not turned away,(K)
    his hand is still upraised.

God’s Judgment on Assyria

“Woe(L) to the Assyrian,(M) the rod(N) of my anger,
    in whose hand is the club(O) of my wrath!(P)
I send him against a godless(Q) nation,
    I dispatch(R) him against a people who anger me,(S)
to seize loot and snatch plunder,(T)
    and to trample(U) them down like mud in the streets.
But this is not what he intends,(V)
    this is not what he has in mind;
his purpose is to destroy,
    to put an end to many nations.
‘Are not my commanders(W) all kings?’ he says.
    ‘Has not Kalno(X) fared like Carchemish?(Y)
Is not Hamath(Z) like Arpad,(AA)
    and Samaria(AB) like Damascus?(AC)
10 As my hand seized the kingdoms of the idols,(AD)
    kingdoms whose images excelled those of Jerusalem and Samaria—
11 shall I not deal with Jerusalem and her images
    as I dealt with Samaria and her idols?(AE)’”

12 When the Lord has finished all his work(AF) against Mount Zion(AG) and Jerusalem, he will say, “I will punish the king of Assyria(AH) for the willful pride(AI) of his heart and the haughty look(AJ) in his eyes. 13 For he says:

“‘By the strength of my hand(AK) I have done this,(AL)
    and by my wisdom, because I have understanding.
I removed the boundaries of nations,
    I plundered their treasures;(AM)
    like a mighty one I subdued[a] their kings.(AN)
14 As one reaches into a nest,(AO)
    so my hand reached for the wealth(AP) of the nations;
as people gather abandoned eggs,
    so I gathered all the countries;(AQ)
not one flapped a wing,
    or opened its mouth to chirp.(AR)’”

15 Does the ax raise itself above the person who swings it,
    or the saw boast against the one who uses it?(AS)
As if a rod were to wield the person who lifts it up,
    or a club(AT) brandish the one who is not wood!
16 Therefore, the Lord, the Lord Almighty,
    will send a wasting disease(AU) upon his sturdy warriors;(AV)
under his pomp(AW) a fire(AX) will be kindled
    like a blazing flame.
17 The Light of Israel will become a fire,(AY)
    their Holy One(AZ) a flame;
in a single day it will burn and consume
    his thorns(BA) and his briers.(BB)
18 The splendor of his forests(BC) and fertile fields
    it will completely destroy,(BD)
    as when a sick person wastes away.
19 And the remaining trees of his forests(BE) will be so few(BF)
    that a child could write them down.

The Remnant of Israel

20 In that day(BG) the remnant of Israel,
    the survivors(BH) of Jacob,
will no longer rely(BI) on him
    who struck them down(BJ)
but will truly rely(BK) on the Lord,
    the Holy One of Israel.(BL)
21 A remnant(BM) will return,[b](BN) a remnant of Jacob
    will return to the Mighty God.(BO)
22 Though your people be like the sand(BP) by the sea, Israel,
    only a remnant will return.(BQ)
Destruction has been decreed,(BR)
    overwhelming and righteous.
23 The Lord, the Lord Almighty, will carry out
    the destruction decreed(BS) upon the whole land.(BT)

24 Therefore this is what the Lord, the Lord Almighty, says:

“My people who live in Zion,(BU)
    do not be afraid(BV) of the Assyrians,
who beat(BW) you with a rod(BX)
    and lift up a club against you, as Egypt did.
25 Very soon(BY) my anger against you will end
    and my wrath(BZ) will be directed to their destruction.(CA)

26 The Lord Almighty will lash(CB) them with a whip,
    as when he struck down Midian(CC) at the rock of Oreb;
and he will raise his staff(CD) over the waters,(CE)
    as he did in Egypt.
27 In that day(CF) their burden(CG) will be lifted from your shoulders,
    their yoke(CH) from your neck;(CI)
the yoke(CJ) will be broken
    because you have grown so fat.[c]

28 They enter Aiath;
    they pass through Migron;(CK)
    they store supplies(CL) at Mikmash.(CM)
29 They go over the pass, and say,
    “We will camp overnight at Geba.(CN)
Ramah(CO) trembles;
    Gibeah(CP) of Saul flees.(CQ)
30 Cry out, Daughter Gallim!(CR)
    Listen, Laishah!
    Poor Anathoth!(CS)
31 Madmenah is in flight;
    the people of Gebim take cover.
32 This day they will halt at Nob;(CT)
    they will shake their fist(CU)
at the mount of Daughter Zion,(CV)
    at the hill of Jerusalem.

33 See, the Lord, the Lord Almighty,
    will lop off(CW) the boughs with great power.
The lofty trees will be felled,(CX)
    the tall(CY) ones will be brought low.(CZ)
34 He will cut down(DA) the forest thickets with an ax;
    Lebanon(DB) will fall before the Mighty One.(DC)

Footnotes

  1. Isaiah 10:13 Or treasures; / I subdued the mighty,
  2. Isaiah 10:21 Hebrew shear-jashub (see 7:3 and note); also in verse 22
  3. Isaiah 10:27 Hebrew; Septuagint broken / from your shoulders